M’Cheyne Bible Reading Plan
Za ku Nkhondo
20 Pamene mukupita kokachita nkhondo ndi adani anu, mukaona akavalo kapena magaleta kapena gulu la ankhondo kuposa inuyo musamaope chifukwa Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto adzakhala nanu. 2 Pamene mwatsala pangʼono kuyamba nkhondo, wansembe azibwera kutsogolo ndipo aziyankhula ku gulu lonse lankhondolo. 3 Iye aziti, “Tamverani inu Aisraeli, mukupita kukachita nkhondo ndi adani anu lero. Musataye mitima kapena kuchita mantha ayi. Musaopsedwe kapena kunjenjemera pamaso pawo, 4 pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye amene apite nanu kukakumenyerani nkhondo ndi kugonjetsa adani anu.”
5 Akuluakulu ankhondo adzati kwa gulu la ankhondolo, “Kodi pali wina amene wangomanga nyumba kumene ndipo sanayitsekulire? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondoko ndipo wina ndi kudzayitsekulira. 6 Kodi pali wina amene analima munda wamphesa ndipo sanayambe kudyerera? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzadyerera mundawo. 7 Kodi pali amene wachita chinkhoswe ndi mkazi ndipo sanamukwatire mkaziyo? Ayambe wabwerera ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzakwatira mkaziyo.” 8 Ndipo akuluakulu ankhondowo akapitirize kuti, “Kodi pali amene akuchita mantha kapena kutaya mtima? Abwerere ku mudzi kuopa kuti abale ake angatayenso mtima.” 9 Akuluakuluwo akatsiriza kuyankhula ndi gulu la ankhondolo, adzasankhe olilamulira.
10 Pamene mukuyandikira kuphwanya mzinda, muyambe mwafunsa anthu a mu mzindawo ngati afuna zamtendere. 11 Akavomera natsekula zipata zawo, anthu wonse mu mzindawo adzagwidwa ukapolo nakugwirirani ntchito. 12 Koma akakana za mtendere nachita nanu nkhondo, muwuphwanye mzindawo. 13 Yehova Mulungu wanu akakupatsani mzindawo, muwaphe amuna onse. 14 Akazi, ana, ziweto ndi china chilichonse mu mzindamo, mukhoza kuzitenga kuti zikhale zanu monga katundu wolanda ku nkhondo. Katundu wa adani anuyu amene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, mukhoza kumugwiritsa ntchito. 15 Mizinda yonse yakutali osati ya mitundu yapafupi, muzichita nayo chomwechi.
16 Komabe mʼmizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, musasiyemo chamoyo chilichonse. 17 Muwawononge kwathunthu Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi monga momwe Yehova Mulungu wanu anakulamulirani. 18 Mukapanda kutero adzakuphunzitsani kuti mutengere zinthu zonyansa zimene amachita popembedza milungu yawo ndipo mudzachimwira Yehova Mulungu wanu.
19 Mukalimbana ndi mzinda nthawi yayitali, kuchita nawo nkhondo pofuna kuwugonjetsa, musawononge podula mitengo yake ndi nkhwangwa, osayidula chifukwa zipatso zakezo mukhoza kudya. Kodi mitengo ya ku munda ndi anthu kuti mukalimbane nayo? 20 Komabe mukhoza kudula mitengo imene mukudziwa kuti si ya zipatso ndi kuyigwiritsa ntchito pa nkhondo mpaka mzinda umene mukumenyana nawowo utagwetsedwa.
BUKU LACHISANU
Masalimo 107–150
107 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Owomboledwa a Yehova anene zimenezi
amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
3 iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,
kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
4 Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,
osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
5 Iwo anamva njala ndi ludzu,
ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
6 Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
7 Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka
kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
8 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
9 pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu
ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
10 Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,
amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
11 pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu
ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
12 Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;
anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
13 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
14 Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu
ndipo anadula maunyolo awo.
15 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
16 pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa
ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.
17 Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,
ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
18 Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse
ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
19 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
20 Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;
anawalanditsa ku manda.
21 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
22 Apereke nsembe yachiyamiko
ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.
23 Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;
Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
24 Anaona ntchito za Yehova,
machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
25 Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho
imene inabweretsa mafunde ataliatali.
26 Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;
pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
27 Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;
anali pa mapeto a moyo wawo.
28 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
29 Yehova analetsa namondwe,
mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
30 Anali osangalala pamene kunakhala bata,
ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
31 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
32 Akuze Iye mu msonkhano wa anthu
ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.
33 Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,
akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
34 ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,
chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
35 Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi
ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
36 kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,
ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
37 Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa
ndipo anakolola zipatso zochuluka;
38 Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,
ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.
39 Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa
chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
40 Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka
anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
41 Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo
ngati magulu a nkhosa.
42 Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,
koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.
43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi
ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
Kugwa kwa Babuloni
47 “Tsika, ndi kukhala pa fumbi,
iwe namwali, Babuloni;
khala pansi wopanda mpando waufumu,
iwe namwali, Kaldeya
pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera
kumugwira mosamala.
2 Tenga mphero ndipo upere ufa;
chotsa nsalu yako yophimba nkhope
kwinya chovala chako mpaka ntchafu
ndipo woloka mitsinje.
3 Maliseche ako adzakhala poyera
ndipo udzachita manyazi.
Ndidzabwezera chilango
ndipo palibe amene adzandiletse.”
4 Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu,
dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
5 “Khala chete, ndipo lowa mu mdima,
iwe namwali, Kaldeya;
chifukwa sadzakutchulanso
mfumukazi ya maufumu.
6 Ndinawakwiyira anthu anga,
osawasamalanso.
Ndinawapereka manja mwako,
ndipo iwe sunawachitire chifundo.
Iwe unachitira nkhanza
ngakhale nkhalamba.
7 Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse
ngati mfumukazi.’
Koma sunaganizire zinthu izi
kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.
8 “Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe,
amene ukukhala mosatekesekawe,
umaganiza mu mtima mwako kuti,
‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina.
Sindidzakhala konse mkazi wamasiye,
ndipo ana anga sadzamwalira.’
9 Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi,
zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira:
ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye.
Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu
ngakhale ali ndi amatsenga ambiri
ndi mawula amphamvu.
10 Iwe unkadalira kuyipa kwako
ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’
Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza,
choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti,
‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’
11 Ngozi yayikulu idzakugwera
ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako.
Mavuto adzakugwera
ndipo sudzatha kuwachotsa;
chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa
chidzakugwera mwadzidzidzi.
12 “Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako,
pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo,
wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako.
Mwina udzatha kupambana
kapena kuopsezera nazo adani ako.
13 Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi!
Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni.
Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi
zimene ziti zidzakuchitikire.
14 Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi;
adzapsa ndi moto.
Sangathe kudzipulumutsa okha
ku mphamvu ya malawi a moto.
Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha;
kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
15 Umu ndi mmene adzachitire amatsenga,
anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito
ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako.
Onse adzamwazika ndi mantha,
sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”
Mkazi Wachiwerewere
17 Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja amene anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri anadza nati kwa ine, “Bwera ndikuonetse chilango cha mkazi wadama wotchuka uja amene akukhala pambali pa madzi ambiri. 2 Mafumu a dziko lapansi amachita naye chigololo ndipo okhala pa dziko lapansi analedzera ndi vinyo wa zigololo zake.”
3 Kenaka mngeloyo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku chipululu. Kumeneko ndinaona mkazi atakhala pa chirombo chofiira chokutidwa ndi mayina a chipongwe ndipo chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi. 4 Mkaziyo anavala zovala za pepo ndi zofiira nadzikongoletsa ndi golide, miyala yapamwamba ndi ngale. Ananyamula chikho chagolide mʼdzanja lake, chodzaza ndi zinthu zonyansa ndi fungo loyipa la zigololo zake. 5 Pa mphumi pake panalembedwa dzina lodabwitsa:
BABULONI WAMKULU
MAYI WA AKAZI ADAMA
NDI WAZOYIPITSA ZA DZIKO LAPANSI.
6 Ndinaona kuti mkaziyo anali ataledzera ndi magazi a oyera mtima, magazi a amene anachitira umboni Yesu.
Nditamuona mkaziyo ndinadabwa kwambiri. 7 Kenaka mngelo uja anati kwa ine, “Bwanji ukudabwa? Ndikufotokozera chinsinsi cha mkaziyu ndi chinsinsi cha chirombo chimene wakwerapochi chokhala ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi. 8 Chirombo chimene wachionachi chinalipo kale koma tsopano kulibe ndipo chidzatuluka ku chidzenje chakuya ndi kupita kukawonongedwa. Anthu okhala pa dziko lapansi amene mayina awo sanalembedwe mʼbuku lamoyo kuyambira pa kulengedwa kwa dziko lapansi adzadabwa pamene adzaona chirombocho, chifukwa chinalipo kale, tsopano kulibe, komabe chidzabwera.
9 “Zimenezi zikufunika kuganizira mwanzeru. Mitu isanu ndi iwiriyo ndi mapiri asanu ndi awiri pomwe mkazi uja amakhalirapo. Yomweyonso ndi mafumu asanu ndi awiri. 10 Mafumu asanu anagwa, imodzi ilipo ndipo ina sinabwere; koma pamene idzafika, idzayenera kukhala kwa kanthawi kochepa. 11 Chirombo chomwe chinalipo kale ndipo tsopano kulibe ndiyo mfumu yachisanu ndi chitatu. Iyo ndi ya mʼgulu la asanu ndi awiriwo ndipo ikupita kukawonongedwa.
12 “Nyanga khumi unaziona zija ndi mafumu khumi amene sanapatsidwe ulamuliro, koma adzapatsidwa ulamuliro pamodzi ndi chirombo kwa ora limodzi. 13 Mafumuwo ali ndi cholinga chimodzi ndipo adzapereka mphamvu ndi ulamuliro wawo kwa chirombocho. 14 Iwo adzachita nkhondo ndi Mwana Wankhosa, koma Mwana Wankhosayo adzawagonjetsa chifukwa Iye ndi Mbuye wa ambuye ndi Mfumu ya mafumu, ndipo amene adzakhala ndi Iye ndi oyitanidwa ake, osankhidwa ndi otsatira ake okhulupirika.”
15 Kenaka mngeloyo anati kwa ine, “Madzi amene unawaona pamene mkazi wadamayo anakhalapo ndiwo anthu ochuluka, mitundu ndi ziyankhulo. 16 Nyanga khumi ndi chirombo unazionazo zidzadya mkazi wadamayo. Zidzamufwifwitsa ndi kumusiya wamaliseche; zidzadya nyama yake ndi kumutentha ndi moto. 17 Pakuti Mulungu wayika ichi mʼmitima mwawo kuti akwaniritse cholinga chake povomerezana kupereka mphamvu zawo zolamulira kwa chirombo, kufikira Mawu a Mulungu atakwaniritsidwa. 18 Mkazi unamuonayo ndi mzinda waukulu umene ulamulira mafumu a dziko lapansi.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.