M’Cheyne Bible Reading Plan
Nsembe Yopepesera Munthu Akaphedwa Mosadziwika Bwino
21 Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha, 2 akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira. 3 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli 4 ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo. 5 Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana. 6 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija, 7 nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako. 8 Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa. 9 Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.
Kukwatira Mkazi Wogwidwa ku Nkhondo
10 Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo, 11 ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu. 12 Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake 13 ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu. 14 Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.
Ufulu wa Mwana Woyamba Kubadwa
15 Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo, 16 akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda. 17 Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.
Mwana Wamwamuna Wowukira
18 Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza, 19 abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo 20 akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.” 21 Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.
Malamulo Osiyanasiyana
22 Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo, 23 musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.
Nyimbo. Salimo la Davide.
108 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu;
ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe!
Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;
ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba;
kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba,
ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja
kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:
“Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu
ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;
Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,
Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo
ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu;
ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa?
Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana
ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani,
pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano,
ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide.
109 Mulungu amene ndimakutamandani,
musakhale chete,
2 pakuti anthu oyipa ndi achinyengo
atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane;
iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 Andizungulira ndi mawu audani,
amandinena popanda chifukwa.
4 Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza,
koma ine ndine munthu wapemphero.
5 Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino,
ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye;
lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa,
ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Masiku ake akhale owerengeka;
munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Ana ake akhale amasiye
ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha;
apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo;
alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima
kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa,
mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova;
tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse,
kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo,
koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka
ndi osweka mtima.
17 Anakonda kutemberera,
matembererowo abwerere kwa iye;
sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena,
choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Anavala kutemberera ngati chovala;
kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi,
kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho,
ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga,
kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse,
muchite nane molingana ndi dzina lanu,
chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa,
ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo,
ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya,
thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane;
akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga;
pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu,
kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa;
pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi,
koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo,
ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri;
ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo,
kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
Israeli ndi Nkhutukumve
48 “Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo,
inu amene amakutchani dzina lanu Israeli,
ndinu a fuko la Yuda,
inu mumalumbira mʼdzina la Yehova,
ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli,
ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.
2 Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika
ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli,
amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
3 Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale,
zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza;
tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.
4 Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve
wa nkhongo gwaa,
wa mutu wowuma.
5 Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe;
zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe
kuti unganene kuti,
‘Fano langa ndilo lachita zimenezi,
kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’
6 Inu munamva zinthu zimenezi.
Kodi inu simungazivomereze?
“Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano
zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.
7 Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale;
munali musanazimve mpaka lero lino.
Choncho inu simunganene kuti,
‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’
8 Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa;
makutu anu sanali otsekuka.
Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti
chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.
9 Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa.
Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze.
Sindidzakuwonongani kotheratu.
10 Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva;
ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.
11 Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi.
Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke?
Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.
Kumasulidwa kwa Israeli
12 “Tamvera Ine, iwe Yakobo,
Israeli, amene ndinakuyitana:
Mulungu uja Woyamba
ndi Wotsiriza ndine.
13 Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi,
dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga.
Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba
ndi dziko lapansi.
14 “Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani:
Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi?
Wokondedwa wa Yehova uja adzachita
zomwe Iye anakonzera Babuloni;
dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.
15 Ine, Inetu, ndayankhula;
ndi kumuyitana
ndidzamubweretsa ndine
ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.
16 “Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi:
“Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa;
pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.”
Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake
ndi kundituma.
17 Yehova, Mpulumutsi wanu,
Woyerayo wa Israeli akuti,
“Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndimakuphunzitsa kuti upindule,
ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.
18 Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga,
bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje,
ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.
19 Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga,
ana ako akanachuluka ngati fumbi;
dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga
ndipo silikanafafanizidwa konse.”
20 Tulukani mʼdziko la Babuloni!
Thawani dziko la Kaldeya!
Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo
ndipo muzilalikire
mpaka kumathero a dziko lapansi;
muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”
21 Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu;
anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe;
anangʼamba thanthwelo ndipo
munatuluka madzi.
22 “Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.
Kugwa kwa Babuloni
18 Zitatha izi ndinaona mngelo wina akutsika kuchokera kumwamba. Iye anali ndi ulamuliro waukulu, ndipo dziko lapansi linawala ndi ulemerero. 2 Mngeloyo anafuwula ndi mawu amphamvu kuti:
“ ‘Wagwa! Wagwa Babuloni Wamkulu!’
Wasandulika mokhalamo ziwanda
ndi kofikako mizimu yonse yoyipa
ndi mbalame zonse zonyansa
ndi zodetsedwa.
3 Pakuti mayiko onse amwa
vinyo ozunguza mutu wazigololo zake.
Mafumu a dziko lapansi achita naye chigololo,
ndipo amalonda a dziko lapansi analemera kuchokera pa zolakalaka zake zosefukira.”
Awachenjeza kuti Athawe Chiweruzo cha Babuloni
4 Ndiponso ndinamva mawu ena kuchokera kumwamba akuti:
“ ‘Anthu anga tulukani, mwa iye,’
mungachimwe naye
kuti musadzalandire nawo gawo lililonse la miliri yake;
5 pakuti machimo ake awunjikana mpaka kumwamba,
ndipo Mulungu wakumbukira milandu yake.
6 Bwezerani Iye monga momwe iye anakuchitirani.
Mubwezereni mowirikiza pa zimene anachita.
Mumusakanizire magawo awiri kuchokera mʼchikho chake.
7 Mumuzunze, kumumvetsa chisoni kwambiri
monga mwaulemerero ndi zolakalaka
zimene anadzaza mu mtima mwake. Iye anadzikuza nʼkumati,
‘Ndinakhala monga mfumu yayikazi,
ine sindine wamasiye
ndipo sindidzalira maliro.’
8 Chifukwa chake miliri yake idzamugonjetsa tsiku limodzi;
imfa, kulira maliro ndi njala.
Iye adzanyeka ndi moto
pakuti wamphamvu ndi Mulungu Ambuye amene wamuweruza.
Tsoka la Babuloni
9 “Mafumu a dziko lapansi, amene anachita naye chigololo nachita naye pamodzi zosangalatsa moyo uno, akadzaona utsi wa kunyeka kwake, adzalira nakhuza maliro ake. 10 Iwo adzayima kutali nalira chifukwa choopsedwa ndi mazunzo ake.
“ ‘Tsoka! Tsoka mzinda waukulu
iwe, Babuloni mzinda wamphamvu!
Mu ora limodzi chiwonongeko chako chafika!’
11 “Amalonda a dziko lapansi adzalira nakhuza maliro ake chifukwa palibenso amene akugula katundu wawo, 12 katundu wagolide, siliva, miyala yamtengo wapamwamba ndi ngale; nsalu zoyera kwambiri zapamwamba ndi zofiira; nsalu zasilika ndi zapepo; mitengo iliyonse yonunkhira ndi zinthu zilizonse zopangidwa ndi mnyanga, kapena matabwa ogulidwa ndi ndalama zambiri kapena mkuwa kapena chitsulo ndi mwala wonyezimira; 13 zokometsera zakudya, mure, lubani ndi zofukiza zina, vinyo ndi mafuta a olivi, ufa wosalala ndi tirigu; ngʼombe ndi nkhosa; akavalo ndi ngolo; ndi anthu adzagulitsidwa ukapolo.
14 “Iwo adzanena kuti, ‘Chipatso chimene unachilakalaka chakuchokera. Chuma chako chonse ndi ulemerero zatha, sizidzapezekanso.’ 15 Amalonda amene anagulitsa zinthu izi napeza chuma kuchokera kwa iye adzayima patali potero ataopsedwa ndi mazunzo ake. Adzalira ndi kukhuza maliro 16 ndipo adzalira mokuwa kuti,
“ ‘Tsoka! Tsoka! Mzinda waukulu,
iwe wovala nsalu zoyera kwambiri, zapepo ndi zofiira,
ndi wonyezimira ndi golide, miyala yamtengo wapamwamba ndi ngale!
17 Chuma chambiri choterechi chafika powonongeka mu ora limodzi!’
“Oyendetsa sitima ndi onse oyenda pa sitima ya pamadzi, ogwira ntchito mʼsitima ndi onse amene amadalira nyanja pamoyo wa tsiku ndi tsiku adzayima patali potero. 18 Akadzaona utsi wa kunyeka kwake, adzakuwa kuti, ‘Kodi panalinso mzinda wina ngati mzinda waukuluwu?’ 19 Adzathira fumbi pamitu pawo ndipo adzalira nakhuza maliro kuti,
“Tsoka! Tsoka mzinda waukulu iwe,
kumene onse anali ndi sitima pa nyanja
analemera kudzera mʼchuma chake!
Mu ora limodzi wawonongedwa.
20 “Kondwerani chifukwa cha iye inu kumwamba!
Kondwerani oyera mtima
ndi atumwi ndi aneneri!
Mulungu wamuweruza iye
monga momwe anakuchitirani inu.”
Chiwonongeko Chotsiriza cha Babuloni
21 Kenaka mngelo wamphamvu ananyamula mwala waukulu ngati mphero yayikulu nawuponya mʼnyanja nanena kuti,
“Mwa mphamvu chonchi
mzinda waukulu wa Babuloni udzaponyedwa pansi,
sudzapezekanso.
22 Mwa iwe simudzamvekanso liwu la woyimba zeze, ndi akatswiri a zoyimbayimba,
oyimba zitoliro, ndi lipenga.
Mwa iwe simudzapezekanso
mʼmisiri wina aliyense.
Mwa iwe simudzapezekanso
phokoso la mphero.
23 Kuwala kwa nyale
sikudzawunikanso mwa inu.
Mawu a mkwati ndi mkwatibwi
sadzamvekanso mwa iwe.
Amalonda anu anali akuluakulu a dziko lapansi.
Mitundu yonse inasokonezedwa ndi zamatsenga zako.
24 Mwa iye munapezeka magazi a aneneri ndi a oyera mtima,
ndi onse amene anaphedwa pa dziko lapansi.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.