Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

M’Cheyne Bible Reading Plan

The classic M'Cheyne plan--read the Old Testament, New Testament, and Psalms or Gospels every day.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Numeri 20

Madzi Ochokera Mʼthanthwe

20 Pa mwezi woyamba gulu lonse la Aisraeli linafika ku chipululu cha Zini, ndipo anakhala ku Kadesi. Miriamu anafera kumeneko ndipo anayikidwa mʼmanda.

Kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa, choncho anthuwo anasonkhana motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Anakangana ndi Mose kuti, “Kunali bwino ifenso tikanangofa pamene abale athu anafa pamaso pa Yehova! Chifukwa chiyani unabweretsa gulu la Yehova mʼchipululu muno, kuti ife ndi ziweto zathu tife kuno? Nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto ndi kutibweretsa kumalo woyipa ano? Kuno kulibe tirigu kapena nkhuyu, mphesa kapena makangadza. Ndipo kuno kulibenso madzi akumwa!”

Mose ndi Aaroni anachoka mu msonkhano ndi kupita pa khomo la tenti ya msonkhano, nagwa pansi chafufumimba ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera. Yehova anati kwa Mose, “Tenga ndodo, ndipo iwe ndi mʼbale wako Aaroni musonkhanitse anthu onse pamodzi. Uyankhule ndi thanthwe ilo iwo akuona ndipo lidzatulutsa madzi ake. Udzatulutsa madzi mʼthanthwe limeneli kuti anthu onse ndi ziweto zawo amwe.”

Choncho Mose anatenga ndodo pamaso pa Yehova monga momwe anamulamulira. 10 Mose ndi Aaroni anasonkhanitsa anthuwo pamodzi ku thanthwelo ndipo Mose anawawuza kuti, “Tamverani osamvera inu, kodi tikupatseni madzi kuchokera ku thanthwe ili?” 11 Choncho Mose anatukula dzanja lake ndi kumenya thanthwelo kawiri ndi ndodo yake ndipo madzi ambiri anatuluka mwamphamvu, ndipo anthu ndi ziweto zawo anamwa.

12 Koma Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Chifukwa chakuti simunandikhulupirire ndiponso simunandilemekeze monga Woyera pamaso pa Aisraeli, simudzalowetsa anthuwa mʼdziko limene ndikupereka kwa iwo.”

13 Awa anali madzi a ku Meriba, kumene Aisraeli anakangana ndi Yehova ndiponso kumene Yehovayo anadzionetsa yekha kuti ndi Woyera pakati pawo.

Aedomu Akaniza Njira Aisraeli

14 Mose anatumiza amithenga kuchokera ku Kadesi kupita kwa mfumu ya ku Edomu, kukanena kuti,

“Mʼbale wako Israeli akunena izi: Inuyo mukudziwa za mavuto onse amene anatigwera. 15 Makolo athu anapita ku Igupto ndipo tinakhala kumeneko zaka zambiri. Aigupto anatizunza pamodzi ndi makolo athuwo, 16 koma titalirira Yehova, Iyeyo anamva kulira kwathuko ndipo anatitumizira mngelo amene anatitulutsa ku Igupto.”

“Taonani, tsopano tili pano pa Kadesi, mzinda wa mʼmalire a dziko lanu. 17 Chonde mutilole tidutse mʼdziko lanu. Sitidzera mʼminda yanu kapena mu mpesa wanu, kapenanso kumwa madzi mʼchitsime chilichonse. Tidzayenda kutsata msewu waukulu wa mfumu ndipo sitidzapatukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”

18 Koma Edomu anayankha kuti,

“Musadutse kuno: Mukangoyesera tidzabwera ndi kumenyana nanu ndi lupanga.”

19 Aisraeli anayankha kuti,

“Tidzayenda motsata msewu waukulu. Ndipo ngati ife kapena ziweto zathu tidzamwa madzi anu tidzalipira. Tikungofuna tidutse nawo, palibenso china.”

20 Koma Edomu anayankhanso kuti,

“Musadutse.”

Kenaka Edomu anatuluka ndi gulu lankhondo lalikulu komanso lamphamvu. 21 Edomu anakaniza Israeli kuti adutse mʼdziko lake, choncho Israeli anabwerera.

Aaroni Amwalira

22 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Kadesi ndipo linafika ku phiri la Hori. 23 Ali pa phiri la Hori, pafupi ndi malire a Edomu, Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, 24 “Aaroni adzakakhala ndi anthu a mtundu wake, sadzalowa mʼdziko limene ndapereka kwa Aisraeli, chifukwa nonse munandiwukira motsutsana ndi malamulo anga ku madzi a ku Meriba. 25 Tenga Aaroni ndi mwana wake wamwamuna Eliezara ndipo ukwere nawo ku phiri la Hori. 26 Uvule Aaroni zovala zake ndipo umuveke mwana wake Eliezara, pakuti Aaroni adzafera komweko, ndipo adzakakhala ndi anthu a mtundu wake.”

27 Mose anachita monga Yehova anamulamulira: Anapita ku phiri la Hori gulu lonse likuona. 28 Pamenepo Mose anavula Aaroni zovala zake ndi kuveka mwana wake Eliezara. Aaroni anafa kumeneko pamwamba pa phirilo. Koma Mose ndi Eliezara anatsika ku phiriko, 29 ndipo pamene anthu onse anamva kuti Aaroni wafa, nyumba yonse ya Israeli inamulira Aaroniyo masiku makumi atatu.

Masalimo 58-59

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.

58 Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?
    Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,
    ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;
    kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,
    ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga,
    ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.

Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,
    Yehova khadzulani mano a mikango!
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda
    pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;
    ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.

Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,
    kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,
    pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Ndipo anthu adzanena kuti,
    “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;
    zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe.

59 Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu;
    munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
Landitseni kwa anthu ochita zoyipa
    ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.

Onani momwe iwo akundibisalira!
    Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane;
    osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo.
    Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
    dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse;
    musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.

Iwo amabweranso madzulo
    akuchita phokoso ngati agalu
    ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo;
    iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo,
    ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
Koma Inu Yehova, mumawaseka,
    mumayinyoza mitundu yonseyo.

Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu;
Inu Mulungu, ndinu linga langa. 10     Mulungu wanga wachikondi.

Mulungu adzapita patsogolo panga
    ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu,
    kuopa kuti anthu anga angayiwale.
Mwa mphamvu zanu,
    lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo
    chifukwa cha mawu a milomo yawo,
    iwo akodwe mʼkunyada kwawo.
Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13     muwawononge mu ukali (wanu)
    muwawononge mpaka atheretu.
Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi
    kuti Mulungu amalamulira Yakobo.

14 Iwo amabweranso madzulo,
    akuchita phokoso ngati agalu
    ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya
    ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu,
    mmawa ndidzayimba zachikondi chanu;
pakuti ndinu linga langa,
    pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.

17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu;
    Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.

Yesaya 9:8-10:4

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo;
    ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
Anthu onse okhala mu
    Efereimu ndi okhala mu Samariya,
adzadziwa zimenezi.
    Iwo amayankhula modzikuza kuti,
10 “Ngakhale njerwa zagumuka,
    koma ife tidzamanga ndi miyala yosema.
Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa,
    koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
11 Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo
    ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
12 Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo
    ayasama pakamwa kuti adye a Israeli.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

13 Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja,
    ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
14 Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe,
    nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
15 mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka,
    mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
16 Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa,
    ndipo otsogoleredwa amatayika.
17 Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata,
    ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye,
pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo
    aliyense amayankhula zopusa.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

18 Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto;
    moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga,
umayatsa nkhalango yowirira,
    ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
19 Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse,
    dziko lidzatenthedwa
ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto;
    palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya,
    koma adzakhalabe ndi njala;
kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya,
    koma sadzakhuta.
Aliyense azidzadya ana ake omwe.
21     Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase;
    onsewa pamodzi adzadya Yuda.

Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

10 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo,
    kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
kuwalanda anthu osauka ufulu wawo
    ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga,
amalanda zinthu za akazi amasiye
    ndi kubera ana amasiye.
Kodi mudzatani pa tsiku la chilango,
    pofika chiwonongeko chochokera kutali?
Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni?
    Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa
    kapena kufa pamodzi ndi ophedwa.
Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

Yakobo 3

Za Lilime

Abale anga, ambiri musakhale aphunzitsi chifukwa mumadziwa kuti aphunzitsife tidzaweruzidwa mowuma kuposa anthu ena onse. Tonsefe timapunthwa mʼnjira zambiri. Ngati wina salakwa poyankhula, ameneyo ndi munthu wangwiro, wodziwa kuyangʼanira bwino thupi lake lonse.

Tikayika tizitsulo mʼkamwa mwa akavalo kuti atimvere, timatha kuwongolera thupi lake lonse. Taonani sitima zapamadzi. Ngakhale ndi zazikulu kwambiri ndipo zimakankhidwa ndi mphepo yamphamvu, zimawongoleredwa ndi tsigiro lalingʼono kulikonse kumene woyendetsayo akufuna kupita. Momwemonso, lilime ndi kachiwalo kakangʼono ka thupi koma limadzitama kuti nʼkuchita zikuluzikulu. Tangoganizirani za nkhalango yayikulu imene ingapse ndi kalawi kamoto koyamba mochepa. Lilime nalonso ndi moto, dziko la zoyipa pakati pa ziwalo za thupi. Limawononga munthu yense wathunthu. Limayika zonse za moyo wake pa moto, ndipo moto wake ndi wochokera ku gehena.

Mitundu yonse ya nyama, ya mbalame, ya zokwawa ndi ya zolengedwa za mʼnyanja, zikuwetedwa ndipo munthu wakhala akuziweta, koma palibe munthu amene angaweta lilime. Lilime ndipo silitha kupuma, ndi lodzaza ndi ululu wakupha.

Ndi lilime lomwelo timatamanda Ambuye ndi Atate athu, komanso ndi lilime lomwelo timalalatira anthu, amene anapangidwa mʼchifanizo cha Mulungu. 10 Mʼkamwa momwemo mutuluka matamando ndi kulalata. Abale anga, zisamatero ayi. 11 Kodi madzi abwino ndi a mchere angatuluke pa kasupe mmodzi? 12 Abale anga, kodi mtengo wa mkuyu nʼkubala mphesa, kapena mtengo wampesa nʼkubala nkhuyu? Kasupe wa madzi a mchere sangatulutsenso madzi abwino.

Mitundu Iwiri ya Nzeru

13 Ndani mwa inu amene ndi wanzeru ndi womvetsa zinthu? Mulekeni aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru ndiye zikutsogolera kudzichepetsa kwake ndi zochita zake 14 Koma ngati muli ndi mtima wakaduka ndi odzikonda, musadzitamandire kapena kukana choonadi. 15 “Nzeru” zotere sizochokera kumwamba koma ndi za mʼdziko lapansi, si zauzimu koma ndi za ziwanda. 16 Pakuti pamene pali kaduka ndi kudzikonda pomweponso pamakhala chisokonezo ndi zochitika zoyipa zonse.

17 Koma nzeru imene imachoka kumwamba, poyamba ndi yangwiro, ndi yokonda mtendere, yoganizira za ena, yogonjera, yodzaza ndi chifundo ndi chipatso chabwino, yosakondera ndi yoona mtima. 18 Anthu amtendere amene amadzala mtendere amakolola chilungamo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.