Old/New Testament
Ndakatulo ya Asafu.
74 Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu?
Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
2 Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale,
fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola,
phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
3 Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya
chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
4 Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe;
anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
5 Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo
kuti adule mitengo mʼnkhalango.
6 Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo
zonse zimene tinapachika.
7 Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi;
anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
8 Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.”
Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
9 Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa;
palibe aneneri amene atsala
ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu?
Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja?
Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale;
Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu;
munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani
ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje,
munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso;
Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi;
munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova,
momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo;
nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko
asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi;
osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu;
kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu,
chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo.
75 Tikuthokoza Inu Mulungu,
tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe,
anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera,
ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera,
ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba.
Sela
4 Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’
ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba;
musayankhule ndi khosi losololoka.’ ”
6 Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo
kapena ku chipululu.
7 Koma ndi Mulungu amene amaweruza:
Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 Mʼdzanja la Yehova muli chikho
chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera;
Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi
amamwa ndi senga zake zonse.
9 Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya;
ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa
koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu.
76 Mulungu amadziwika mu Yuda;
dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 Tenti yake ili mu Salemu,
malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka,
zishango ndi malupanga, zida zankhondo.
Sela
4 Wolemekezeka ndinu,
wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma,
Iwowo amagona tulo tawo totsiriza;
palibe mmodzi wamphamvu
amene angatukule manja ake.
6 Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo,
kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa.
Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo,
ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze,
kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko.
Sela
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando
ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse;
anthu onse omuzungulira abweretse mphatso
kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira;
amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.
16 Nʼchifukwa chake, izi sizitengera zokhumba za munthu kapena kuyesetsa koma chifundo cha Mulungu. 17 Malemba akuti Mulungu anamuwuza Farao kuti, “Ine ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga, kuti mwa iwe dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.” 18 Choncho Mulungu amachitira chifundo munthu amene akufuna kumuchitira chifundo ndipo amawumitsa mtima munthu amene Iye akufuna kumuwumitsa mtima.
19 Tsono mmodzi wa inu nʼkundifunsa kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mulungu amatipeza olakwa? Nanga ndani amene amakana chifuniro chake?” 20 Koma ndiwe yani, munthu wamba, woti nʼkutsutsana ndi Mulungu? “Kodi chimene chinawumbidwa nʼkufunsa amene anachiwumba kuti, ‘Kodi unandiwumbiranji motere?’ ” 21 Kodi wowumba alibe ufulu wowumba kuchokera ku dothi lomwelo mbiya yamtengowapatali ndi ina yamtengo wotsika?
22 Koma Mulungu, anafuna kuonetsa mkwiyo wake ndi kuti mphamvu yake idziwike. Iye anapirira modekha mtima kwambiri zochita za anthu omwe anawakwiyirawo amene anayeneradi chiwonongeko. 23 Iye anachita izi kufuna kuonetsa kulemera kwa ulemerero wake ndi kuti udziwike kwa amene analandira chifundo chake. Iye anawakonzeratu kuti alandire ulemerero wake 24 ngakhale ifenso amene anatiyitana osati kuchokera kwa Ayuda okha komanso kwa a mitundu ina. 25 Monga momwe Mulungu akunenera mʼbuku la Hoseya kuti,
“Amene sanali anthu anga ndidzawatcha ‘anthu anga;’
ndipo Ine ndidzatcha ‘wokondedwa wanga’ amene sali wokondedwa wanga,”
26 ndipo,
“Pamalo omwewo pamene ananena kuti,
‘Sindinu anthu anga,’
pomweponso adzawatchula kuti, ‘Ana a Mulungu wamoyo.’ ”
27 Yesaya anafuwula za Aisraeli kuti,
“Ngakhale chiwerengero cha Aisraeli chingakhale ngati mchenga wa ku nyanja,
otsala okha ndiye adzapulumuke.
28 Pakuti Ambuye adzagamula milandu
ya anthu pa dziko lapansi mofulumira ndi kumaliziratu.”
29 Monga momwe Yesaya ananena malo ena kuti,
“Ngati Yehova Wamphamvuzonse
akanapanda kutisiyira zidzukulu,
ife tikanawonongeka
ngati anthu a ku Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.”
Kusakhulupirira kwa Aisraeli
30 Kodi nanga tidzati chiyani? Tidzati a mitundu ina amene sanafune chilungamo analandira chilungamo chachikhulupiriro 31 koma Aisraeli, amene anafuna chilungamo cha lamulo sanachilandire. 32 Chifukwa chiyani? Chifukwa iwo sanachifune ndi chikhulupiriro koma ngati mwa ntchito. Iwo anapunthwa pa “Mwala wopunthwitsa.” 33 Monga momwe kwalembedwa kuti,
“Taonani, Ine ndikuyika mwala mu Ziyoni wopunthwitsa anthu,
thanthwe limene limagwetsa anthu.
Koma amene akhulupirira Iye sadzachititsidwa manyazi.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.