Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yeremiya 1-2

Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini. Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda. Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.

Kuyitanidwa kwa Yeremiya

Yehova anayankhula nane kuti,

“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale,
    iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale;
    ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”

Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”

Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira. Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako. 10 Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”

11 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”

12 Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”

13 Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”

14 Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto. 15 Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova.

“Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu
    polowera pa zipata za Yerusalemu;
iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake
    ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo
    chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine.
Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina,
    ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.

17 “Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona. 18 Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo. 19 Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

Aisraeli Asiya Mulungu

Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti,

“ ‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako,
    mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi,
mmene unkanditsata mʼchipululu muja;
    mʼdziko losadzalamo kanthu.
Israeli anali wopatulika wa Yehova,
    anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola;
onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa
    ndipo mavuto anawagwera,’ ”
            akutero Yehova.

Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo,
    inu mafuko onse a Israeli.

Yehova akuti,

“Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji,
    kuti andithawe?
Iwo anatsata milungu yachabechabe,
    nawonso nʼkusanduka achabechabe.
Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti,
    amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto
natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma
    ndi lokumbikakumbika,
mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima,
    dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
Ndinakufikitsani ku dziko lachonde
    kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina.
Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa
    ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
Ansembe nawonso sanafunse kuti,
    ‘Yehova ali kuti?’
Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe;
    atsogoleri anandiwukira.
Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala,
    ndi kutsatira mafano achabechabe.

“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,”
            akutero Yehova.
    “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
10 Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone,
    tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino;
    ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
11 Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake?
    (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe).
Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero
    ndi mafano achabechabe.
12 Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi,
    ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,”
            akutero Yehova.
13 “Popeza anthu anga achita machimo awiri:
Andisiya Ine
    kasupe wa madzi a moyo,
ndi kukadzikumbira zitsime zawo,
    zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
14 Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi.
    Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
15 Adani ake abangulira
    ndi kumuopseza ngati mikango.
Dziko lake analisandutsa bwinja;
    mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
16 Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi
    akuphwanyani mitu.
17 Zimenezitu zakuchitikirani
    chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu
    pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
18 Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto,
    kukamwa madzi a mu Sihori?
Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya,
    kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
19 Kuyipa kwanuko kudzakulangani;
    kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani.
Tsono ganizirani bwino,
    popeza ndi chinthu choyipa
kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu;
    ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu.
            Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.

20 “Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu
    ndi kudula msinga zanu;
    munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’
Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere.
    Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali
    ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
21 Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika;
    unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika.
Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa
    wachabechabe wonga wa kutchire?
22 Ngakhale utasamba ndi soda
    kapena kusambira sopo wambiri,
    kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,”
            akutero Ambuye Yehova.
23 “Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse;
    sindinatsatire Abaala’?
Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja;
    zindikira bwino zomwe wachita.
Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro
    yomangothamanga uku ndi uku,
24 wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu,
    yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika.
    Ndani angayiretse chilakolako chakecho?
Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika.
    Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
25 Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi
    ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu.
Koma unati, ‘Zamkutu!
    Ine ndimakonda milungu yachilendo,
    ndipo ndidzayitsatira.’

26 “Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa,
    moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi;
Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo,
    ansembe ndi aneneri awo.
27 Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’
    ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’
Iwo andifulatira Ine,
    ndipo safuna kundiyangʼana;
Koma akakhala pa mavuto amati,
    ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
28 Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha?
    Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani
    pamene muli pamavuto!
Inu anthu a ku Yuda,
    milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.

29 “Kodi mukundizengeranji mlandu?
    Nonse mwandiwukira,”
            akutero Yehova.
30 “Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu;
    iwo sanaphunzirepo kanthu.
Monga mkango wolusa,
    lupanga lanu lapha aneneri anu.

31 “Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova:

“Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli
    kapena ngati dziko la mdima wandiweyani?
Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda;
    sitidzabweranso kwa Inu’?
32 Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake,
    kapena kuyiwala zovala zake za ukwati?
Komatu anthu anga andiyiwala
    masiku osawerengeka.
33 Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi!
    Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
34 Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo
    magazi a anthu osauka osalakwa.
    Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba.
Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
35     inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa,
    sadzatikwiyira.’
Ndidzakuyimbani mlandu
    chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
36 Chifukwa chiyani
    mukunkabe nimusinthasintha njira zanu?
Aigupto adzakukhumudwitsani
    monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
37 Mudzachokanso kumeneko
    manja ali kunkhongo.
Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira,
    choncho sadzakuthandizani konse.

1 Timoteyo 3

Zowayenereza Oyangʼanira ndi Atumiki

Mawu woona ndi awa: Ngati munthu akufunitsitsa atakhala woyangʼanira, ndiye kuti akufuna ntchito yabwino. Tsono woyangʼanira ayenera kukhala munthu wopanda chotsutsika nacho, mwamuna wa mkazi mmodzi yekha, woganiza bwino, wodziretsa, waulemu, wosamala bwino alendo, wodziwa kuphunzitsa. Asakhale chidakwa, asakhale wandewu, koma wofatsa, asakhale wokonda mikangano, kapena wokonda ndalama. Akhale wodziwa kusamala bwino banja lake ndi kulera ana ake bwino, kuti akhale omvera ndi aulemu weniweni. (Ngati munthu sadziwa kusamala banja lake lomwe, angathe bwanji kusamala mpingo wa Mulungu?) Asakhale wongotembenuka mtima kumene kuopa kuti angadzitukumule napezeka pa chilango monga Satana. Ayeneranso kukhala munthu wambiri yabwino ndi akunja, kuti anthu asamutonze nagwa mu msampha wa Satana.

Momwemonso atumiki, akhale anthu oyenera ulemu, woona mtima, osakhala okonda zoledzeretsa, osakonda kupeza zinthu mwachinyengo. Ayenera kugwiritsa mozama choonadi cha chikhulupiriro ndi kukhala ndi chikumbumtima chabwino. 10 Ayambe ayesedwa kaye, ndipo ngati palibe kanthu kowatsutsa, aloleni akhale atumiki.

11 Momwemonso, akazi akhale olemekezeka, osasinjirira koma oganiza bwino ndi odalirika pa chilichonse.

12 Mtumiki akhale wokhulupirika kwa mkazi wake ndipo ayenera kukhala wosamalira bwino ana ake ndi onse a pa khomo pake. 13 Iwo amene atumikira bwino amakhala ndi mbiri yabwino ndipo amakhala chitsimikizo chachikulu cha chikhulupiriro chawo mwa Khristu Yesu.

Cholinga cha Malangizo a Paulo

14 Ngakhale ndili ndi chiyembekezo choti ndifika komweko posachedwapa, ndikukulemberani malangizo awa. 15 Ine zina zikandichedwetsa kubwera, mudziwe za mmene anthu ayenera kukhalira mʼNyumba ya Mulungu, imene ndi mpingo wa Mulungu wamoyo, mzati ndi maziko achoonadi. 16 Mosakayikira, chinsinsi cha chikhulupiriro chathu chachikulu:

Khristu anaonekera ali ndi thupi la munthu,
    Mzimu anamuchitira umboni,
angelo anamuona,
    analalikidwa pakati pa mitundu yonse,
dziko lapansi linamukhulupirira,
    anatengedwa kupita kumwamba mwa ulemerero.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.