Old/New Testament
Za Moyo wa Uchitsiru
6 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole,
ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena,
wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 Tsono popeza iwe mwana wanga
wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse:
pita msanga ukamupemphe mnansi wako;
kuti akumasule!
4 Usagone tulo,
usawodzere.
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje,
ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe;
kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 Zilibe mfumu,
zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe
ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe?
Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono
ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 umphawi udzakugwira ngati mbala
ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa,
amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 amatsinzinira maso ake,
namakwakwaza mapazi ake
ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo
ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa;
adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo,
zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 maso onyada,
pakamwa pabodza,
manja akupha munthu wosalakwa,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa,
mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza
komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
Chenjezo pa za Chigololo
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako;
ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse,
uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira;
ukugona, zidzakulondera;
ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale,
malangizowa ali ngati kuwunika,
ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo
moyo weniweni,
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama,
zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake,
asakukope ndi zikope zake,
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi
ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto
zovala zake osapsa?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto
mapazi ake osapserera?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina.
Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba
chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri,
ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru.
Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo,
ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa,
ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 Iye savomera dipo lililonse;
sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
Za Mkazi Wachigololo
7 Mwana wanga, mvera mawu anga;
usunge bwino malamulo angawa.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo;
samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako,
ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,”
ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo
ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga
ndinasuzumira pa zenera.
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa,
pakati pa anyamata,
mnyamata wina wopanda nzeru.
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo,
kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 Inali nthawi yachisisira madzulo,
nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye,
atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve,
iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika,
ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona
ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano.
Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe;
ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Pa bedi panga ndayalapo
nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira
za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa;
tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako;
wapita ulendo wautali:
20 Anatenga thumba la ndalama
ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo;
amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo
ngati ngʼombe yopita kukaphedwa,
monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake,
chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe,
osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Tsono ana inu, ndimvereni;
mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu;
musasochere potsata njira zake.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri;
wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda,
yotsikira ku malo a anthu akufa.
2 Kotero ndinatsimikiza maganizo anga kuti ndisachitenso ulendo wina owawa wobwera kwanuko. 2 Pakuti ngati ndikumvetsani chisoni, kodi angandisangalatse ndani, kupatula inuyo amene ndakumvetsani chisoni? 3 Nʼchifukwa chake ndinakulemberani monga ndinachitiramo kuti nditabwera kwanuko ndisadzamve chisoni ndi anthu oyenera kundisangalatsa. Ndinali ndi chikhulupiriro ndi inu nonse kuti inuyo mukakhala ndi chimwemwe poona kuti inenso ndili ndi chimwemwe. 4 Pakuti ndinakulemberani kalata ija ndili wopsinjika ndi wowawidwa mtima kwambiri ndi kutuluka misozi yambiri, osati pofuna kukumvetsani chisoni koma kuti ndikudziwitseni kuti ndimakukondani kwambiri.
Za Kukhululukira Wolakwa
5 Koma ngati wina wamvetsa chisoni, sanamvetse chisoni ine ndekha, koma koposa mosawonjezera wakhumudwitsa nonsenu, kunenatu mosawonjezera. 6 Chilango chimene ambiri a inu mwamupatsa munthu ameneyu nʼchokwanira. 7 Mʼmalo mwake tsono, muyenera kumukhululukira ndi kumulimbikitsa mtima kuti asamve chisoni choposa muyeso, angataye mtima. 8 Choncho ndikukupemphani kuti mutsimikizire chikondi chanu pa iye. 9 Cholinga china chimene ndinakulemberani kalata ija chinali chofuna kukuonani ngati mudzandimvera pa zonse. 10 Aliyense amene mumukhululukire, inenso ndimukhululukira. Ndipo ndikakhululukira, ngati pali kanthu koti ndikhululukire, ndiye kuti ndakhululuka chifukwa cha inu pamaso pa Khristu, 11 kupewa kuti Satana angapezere mpata pa ife, pajatu timadziwa machenjerero ake.
Atumiki a Pangano Latsopano
12 Tsono nditafika ku Trowa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Khristu, nʼkupeza kuti Ambuye anditsekulira khomo, 13 ndinasowa mtendere mu mtima mwanga, chifukwa sindinapezeko mʼbale wanga Tito. Choncho ndinatsanzikana ndi anthu kumeneko nʼkupita ku Makedoniya.
14 Koma tithokoze Mulungu amene amatitsogolera nthawi zonse monga ogwidwa ku nkhondo a Khristu pa chipambano chake. Tsono amatigwiritsa ntchito yofalitsa ponseponse nzeru zodziwira Khristu ngati fungo labwino. 15 Pakuti kwa Mulungu ndife fungo labwino la Khristu pakati pa iwo amene akupulumutsidwa ndi amene akuwonongeka. 16 Kwa amene akuwonongeka ndife fungo la imfa, limawapha. Ndipo kwa amene akupulumuka ndife fungo lamoyo, limawapatsa moyo. Ndani angayithe ntchito yotereyi? 17 Kusiyana ndi ena ambiri, ife sitilalikira Mawu a Mulungu kuti tipeza phindu. Mʼmalo mwake, ife mwa Khristu timayankhula pamaso pa Mulungu moona mtima, monga anthu otumidwa ndi Mulungu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.