M’Cheyne Bible Reading Plan
Madalitso Akabwerera kwa Yehova
30 Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu, 2 ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino, 3 pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani. 4 Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso. 5 Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu. 6 Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo. 7 Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani. 8 Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino. 9 Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu, 10 ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Moyo kapena Imfa
11 Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali. 12 Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?” 13 Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?” 14 Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
15 Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko. 16 Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
17 Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza, 18 lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
19 Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo. 20 Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
Yodi
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona,
chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama
ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,
molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo,
popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa;
koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine,
iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu
kuti ndisachititsidwe manyazi.
Kafu
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu,
koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu;
Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi
sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti?
Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Anthu osalabadira za Mulungu,
odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika;
thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi
koma sindinataye malangizo anu.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Lamedi
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya;
akhazikika kumwambako.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse;
Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino,
pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa,
ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu,
pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni;
pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge,
koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire,
koma malamulo anu alibe malire konse.
57 Anthu olungama amafa,
ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake;
anthu odzipereka amatengedwa,
ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake.
Anthu olungama amatengedwa
kuti tsoka lisawagwere.
2 Iwo amene amakhala moyo wolungama
amafa mwamtendere;
amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
3 “Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa,
inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
4 Kodi inu mukuseka yani?
Kodi mukumunena ndani
ndi kupotoza pakamwa panu?
Kodi inu si ana owukira,
zidzukulu za anthu abodza?
5 Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu,
ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri.
Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa
ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
6 Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu.
Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo,
ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya.
Kodi zimenezi
zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
7 Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali.
Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
8 Mʼnyumba mwanu mwayika
mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu.
Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu.
Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu,
ndiye mwazilipira kuti mugone nazo.
Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
9 Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta
ndi zonunkhira zochuluka.
Munachita kutumiza akazembe anu kutali;
inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko!
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu,
koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’
Munapezako kumeneko zokhumba zanu
nʼchifukwa chake simunalefuke.
11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa,
kotero kuti mwakhala mukundinamiza,
ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe,
kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine?
Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti
ndakhala chete nthawi yayitali?
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama,
ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo,
mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni!
Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo,
mpweya chabe udzawulutsa mafanowo.
Koma munthu amene amadalira ine
adzalandira dziko lokhalamo.
Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
Mpumulo kwa Anthu Osweka Mtima
14 Ndipo panamveka mawu akuti,
“Undani, undani, konzani msewu!
Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse,
amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo,
akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika,
koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima
kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse
ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya
kapena kuwapsera mtima nthawi zonse,
popeza kuti ndinalenga anthu anga
ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera;
ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya,
koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa;
kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
19 anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo.
Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,”
“Ndipo ndidzawachiritsa.”
Akutero Yehova.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka,
yosatha kukhala bata,
mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.
Chiphunzitso cha pa Phiri
5 Iye ataona anthu ambiri, anakwera pa phiri nakhala pansi. Ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye, 2 ndipo anayamba kuwaphunzitsa kuti,
3 “Odala ndi amene ali osauka mu mzimu,
chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.
4 Odala ndi amene ali achisoni,
chifukwa adzatonthozedwa.
5 Odala ndi amene ali ofatsa,
chifukwa adzalandira dziko lapansi.
6 Odala ndi amene akumva njala ndi ludzu la chilungamo,
chifukwa adzakhutitsidwa.
7 Odala ndi amene ali ndi chifundo,
chifukwa adzawachitira chifundo.
8 Odala ndi amene ali oyera mtima,
chifukwa adzaona Mulungu.
9 Ndi odala amene amabweretsa mtendere,
chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.
10 Odala ndi amene akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo,
pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”
11 “Inu ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani, kukunenerani zoyipa zilizonse ndi kukunamizirani chifukwa cha Ine. 12 Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.
Mchere ndi Kuwunika
13 “Inu ndinu mchere wa dziko lapansi. Koma ngati mcherewo usukuluka, adzawukometsanso ndi chiyani? Ulibenso ntchito koma kungowutaya kunja, anthu nawuponda.
14 “Inu ndinu kuwunika kwa dziko lapansi. Mzinda wa pa phiri sungathe kubisika. 15 Anthu sayatsa nyale ndikuyivundikira ndi mbiya, mʼmalo mwake amayika poonekera ndipo imawunikira onse mʼnyumbamo. 16 Momwemonso kuwunika kwanu kuwale pamaso pa anthu kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kulemekeza Atate anu akumwamba.
Kukwaniritsa Malamulo
17 “Musaganize kuti ndinadza kudzathetsa malamulo kapena zonena za aneneri; sindinabwere kudzathetsa koma kukwaniritsa. 18 Ine ndikukuwuzani zoonadi kuti, kufikira kutha kwa thambo ndi dziko lapansi, chilichonse chimene chinalembedwa mʼmalamulo, ngakhale kalemba kakangʼonongʼono, chidzakwaniritsidwa. 19 Chifukwa chake aliyense amene aphwanya limodzi la malamulowa ngakhale lalingʼonongʼono ndi kuphunzitsa ena kuti achite chimodzimodzi, adzakhala wotsirizira mu ufumu wakumwamba, koma aliyense amene achita ndi kuphunzitsa malamulo awa adzakhala wamkulu mu ufumu wakumwamba. 20 Chifukwa chake ndikuwuzani kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, zoonadi, simudzalowa mu ufumu wakumwamba.
Zokhudza Kupha
21 “Munamva kuti kunanenedwa kwa anthu kale kuti, ‘Usaphe ndipo kuti aliyense amene apha munthu adzaweruzidwa.’ 22 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena.
23 “Nʼchifukwa chake, pamene ukupereka chopereka chako pa guwa lansembe ndipo nthawi yomweyo ukumbukira kuti mʼbale wako ali nawe chifukwa, 24 usiye choperekacho pa guwa lansembepo, choyamba pita kayanjane ndi mʼbale wako; ukatero bwera kudzapereka chopereka chakocho.
25 “Fulumira kuyanjana ndi mnzako amene unamulakwira nthawi ya milandu isanafike chifukwa angakupereke kwa oweruza amene angakupereke kwa mlonda ndipo mlondayo angakutsekere mʼndende. 26 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti sudzatuluka mʼndende mpaka utalipira zonse.
Zokhudza Chigololo
27 “Munamva kuti kunanenedwa kuti, ‘Usachite chigololo.’ 28 Koma Ine ndikuwuzani kuti aliyense woyangʼana mkazi momusirira wachita naye kale chigololo mu mtima mwake. 29 Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. 30 Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena.
Zokhudza Kusudzula Mkazi
31 “Ananena kuti, ‘Aliyense wosudzula mkazi wake ayenera amupatse kalata ya chisudzulo.’ 32 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake pa chifukwa china chilichonse osati chifukwa cha chiwerewere, akumuchititsa mkaziyo chigololo ndipo aliyense wokwatira mkaziyo, akuchitanso chigololo.
Malonjezo
33 “Munamvanso kuti kunanenedwa kwa anthu akale kuti, ‘Musaphwanye lonjezo; koma sungani malonjezo anu amene mwachita kwa Yehova.’ 34 Koma ndikuwuzani kuti musalumbire ndi pangʼono pomwe kutchula kumwamba chifukwa kuli mpando waufumu wa Mulungu. 35 Kapena kutchula dziko lapansi, chifukwa ndi chopondapo mapazi ake; kapena kutchula Yerusalemu, chifukwa ndi mzinda wa mfumu yayikulu. 36 Ndipo musalumbire ndi mutu wanu chifukwa simungathe kuyeretsa ngakhale kudetsa tsitsi limodzi. 37 Koma ‘Inde’ wanu akhaledi ‘Inde’ kapena ‘Ayi’ wanu akhaledi ‘Ayi,’ chilichonse choposera apa, chichokera kwa woyipayo.
Za Kubwezera Choyipa
38 “Munamva kuti, ‘Diso kulipira diso ndi dzino kulipira dzino.’ 39 Koma ndikuwuzani kuti musamukanize munthu woyipa, akakumenya patsaya mupatseni tsaya linalo. 40 Ndipo ngati wina afuna kukuzenga mlandu kuti akulande malaya ako, umupatsenso mkanjo wako. 41 Ngati wina akukakamiza kuti uyende naye mtunda umodzi, iwe uyende naye mitunda iwiri. 42 Wina akakupempha kanthu umupatse, ndipo wofuna kubwereka usamukanize.
Kukonda Adani
43 “Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’ 44 Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani 45 kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’ 46 Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi? 47 Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi? 48 Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.