M’Cheyne Bible Reading Plan
32 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula;
imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula
ndipo mawu anga atsike ngati mame,
ngati mvumbi pa udzu watsopano,
ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova.
Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro,
njira zake zonse ndi zolungama.
Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa,
Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake,
iwo si ana akenso,
koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere,
inu anthu opusa ndi opanda nzeru?
Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu,
amene anakupangani ndi kukuwumbani?
7 Kumbukirani masiku amakedzana;
ganizirani za mibado yakalekale.
Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza,
akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo,
pamene analekanitsa anthu onse,
anayikira malire anthu onse
molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake,
Yakobo ndiye cholowa chake.
10 Anamupeza mʼchipululu,
ku malo owuma ndi kopanda kanthu.
Anamuteteza ndi kumusamalira;
anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake
nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake,
chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo
ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera;
popanda thandizo la mulungu wachilendo.
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko
ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda.
Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe,
ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa,
ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi,
pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani
ndiponso tirigu wabwino kwambiri.
Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira;
atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi.
Anasiya Mulungu amene anamulenga
ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo
ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu,
milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe,
milungu yongobwera kumene,
milungu imene makolo anu sankayiopa.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani;
munayiwala Mulungu amene anakubalani.
19 Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana
chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
20 Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga,
ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani;
pakuti ndi mʼbado wopotoka,
ana amene ndi osakhulupirika.
21 Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu
ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe.
Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake;
ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
22 Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto,
umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa.
Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake
ndipo udzapsereza maziko a mapiri.
23 “Ndidzawawunjikira masautso
ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
24 Ndidzawatumizira njala yoopsa,
malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo;
ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta,
ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
25 Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana;
mantha adzalamulira nyumba zawo.
Anyamata ndi atsikana adzafa,
ngakhalenso makanda ndi okalamba.
26 Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza
ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
27 koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze,
mwina adani anga sadzandimvetsetsa
ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife;
Yehova sanachite zonsezi.’ ”
28 Iwo ndi mtundu wopanda maganizo,
iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
29 Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi
ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
30 Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000
kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse,
Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa,
Yehova akanapanda kuwataya?
31 Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu,
ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
32 Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu
ndiponso ku minda ya ku Gomora.
Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha
ndipo maphava ake ndi owawa.
33 Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka,
ululu woopsa wa mphiri.
34 “Kodi zimenezi sindinazisunge
ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
35 Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.
Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera;
tsiku lawo la masautso layandikira
ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
36 Yehova adzaweruza anthu ake
ndipo adzachitira atumiki ake chifundo
pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha
ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
37 Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo,
thanthwe limene ankabisalamo,
38 milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo
ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?”
Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni!
Ibwere kuti idzakutetezenitu!
39 “Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo!
Palibe mulungu wina koma Ine ndekha.
Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo,
ndavulaza ndipo ndidzachiritsa,
ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti,
‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira
ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo,
ndidzabwezera chilango adani anga
ndi kulanga onse odana nane.
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo
pamene lupanga langa lidzawononga mnofu:
magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo,
mitu ya atsogoleri a adani.’ ”
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake,
pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake;
adzabwezera chilango adani ake
ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva. 45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli, 46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa. 47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
Mose Adzafera pa Phiri la Nebo
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti, 49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo. 50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. 51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli. 52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”
Ayini
121 Ndachita zolungama ndi zabwino;
musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino,
musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu,
kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa,
kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu;
malamulo anu akuswedwa.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu
kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka,
ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Pe
129 Maumboni anu ndi odabwitsa
nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika;
ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu,
kufunafuna malamulo anu.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo,
monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu;
musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza,
kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga,
chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Tsade
137 Yehova ndinu wolungama,
ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;
ndi odalirika ndithu.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga
chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri
nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,
sindiyiwala malangizo anu.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya,
ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera,
koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Tchimo, Kuvomereza ndi Chipulumutso
59 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa,
kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani
ndi Mulungu wanu;
ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu,
kotero Iye sadzamva.
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi.
Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu.
Pakamwa panu payankhula zabodza,
ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama,
palibe amene akupita ku mlandu moona mtima.
Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza;
amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
5 Iwo amayikira mazira a mamba
ndipo amaluka ukonde wakangawude.
Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa,
ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala;
ndipo chimene apangacho sangachifunde.
Ntchito zawo ndi zoyipa,
ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
7 Amathamangira kukachita zoyipa;
sachedwa kupha anthu osalakwa.
Maganizo awo ndi maganizo oyipa;
kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere;
zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo.
Njira zawo zonse nʼzokhotakhota;
aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira;
ndipo chipulumutso sichitifikira.
Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha;
tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona,
kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso.
Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku;
timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo:
Timalira modandaula ngati nkhunda.
Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza.
Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu,
ndipo machimo athu akutsutsana nafe.
Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse
ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 Tawukira ndi kumukana Yehova.
Tafulatira Mulungu wathu,
pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova,
ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka
ndipo choonadi chili kutali ndi ife;
kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu,
ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko,
ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto.
Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa
kuti panalibe chiweruzo cholungama.
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe,
Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera;
Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza,
ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa,
ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso;
anavala kulipsira ngati chovala
ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake
molingana ndi zimene anachita,
adzaonetsa ukali kwa adani ake
ndi kubwezera chilango odana naye.
Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
19 Choncho akadzabwera ngati madzi
oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho.
Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa
adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
20 “Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni
kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,”
akutero Yehova.
21 Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,”
akutero Yehova.
Za Kuweruza Ena
7 “Musaweruze ena, kuti inunso mungadzaweruzidwe. 2 Pakuti momwe inu muweruzira ena, inunso mudzaweruzidwa chimodzimodzi, muyeso umene muyesera ena inunso mudzayesedwa ndi womwewo.
3 “Chifukwa chiyani iwe uyangʼana kachitsotso ka mʼdiso la mʼbale wako koma susamalira chimtengo chili mʼdiso mwako? 4 Kodi unganene bwanji kwa mʼbale wako kuti, ‘Ndikuchotse kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene nthawi zonse chimtengo uli nacho mʼdiso mwako? 5 Wachiphamaso iwe! Yamba wachotsa chimtengo chili mʼdiso mwako ndipo pamenepo udzatha kuona bwino ndi kuchotsa kachitsotso kali mʼdiso mwa mʼbale wako.
6 “Musapatse agalu zinthu zopatulika; kapena musaponyere nkhumba ngale zanu. Pakuti ngati mutero, zidzaziponda ndipo pomwepo zidzakutembenukirani ndi kukudulani nthulinthuli.
Pemphani, Funafunani, Gogodani
7 “Pemphani ndipo mudzapatsidwa; funafunani ndipo mudzapeza; gogodani ndipo adzakutsekulirani. 8 Pakuti wopempha aliyense amalandira; ndi wofuna amapeza; ndipo iye amene agogoda, adzamutsekulira.
9 “Ndani mwa inu, mwana wake akamupempha buledi amamupatsa mwala? 10 Kapena ngati mwana apempha nsomba, kodi amamupatsa njoka? 11 Tsono ngati inu woyipitsitsa mumadziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, nanga Atate anu akumwamba sadzapereka mphatso zabwino kwa iwo amene amupempha? 12 Nʼchifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu akuchitireni, yambani ndinu kuwachitira, pakuti izi ndi zimene malamulo ndi aneneri amaphunzitsa.
Zipata Ziwiri ndi Njira Ziwiri
13 “Lowani pa chipata chopapatiza. Pakuti chipata cholowera kuchiwonongeko nʼchachikulu ndipo msewu wake ndi waukulunso. Ndipo anthu ambiri amalowera pamenepo. 14 Koma chipata ndi chopapatiza ndi msewu ndi waungʼono umene utsogolera anthu ku moyo wosatha ndipo ndi owerengeka okha amene ayipeza njirayo.
Aneneri Owona ndi Onyenga
15 “Chenjerani nawo aneneri onyenga. Amabwera kwa inu atavala zikopa zankhosa, koma mʼkati mwawo ali mimbulu yolusa. 16 Mudzawazindikira iwo ndi zipatso zawo. Kodi anthu amathyola mpesa pa mtengo wa minga, kapena nkhuyu pa nthula? 17 Chimodzimodzinso mtengo wabwino umabala chipatso chabwino, koma mtengo woyipa umabala chipatso choyipa. 18 Mtengo wabwino sungabale chipatso choyipa, ndi mtengo woyipa sungabale chipatso chabwino. 19 Mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino umadulidwa ndi kuponyedwa pa moto. 20 Momwemonso, ndi zipatso zawo iwo mudzawazindikira.
Ophunzira Owona ndi Onyenga
21 “Si munthu aliyense amene amanena kwa Ine, ‘Ambuye, Ambuye,’ adzalowe mu ufumu wakumwamba, koma ndi yekhayo amene amachita chifuniro cha Atate anga amene ali kumwamba. 22 Ambiri adzati kwa Ine pa tsikulo, ‘Ambuye, Ambuye, kodi sitinkanenera mʼdzina lanu ndi mʼdzina lanunso tinkatulutsa ziwanda ndi kuchita zodabwitsa zambiri?’ 23 Pamenepo ndidzawawuza momveka bwino kuti, ‘Sindinakudziweni inu. Chokani kwa Ine, inu ochita zoyipa!’
Womanga Nyumba Wanzeru ndi Wopusa
24 “Nʼchifukwa chake aliyense amene amva mawu anga ndi kuwachita akufanana ndi munthu wanzeru amene anamanga nyumba yake pa thanthwe. 25 Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo; koma sinagwe, chifukwa maziko ake anali pa thanthwe. 26 Koma aliyense amene amva mawu angawa ndi kusawachita ali ngati munthu wopusa amene anamanga nyumba yake pa mchenga. 27 Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo, ndipo inagwa ndipo kugwa kwake kunali kwakukulu.”
28 Yesu atamaliza kunena zonsezi, magulu a anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, 29 chifukwa anaphunzitsa ngati amene anali ndi ulamuliro osati ngati aphunzitsi amalamulo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.