M’Cheyne Bible Reading Plan
Mose Adalitsa Mafuko a Aisraeli
33 Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe. 2 Iye anati:
“Yehova anabwera kuchokera ku Sinai
ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri;
anawala kuchokera pa Phiri la Parani.
Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo
kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.
3 Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu;
opatulika ake onse ali mʼmanja mwake.
Onse amagwada pansi pa mapazi anu
kuchokera kwa inu amalandira malangizo,
4 malamulo amene Mose anatipatsa,
chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.
5 Iye anali mfumu ya Yesuruni
pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,
pamodzi ndi mafuko a Israeli.
6 “Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe,
anthu ake asachepe pa chiwerengero.”
7 Ndipo ponena za Yuda anati:
“Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda;
mubweretseni kwa anthu ake.
Ndi manja ake omwe adziteteze yekha.
Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”
8 Za fuko la Alevi anati:
“Tumimu wanu ndi Urimu ndi za
mtumiki wanu wokhulupirika.
Munamuyesa ku Masa;
munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.
9 Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti,
‘Sindilabadira za iwo.’
Sanasamale za abale ake
kapena ana ake,
koma anayangʼanira mawu anu
ndipo anateteza pangano lanu.
10 Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu
ndi malamulo anu kwa Israeli.
Amafukiza lubani pamaso panu
ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.
11 Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse
ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake.
Menyani adani awo mʼchiwuno
kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”
12 Za fuko la Benjamini anati:
“Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye,
pakuti amamuteteza tsiku lonse,
ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”
13 Za fuko la Yosefe anati:
“Yehova adalitse dziko lake
ndi mame ambiri ochokera kumwamba
ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;
14 ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa
ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;
15 ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa
ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;
16 ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo
ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto.
Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe,
wapaderadera pakati pa abale ake.
17 Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa;
nyanga zake zili ngati za njati.
Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina,
ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi.
Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu;
nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”
18 Za fuko la Zebuloni anati:
“Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka,
ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.
19 Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri,
kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo;
kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja,
chuma chobisika mu mchenga.”
20 Za fuko la Gadi anati:
“Wodala amene amakulitsa malire a Gadi!
Gadi amakhala kumeneko ngati mkango,
kukhadzula mkono kapena mutu.
21 Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri;
gawo la mtsogoleri anasungira iye.
Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,
anachita chifuniro cha Yehova molungama,
ndiponso malamulo onena za Israeli.”
22 Za fuko la Dani anati:
“Dani ndi mwana wamkango,
amene akutuluka ku Basani.”
23 Za fuko la Nafutali anati:
“Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova
ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake;
cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”
24 Za fuko la Aseri anati:
“Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri;
abale ake amukomere mtima,
ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.
25 Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa,
ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.
26 “Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni,
amene amakwera pa thambo kukuthandizani
ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.
27 Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu,
ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha.
Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu,
adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’
28 Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere;
zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere
mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano,
kumene thambo limagwetsa mame.
29 Iwe Israeli, ndiwe wodala!
Wofanana nanu ndani
anthu opulumutsidwa ndi Yehova?
Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu
ndi lupanga lanu la ulemerero.
Adani ako adzakugonjera,
ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”
Mose Amwalira
34 Ndipo Mose anakwera Phiri la Nebo kuchokera ku chigwa cha Mowabu ndi kukafika pamwamba pa Phiri la Pisiga, kummawa kwa Yeriko. Kumeneko Yehova anamuonetsa dziko lonse; kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani. 2 Dera lonse la Nafutali, dziko lonse la Efereimu ndi Manase, dziko lonse la Yuda mpaka kukafika kumadzulo kwa nyanja, 3 Negevi ndi chigawo chonse kuchokera ku Chigwa cha Yeriko, Mzinda wa mitengo ya migwalangwa, mpaka ku Zowari. 4 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, “Limenelo ndi dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo pamene ndinanena kuti, ‘Ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ Ndakulola kuti ulione, koma sudzawoloka kuti ukalowemo.”
5 Choncho Mose mtumiki wa Yehova anamwalira kumeneko ku Mowabu, monga momwe ananenera Yehova. 6 Yehova anamuyika mʼmanda ku Mowabu, mʼchigwa choyangʼanana ndi Beti-Peori, koma mpaka lero palibe amene amadziwa pamene pali manda ake. 7 Mose anamwalira ali ndi zaka 120, koma maso ake ankaonabe ndipo anali amphamvu. 8 Aisraeli analira maliro a Mose mʼchikhwawa cha Mowabu kwa masiku makumi atatu mpaka nthawi ya kulira maliro ndi kukhuza inatha.
9 Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.
10 Kuyambira nthawi imeneyi, mu Israeli simunakhalepo mneneri wina aliyense wofanana ndi Mose, amene Yehova amayankhula naye maso ndi maso. 11 Amene anachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi ndi zozizwitsa zimene Yehova anamutuma kuti achite mu Igupto, kwa Farao ndi kwa nduna zake zonse ndiponso mʼdziko lake lonse. 12 Ndithudi palibe mneneri wina aliyense amene anachita zinthu zazikulu ndi zoopsa zofanana ndi zomwe Mose anachita pamaso pa Aisraeli onse.
Kofu
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova,
ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni
ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;
chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,
kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira,
koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi,
malamulo anu onse ndi woona.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu
kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Reshi
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola;
sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa,
pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu;
sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri,
koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro,
popeza samvera mawu anu.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu;
sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Mawu anu onse ndi owona;
malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Sini ndi Shini
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa,
koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu,
ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho,
koma ndimakonda malamulo anu.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku
pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu,
ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova,
ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Ndimamvera umboni wanu
pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu,
pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Tawu
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova;
patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu;
pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga,
pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu,
popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza
pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova,
ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,
ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika,
funafunani mtumiki wanu,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Ulemerero wa Ziyoni
60 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika,
ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi
ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina,
koma Yehova adzakuwalira iwe,
ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako
ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika.
Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe;
ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali
ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri,
mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe;
chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe
chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako,
ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai.
Ndipo onse a ku Seba adzabwera
atanyamula golide ndi lubani
uku akutamanda Yehova.
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu,
nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani;
zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe,
ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo,
ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali;
patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi,
zikubweretsa ana ako ochokera kutali,
pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo,
kudzalemekeza Yehova Mulungu wako,
Woyerayo wa Israeli,
pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 “Alendo adzamanganso malinga ako,
ndipo mafumu awo adzakutumikira.
Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya,
koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse,
sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku,
kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo,
akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe;
adzawonongeka kotheratu.
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini,
mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni
kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika;
ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani;
onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu.
Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova;
Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe,
koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya,
ndipo udzakhala malo a chimwemwe
cha anthu amibado yonse.
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu
ndi kuleredwa pa maere aufumu,
motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako,
Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa,
ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo.
Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa
ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala.
Olamulira ako adzakhala a mtendere.
Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako,
bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako,
ndidzakhala malinga ako okuteteza
ndipo udzanditamanda.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire,
kapena mwezi kuti uwunikire usiku,
pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya,
ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Dzuwa lako silidzalowanso,
ndipo mwezi wako sudzazimiriranso;
Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya,
ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama
ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya.
Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala,
ntchito ya manja anga,
kuti aonetse ulemerero wanga.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko,
kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu.
Ine ndine Yehova,
nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
Yesu Achiritsa Wakhate
8 Iye atatsika ku phiri kuja, anthu ambirimbiri anamutsata. 2 Ndipo munthu wakhate anadza kwa Yesu namugwadira nati, “Ambuye, ngati mufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
3 Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” Nthawi yomweyo anachiritsidwa khate lake. 4 Ndipo Yesu anati kwa iye, “Taona, usawuze wina aliyense. Koma upite kwa mkulu wa ansembe ukadzionetse wekha ndi kupereka mphatso imene Mose analamulira, kuti ukhale umboni kwa iwo.”
Chikhulupiriro cha Kenturiyo
5 Yesu atalowa mʼKaperenamu, Kenturiyo anabwera kwa Iye napempha chithandizo, 6 nati, “Ambuye, wantchito wanga ali chigonere ku nyumba, sakuthanso kuyenda, akumva kuwawa kwambiri.”
7 Ndipo Yesu anati kwa iye, “Ine ndibwera kudzamuchiritsa.”
8 Kenturiyo uja anayankha kuti, “Ambuye, ndine wosayenera kuti Inu mukalowe mʼnyumba mwanga. Koma mungonena mawu ndipo wantchito wanga adzachiritsidwa. 9 Pakuti inenso ndili pansi pa ulamuliro ndipo ndili ndi asilikali amene ndiwalamulira. Ndikalamulira mmodzi kuti, ‘Pita,’ amapita; ndi kwa wina kuti, ‘Bwera,’ amabwera. Ndikawuza wantchito wanga kuti, ‘Chita ichi,’ iye amachita.”
10 Yesu atamva zimenezi, anadabwa ndipo anati kwa omutsatira, “Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti sindinapeze wina aliyense mu Israeli wachikhulupiriro chachikulu chotere. 11 Ndikuwuzani kuti ambiri adzabwera kuchokera kummawa ndi kumadzulo, nadzakhala nawo pa phwando pamodzi ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo mu ufumu wakumwamba. 12 Koma eni ake ufumuwo adzaponyedwa ku mdima wakunja kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
13 Pamenepo Yesu anati kwa Kenturiyo, “Pita! Zichitike monga momwe wakhulupirira.” Ndipo wantchito wake anachira pa nthawi yomweyo.
Yesu Achiritsa Anthu Ambiri
14 Ndipo Yesu atalowa mʼnyumba ya Petro, anaona mpongozi wake wa Petro ali gone akudwala malungo. 15 Ndipo Yesu anakhudza dzanja lake ndipo pomwepo anachira nayamba kumutumikira.
16 Itafika nthawi yamadzulo, anthu anabweretsa kwa Iye anthu ambiri ogwidwa ndi ziwanda ndipo anatulutsa ziwandazo ndi mawu okha, nachiritsa odwala onse. 17 Uku kunali kukwaniritsa zimene ananena mneneri Yesaya kuti,
“Iye anatenga zofowoka zathu,
nanyamula nthenda zathu.”
Za Kutsatira Yesu
18 Yesu ataona gulu la anthu litamuzungulira, analamula kuti awolokere kutsidya lina la nyanja. 19 Ndipo mphunzitsi wa malamulo anabwera kwa Iye nati, “Aphunzitsi, ine ndidzakutsatani kulikonse kumene muzipita.”
20 Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ndi mbalame zamlengalenga zili ndi zisa, koma Mwana wa Munthu alibe malo ogona ngakhale potsamira mutu wake.”
21 Wophunzira wina anati kwa Iye, “Ambuye, mundilole ndiyambe ndakayika maliro a abambo anga.”
22 Koma Yesu anamuwuza kuti, “Nditsate Ine ndipo uwaleke akufa ayikane akufa okhaokha.”
Yesu Aletsa Namondwe
23 Iye atalowa mʼbwato, ophunzira ake anamutsatira. 24 Ndipo taonani mwadzidzidzi mphepo yayikulu yamkuntho inawomba pa nyanjapo, kotero kuti bwatolo linayamba kumizidwa ndi mafunde. Koma Yesu anali mtulo. 25 Ophunzira ake anapita namudzutsa nati, “Ambuye! Tipulumutseni! Tikumira!”
26 Iye anawayankha kuti, “Inu achikhulupiriro chochepa, chifukwa chiyani mukuchita mantha?” Ndipo anayimirira nadzudzula mphepoyo ndi mafunde ndipo panali bata lalikulu.
27 Ndipo ophunzirawo anadabwa nafunsa kuti, “Ndi munthu wotani uyu? Kuti ngakhale mphepo ndi mafunde zimvera Iye!”
Ogwidwa ndi Ziwanda a ku Gadara
28 Ndipo atafika ku mbali ina ya dera la Gadara, anakumana ndi anthu awiri ogwidwa ndi ziwanda akuchokera ku manda. Iwowa anali woopsa kwambiri kotero kuti panalibe munthu akanatha kudzera njira imeneyo. 29 Ndipo iwo anafuwulira kwa Yesu nati, “Mukufuna chiyani kwa ife, Inu Mwana wa Mulungu? Kodi mwabwera kuno kudzatizunza nthawi yake isanafike?”
30 Ndipo patali pake panali gulu la nkhumba zimene zimadya. 31 Ndipo ziwandazo zinamupempha Yesu kuti, “Ngati mutitulutsa ife mutitumize mu nkhumba izo.”
32 Iye anati kwa ziwandazo, “Pitani!” Ndipo pamenepo zinatuluka ndi kukalowa mʼnkhumbazo ndipo nkhumba zonse zinathamangira mʼnyanja ndi kufera momwemo. 33 Koma amene amaziweta anathawa nalowa mʼmudzi nafotokoza zonse, kuphatikizapo zimene zinachitika ndi anthu ogwidwa ndi ziwanda aja. 34 Ndipo anthu onse a mʼmudziwo anatuluka kukakumana ndi Yesu. Ndipo atamuona Iye, anamupempha kuti achoke mʼdera lawo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.