Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Amosi 1-3

Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.

Amosi anati:

“Yehova akubangula mu Ziyoni
    ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu;
msipu wa abusa ukulira,
    ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”

Chiweruzo pa Anthu Oyandikana ndi Israeli

Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anapuntha Giliyadi
    ndi zopunthira za mano achitsulo,
Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli
    umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
Ndidzathyola chipata cha Damasiko;
    ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni,
ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni.
    Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,”
            akutero Yehova.

Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu
    ndi kuwugulitsa ku Edomu,
ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza
    umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi
    komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni.
Ndidzalanga Ekroni,
    mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,”
            akutero Ambuye Yehova.

Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu,
    osasunga pangano laubale lija,
10 Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo
    umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”

11 Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,
    popanda nʼchifundo chomwe.
Popeza mkwiyo wake unakulabe
    ndipo ukali wake sunatonthozeke,
12 Ine ndidzatumiza moto pa Temani
    umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”

13 Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi
    nʼcholinga choti akuze malire awo,
14 Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba
    umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo,
    kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
15 Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo,
    iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,”
            akutero Yehova.

Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu,
    mpaka kuwasandutsa phulusa,
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu,
    umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti.
Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa,
    mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
Ndidzawononga wolamulira wake
    ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,”
            akutero Yehova.

Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Popeza iwo akana lamulo la Yehova
    ndipo sanasunge malangizo ake,
popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza,
    milungu imene makolo awo ankayitsatira,
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda,
    umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”

Chilango cha Anthu a ku Israeli

Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva,
    ndi osauka ndi nsapato.
Amapondereza anthu osauka
    ngati akuponda fumbi,
    ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa.
Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo,
    ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe
    pa zovala zimene anatenga ngati chikole.
Mʼnyumba ya mulungu wawo
    amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.

“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo,
    ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza
    ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu.
Ndinawononga zipatso zawo
    ndiponso mizu yawo.

10 “Ine ndinakutulutsani ku Igupto,
    ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi,
    kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri,
    ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri.
Kodi si choncho, inu Aisraeli?”
            akutero Yehova.
12 “Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja,
    ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.

13 “Tsono Ine ndidzakupsinjani
    monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 Munthu waliwiro sadzatha kuthawa,
    munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga,
    wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 Munthu wa uta sadzalimbika,
    msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka,
    ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri
    adzathawa ali maliseche pa tsikulo,”
            akutero Yehova.

Mboni Zotsutsa Israeli

Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:

“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani
    pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;
nʼchifukwa chake ndidzakulangani
    chifukwa cha machimo anu onse.”

Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi
    asanapangane?
Kodi mkango umabangula mʼnkhalango
    usanagwire nyama?
Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake
    pamene sunagwire kanthu?
Kodi mbalame nʼkutera pa msampha
    pamene palibe nyambo yake?
Kodi msampha umafwamphuka
    usanakole kanthu?
Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,
    anthu sanjenjemera?
Pamene tsoka lafika mu mzinda,
    kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?

Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu
    asanawulule zimene akufuna kuchita
    kwa atumiki ake, aneneri.

Mkango wabangula,
    ndani amene sachita mantha?
Ambuye Yehova wayankhula,
    ndani amene sanganenere?

Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi
    ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:
“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;
    onani chisokonezo pakati pake
    ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”

10 “Iwo sadziwa kuchita zolungama,
    ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.

11 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:

“Mdani adzalizungulira dzikoli;
    iye adzagwetsa malinga ako,
    ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”

12 Yehova akuti,

“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango
    miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,
    moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli
amene amakhala mu Samariya
    pa msonga za mabedi awo,
    ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”

13 “Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

14 “Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,
    ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;
nyanga za guwa zidzathyoka
    ndipo zidzagwa pansi.
15 Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira
    pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;
nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa
    ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”
            akutero Yehova.

Chivumbulutso 6

Kutsekulidwa kwa Zimatiro Zisanu ndi Chimodzi

Ndinaona pamene Mwana Wankhosa anatsekula chomatira choyamba cha zomatira zisanu ndi ziwiri zija. Ndipo ndinamva chimodzi mwa zamoyo zinayi zija chikunena liwu lomveka ngati bingu kuti, “Bwera!” Nditayangʼana patsogolo pake ndinaona kavalo woyera! Wokwerapo wake anali ndi uta ndipo anapatsidwa chipewa chaufumu, ndipo anatuluka kupita kukagonjetsa anthu ena.

Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachiwiri, ndinamva chamoyo chachiwiri chija chikuti, “Bwera!” Pamenepo kavalo wina wofiira anatulukira. Wokwerapo wake anapatsidwa mphamvu yochotsa mtendere pa dziko lapansi ndi kuchititsa anthu kuti aziphana wina ndi mnzake. Iyeyu anapatsidwa lupanga lalikulu.

Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachitatu, ndinamva chamoyo chachitatu chikuti, “Bwera!” Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wakuda! Wokwerapo wake anali ndi masikelo awiri mʼmanja mwake. Ndinamva ngati liwu kuchokera pakati pa zamoyo zinayi zija likuti, “Kilogalamu imodzi ya tirigu mtengo ndi malipiro a tsiku limodzi ndipo makilogalamu atatu a barele mtengo wake ndi malipiro a tsiku limodzi koma usawononge mafuta ndi vinyo!”

Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachinayi, ndinamva chamoyo chachinayi chija chikunena kuti, “Bwera!” Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wotuwa! Wokwerapo wake dzina lake linali Imfa ndipo Hade inali kumutsatira pambuyo pake. Anapatsidwa ulamuliro pa gawo limodzi la magawo anayi a dziko lapansi kuti aphe ndi lupanga, njala, mliri, ndi zirombo zakuthengo za mʼdziko lapansi.

Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachisanu, ndinaona kunsi kwa guwa lansembe kunali mizimu ya anthu amene anaphedwa chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi chifukwa chochitira umboni. 10 Iwo anafuwula kuti, “Mudzawaleka mpaka liti, Inu Ambuye wamkulu, woyera ndi woona, osawaweruza anthu okhala mʼdziko lapansi ndi kulipsira magazi athu?” 11 Pamenepo aliyense wa anthuwo anapatsidwa mwinjiro woyera ndipo anawuzidwa kuti adikire pangʼono kufikira chiwerengero cha anzawo ndi abale awo amene anayeneranso kuphedwa ngati iwo, chitakwanira.

12 Ndinayangʼanitsitsa pamene ankatsekula chomatira chachisanu ndi chimodzi. Ndipo panachitika chivomerezi champhamvu. Dzuwa linada ngati chiguduli chopanga ndi bweya wambuzi wakuda. Mwezi wonse unafiira ngati magazi, 13 ndipo nyenyezi zakuthambo zinagwa pa dziko lapansi ngati muja zimagwera nkhuyu zotsalira mu mtengo mphepo yamphamvu ikawomba. 14 Thambo linachoka ngati amayalulira mphasa ndipo phiri lililonse ndi chilumba chilichonse zinachotsedwa pa malo pake.

15 Kenaka, mafumu a pa dziko lapansi, ana a mafumu, atsogoleri a ankhondo, olemera, amphamvu, kapolo aliyense, ndi mfulu aliyense anakabisala kumapanga ndi pakati pa matanthwe a ku mapiri. 16 Iwo anafuwulira mapiri ndi matanthwe kuti, “Tigwereni ndi kutivundikira kuti asatione wokhala pa mpando waufumuyo ndi kupulumuka ku mkwiyo wa Mwana Wankhosa! 17 Pakuti tsiku lalikulu la mkwiyo wawo lafika ndipo ndi ndani angathe kulimbapo?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.