M’Cheyne Bible Reading Plan
Za Nyale
8 Yehova anawuza Mose kuti, 2 “Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
3 Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose. 4 Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
Za Kupatulidwa kwa Alevi
5 Yehova anawuza Mose kuti, 6 “Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse. 7 Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse. 8 Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo. 9 Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli. 10 Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo. 11 Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
12 “Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi. 13 Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova. 14 Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
15 “Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano. 16 Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi. 17 Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini. 18 Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli. 19 Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
20 Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose. 21 Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa. 22 Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
23 Yehova anawuza Mose kuti, 24 “Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano. 25 Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo. 26 Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.
44 Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;
makolo athu atiwuza
zimene munachita mʼmasiku awo,
masiku akalekalewo.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena
ndi kudzala makolo athu;
Inu munakantha mitundu ya anthu,
koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo,
si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,
koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,
pakuti munawakonda.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga
amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;
kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 Sindidalira uta wanga,
lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu,
mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,
ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;
Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani
ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa
ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,
osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,
chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;
anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse
ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,
chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Zonsezi zinatichitikira
ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu
kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;
mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe
ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu
kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,
pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,
tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!
Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,
ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;
matupi athu amatirira pa dothi.
26 Imirirani ndi kutithandiza,
tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Abwenzi
6 Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,
kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti?
Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti
kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?
Mkazi
2 Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake,
ku timinda ta zokometsera zakudya,
akukadyetsa ziweto zake ku minda,
ndiponso akuthyola maluwa okongola.
3 Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga;
amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.
Mwamuna
4 Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza,
wokongola kwambiri ngati Yerusalemu,
ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.
5 Usandipenyetsetse;
pakuti maso ako amanditenga mtima.
Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi
zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
6 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa
zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa,
iliyonse ili ndi ana amapasa,
palibe imene ili yokha.
7 Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu,
masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.
8 Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60,
ndi azikazi 80,
ndi anamwali osawerengeka;
9 koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense;
mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake,
mwana wapamtima wa amene anamubereka.
Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala;
akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.
Abwenzi
10 Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha,
wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa,
wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?
Mwamuna
11 Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi
kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa,
kukaona ngati mpesa waphukira
kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.
12 Ndisanazindikire kanthu,
ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.
Abwenzi
13 Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami;
bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe!
Mwamuna
Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami,
pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?
6 Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu, 2 za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. 3 Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.
4 Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera. 5 Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. 6 Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.
7 Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa. 8 Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.
9 Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso. 10 Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano. 11 Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera. 12 Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.
Kukhazikika kwa Malonjezo a Mulungu
13 Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti, 14 “Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.” 15 Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.
16 Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse. 17 Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro. 18 Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira. 19 Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga. 20 Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.