M’Cheyne Bible Reading Plan
Uthenga Woyamba wa Balaamu
23 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.” 2 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
3 Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.
4 Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”
5 Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
6 Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu. 7 Ndipo Balaamu ananena uthenga wake:
“Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu,
mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa.
Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga,
pita nyoza Israeli.’
8 Ndingatemberere bwanji
amene Mulungu sanawatemberere?
Ndinganyoze bwanji
amene Yehova sanawanyoze?
9 Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu,
ndikuwaona kuchokera pa zitunda.
Ndikuona anthu okhala pawokha,
osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.
10 Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi,
kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli?
Lekeni ndife imfa ya oyera mtima,
ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”
11 Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”
12 Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”
Uthenga Wachiwiri wa Balaamu
13 Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.” 14 Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
15 Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”
16 Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
17 Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”
18 Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake:
“Nyamuka Balaki ndipo tamvera;
Undimvere iwe mwana wa Zipori.
19 Mulungu si munthu kuti aname,
kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake.
Kodi amayankhula koma osachita?
Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?
20 Wandilamula kuti ndidalitse,
Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.
21 “Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo,
sanaone chovuta mu Israeli.
Yehova Mulungu wawo ali nawo:
mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.
22 Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto,
ali ndi mphamvu ngati za njati.
23 Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo,
palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli.
Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti,
‘Onani zimene Mulungu wachita!’
24 Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi;
adzuka okha ngati mkango waumuna
umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira
ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”
25 Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!
26 “Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’ ”
Uthenga Wachitatu wa Balaamu
27 Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.” 28 Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.
29 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.” 30 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
64 Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;
tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,
ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,
amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;
amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,
amayankhula zobisa misampha yawo;
ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,
“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”
Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;
mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa
ndi kuwasandutsa bwinja;
onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9 Anthu onse adzachita mantha;
adzalengeza ntchito za Mulungu
ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova
ndi kubisala mwa Iye,
owongoka mtima onse atamande Iye!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo.
65 Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni;
kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 Inu amene mumamva pemphero,
kwa inu anthu onse adzafika.
3 Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo,
Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Odala iwo amene inu muwasankha
ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu!
Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu,
za mʼNyumba yanu yoyera.
5 Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo,
Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi
ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu,
mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 Amene munakhalitsa bata nyanja
kukokoma kwa mafunde ake,
ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu;
kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera.
Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira;
Inuyo mumalilemeretsa kwambiri.
Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi
kuti upereke tirigu kwa anthu,
pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake,
mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka,
ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira;
mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Madambo akutidwa ndi zoweta
ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu;
izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.
Kulangidwa Kwa Babuloni
13 Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2 Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see,
muwafuwulire ankhondo;
muwakodole kuti adzalowe pa zipata
za anthu olemekezeka.
3 Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga;
ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira
amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4 Tamvani phokoso ku mapiri,
likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu!
Tamvani phokoso pakati pa maufumu,
ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi!
Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera
kuchita nkhondo.
5 Iwo akuchokera ku mayiko akutali,
kuchokera kumalekezero a dziko
Yehova ali ndi zida zake za nkhondo
kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6 Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira;
lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7 Zimenezi zinafowoketsa manja onse,
mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8 Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu,
zowawa ndi masautso zidzawagwera;
adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka.
Adzayangʼanana mwamantha,
nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9 Taonani, tsiku la Yehova likubwera,
tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo;
kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu
ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10 Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga
sizidzaonetsa kuwala kwawo.
Dzuwa lidzada potuluka,
ndipo mwezi sudzawala konse.
11 Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake,
anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo.
Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza,
ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12 Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino.
Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13 Tsono ndidzagwedeza miyamba
ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake.
Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse
pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14 Ngati mbawala zosakidwa,
ngati nkhosa zopanda wozikusa,
munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo,
aliyense adzathawira ku dziko lake.
15 Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa
adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16 Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona;
nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17 Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva
ndipo sasangalatsidwa ndi golide,
kuti amenyane ndi Ababuloni.
18 Adzapha anyamata ndi mauta awo;
sadzachitira chifundo ana
ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19 Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse.
Anthu ake amawunyadira.
Koma Yehova adzawuwononga
ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20 Anthu sadzakhalamonso
kapena kukhazikikamo pa mibado yonse;
palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake,
palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21 Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko,
nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe;
mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi,
ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22 Mu nsanja zake muzidzalira afisi,
mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe.
Nthawi yake yayandikira
ndipo masiku ake ali pafupi kutha.
1 Ndine Petro, mtumwi wa Yesu Khristu.
Ndikulemba kalatayi kwa onse osankhidwa ndi Mulungu, alendo mʼdziko lapansi, obalalikira ku Ponto, Galatiya, Kapadokiya, Asiya ndi Bituniya. 2 Mulungu Atate anakusankhani, atakudziwani kuyambira pachiyambi, ndipo Mzimu Woyera wakuyeretsani kuti mumvere Yesu Khristu ndikutsukidwa ndi magazi ake.
Chisomo ndi mtendere zikhale ndi inu mochuluka.
Kuyamika Mulungu Chifukwa cha Chiyembekezo Chamoyo
3 Alemekezedwe Mulungu, Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu. Mwachifundo chake chachikulu anatibadwitsa kwatsopano, mʼchiyembekezo chamoyo pomuukitsa Yesu Khristu kwa akufa, 4 kuti tidzalandire chuma chomwe sichingawonongeke, kuyipitsidwa kapena kufota. Chuma chimenechi akukusungirani kumwamba. 5 Mwachikhulupiriro, mukusungidwa ndi mphamvu ya Mulungu mpaka chipulumutso chitafika chimene chinakonzedwa kuti adzachionetse nthawi yotsiriza. 6 Zimenezi zikukondweretseni kwambiri, ngakhale tsopano, kwa kanthawi kochepa, mukumva zowawa mʼmayesero osiyanasiyana. 7 Mayeserowa abwera nʼcholinga chakuti chikhulupiriro chanu, chimene ndi chamtengo woposa wa golide, amene amawonongeka ngakhale amayengedwa ndi moto, chitsimikizike kuti ndi chenicheni. Pamenepo ndiye mudzalandire mayamiko, ulemerero ndi ulemu pamene Yesu Khristu adzaoneka. 8 Ngakhale kuti simunamuone, mumamukonda; ndipo ngakhale kuti simukumuona tsopano, mumamukhulupirira ndipo mumakondwera ndi chimwemwe chachikulu ndi chosaneneka. 9 Motero mukulandira mphotho ya chikhulupiriro chanu, ndiyo chipulumutso cha moyo wanu.
10 Kunena za chipulumutso chimenechi, aneneri amene ananeneratu za chisomo chimene chimabwera kwa inu, anafunafuna mofufuzafufuza za chipulumutsochi, 11 kufuna kudziwa nthawi ndi momwe zidzachitikire zinthu zimene Mzimu wa Khristu amene ali mwa iwo ankanenera za kuvutika kwa Khristu, ndi ulemerero umene adzakhale nawo pambuyo pake. 12 Mulungu anawawululira kuti ntchito yawoyo sankayigwira chifukwa cha iwo eni, koma chifukwa inu, pamene iwo ankayankhula zinthu zimene mwamva tsopano kuchokera kwa amene amalalikira Uthenga Wabwino mwamphamvu ya Mzimu Woyera wotumidwa kuchokera kumwamba. Ngakhale angelo amalakalaka kuona nawo zinthuzi.
Khalani Oyera Mtima
13 Choncho konzani mtima wanu, khalani odziretsa; khazikitsani chiyembekezo chanu kotheratu pa chisomo chimene mudzapatsidwe pamene Yesu Khristu adzaonekera. 14 Monga ana omvera, musatsatenso zilakolako zoyipa zomwe munali nazo pamene munali osadziwa. 15 Koma monga amene anakuyitanani ndi woyera, inunso khalani oyera mtima mʼmakhalidwe anu wonse. 16 Pakuti, kwalembedwa kuti, “Khalani oyera mtima, chifukwa Ine ndine Woyera.”
17 Popeza mumapemphera kwa Atate amene amaweruza munthu aliyense mopanda tsankho molingana ndi zochita zake, pa nthawi imene muli alendo pa dziko lapansi khalani moopa Mulungu. 18 Pakuti mukudziwa kuti simunawomboledwe ndi zinthu zimene zimawonongeka monga siliva kapena golide, kuchoka ku khalidwe lanu lachabe limene munalandira kwa makolo anu. 19 Koma munawomboledwa ndi magazi a mtengowapatali a Khristu, Mwana Wankhosa wopanda banga kapena chilema. 20 Iye anasankhidwa lisanalengedwe dziko lapansi, koma waonetsedwa chifukwa cha inu pa nthawi ino yotsiriza. 21 Kudzera mwa Iye mumakhulupirira Mulungu, amene anamuukitsa kwa akufa namupatsa ulemerero. Nʼchifukwa chake chikhulupiriro ndi chiyembekezo chanu chili mwa Mulungu.
22 Tsopano mwayeretsa mitima yanu pomvera choonadi, kuti muzikondana ndi abale anu, kukondana kwenikweni kochokera pansi pa mtima. 23 Popeza mwabadwanso, osati ndi mbewu imene imawonongeka, koma imene siwonongeka, ndiye kuti ndi Mawu a Mulungu amoyo ndi okhalitsa. 24 Pakuti,
“Anthu onse ali ngati udzu,
ndipo ulemerero wawo uli ngati duwa la kuthengo.
Udzu umafota ndipo duwa limathothoka,
25 koma mawu a Ambuye adzakhala mpaka muyaya.”
Ndipo awa ndi mawu amene tinalalikira kwa inu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.