Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

M’Cheyne Bible Reading Plan

The classic M'Cheyne plan--read the Old Testament, New Testament, and Psalms or Gospels every day.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Oweruza 5

Nyimbo ya Debora

“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:

“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;
    ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,
    tamandani Yehova:

“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!
    Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,
    Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.

“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,
    pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,
dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka
    nigwetsa madzi.
Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,
    Mulungu wa Israeli.

“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,
    pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;
    alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi
    mpaka pamene iwe Debora unafika;
    unafika ngati mayi ku Israeli.
Pamene anasankha milungu ina,
    nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,
ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke
    pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,
    uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.
    Tamandani Yehova!

10 “Inu okwera pa abulu oyera,
    okhala pa zishalo,
    ndi inu oyenda pa msewu,
yankhulani. 11 Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;
    kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;
    akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.

“Choncho anthu a Yehova
    anasonkhana ku zipata za mzinda.
12 Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera;
    tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo.
Iwe Baraki! nyamuka
    Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’

13 “Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo;
    anthu a Yehova anapita
kukamenyera Yehova nkhondo
    kulimbana ndi adani amphamvu.
14 Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu;
    akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako.
Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri,
    ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
15 Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora;
    inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki,
    ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira.
Koma pakati pa mafuko a Rubeni
    panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
16 Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera
    zitoliro zoyitanira nkhosa?
Pakati pa anthu a fuko la Rubeni
    panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
17 Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani.
    Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi?
Aseri anali pa gombe la Nyanja;
    anangokhala mʼmadooko mwawo.
18 Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa.
    Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.

19 “Mafumu anabwera, anachita nkhondo;
    mafumu Akanaani anachita nkhondo
ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido,
    koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
20 Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo,
    zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
21 Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,
    chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola.
    Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
22 Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu,
    akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
23 Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’
    ‘Tembererani nzika zake mwaukali,
chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova,
    kulimbana ndi adani ake amphamvu.’

24 “Akhale wodala kupambana akazi onse,
    Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni;
    inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
25 Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka;
    anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
26 Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake,
    anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja.
Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake,
    ndi kumubowola mu litsipa mwake.
27 Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa,
    anagwa; iye anagona pamenepo.
Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa;
    pamene anagwera, pamenepo anaferapo.

28 “Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera;
    nafuwula mokweza kuti,
‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika?
    Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
29 Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha,
    ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
30 ‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane;
    akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri.
    Sisera akumupatsa zofunkha:
    zovala zonyikidwa mu utoto,
    zoti ndizivala mʼkhosi
zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’

31 “Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke,
    koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa
    pamene lituluka ndi mphamvu zake.”

Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.

Machitidwe a Atumwi 9

Kutembenuka Mtima kwa Saulo

Pa nthawi imeneyi, Saulo ankaopsezabe okhulupirira Ambuye nafuna kuwapha. Iye anapita kwa mkulu wa ansembe, ndi kukapempha makalata a chilolezo kuti apite nawo ku masunagoge a ku Damasiko, kuti ngati atakapezeka ena kumeneko otsata Njirayo, kaya ndi amuna kapena amayi, akawamange ndi kuwatenga kubwera nawo ku Yerusalemu. Akuyandikira ku Damasikoku paulendo wake, mwadzidzidzi kuwala kochokera kumwamba kunamuzungulira iye. Iye anagwa pansi ndipo anamva mawu akuti, “Saulo, Saulo ukundizunziranji Ine?”

Saulo anafunsa kuti, “Ndinu yani Ambuye?”

Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu amene iwe ukumuzunza.” “Tsopano dzuka, lowa mu mzindamo, ndipo udzawuzidwa zoyenera kuchita.”

Anthu amene anali naye paulendo, anasowa chonena; iwo anamva mawu koma sanaone wina aliyense. Saulo anayimirira, ndipo pamene anatsekula maso ake sanathe kuona. Kotero anamugwira dzanja ndi kulowa naye mu Damasiko. Anakhala wosaona kwa masiku atatu ndiponso sanadye kapena kumwa kanthu kalikonse.

10 Ku Damasiko kunali wophunzira wina dzina lake Hananiya. Ambuye anamuyitana mʼmasomphenya kuti, “Hananiya!”

Iye anayankha kuti, “Ine Ambuye.”

11 Ambuye anamuwuza iye kuti, “Nyamuka, pita ku nyumba ya Yudasi imene ili pa Njira Yolunjika ndipo ukafunse za munthu wochokera ku Tarisisi dzina lake Saulo, pakuti akupemphera. 12 Ndipo waona mʼmasomphenya munthu, dzina lake Hananiya atabwera ndi kumusanjika manja kuti aonenso.”

13 Hananiya anayankha kuti, “Ambuye, ndinamva zambiri za munthu uyu ndi zonse zoyipa anachitira oyera mtima a ku Yerusalemu. 14 Ndipo wabwera kuno ndi ulamuliro wa akulu ansembe kuti adzamange onse amene amayitana pa dzina lanu.”

15 Koma Ambuye anati kwa Hananiya, “Pita! Munthu uyu ndi chida changa chosankhika chonyamulira dzina langa pamaso pa anthu a mitundu ina ndi mafumu awo ndiponso kwa anthu a Israeli. 16 Ine ndidzamuonetsa zowawa zonse zimene ayenera kumva chifukwa cha dzina langa.”

17 Pamenepo Hananiya ananyamuka ndi kukalowa mʼnyumbayo. Anamusanjika manja Sauloyo ndipo anati, “Mʼbale Saulo, Ambuye Yesu, amene anakuonekera pa msewu pamene umabwera kuno wandituma kuti uwonenso ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.” 18 Nthawi yomweyo mʼmaso mwa Saulo munachoka zinthu zokhala ngati mamba ansomba, ndipo anayambanso kuona. Iye anayimirira nabatizidwa, 19 ndipo atadya chakudya, anapezanso mphamvu.

Saulo Alalikira ku Damasiko

Saulo anakhala masiku angapo ndi ophunzira a ku Damasiko. 20 Posakhalitsa anayamba kulalikira mʼsunagoge kuti Yesu ndiye Mwana wa Mulungu. 21 Onse amene anamva iye akulalikira anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene anayambitsa kuzunza okhulupirira ku mpingo wa ku Yerusalemu? Kodi siwabwera kuno kuti awamange ndi kuwapereka kwa akulu a ansembe?” 22 Koma mphamvu za Saulo zinali kukulirakulira ndipo anathetsa nzeru Ayuda okhala ku Damasiko powatsimikizira kuti Yesu ndi Mpulumutsi.

23 Patapita masiku ambiri, Ayuda anapangana zoti aphe Saulo, 24 koma iye anadziwa za chiwembucho. Anthu ankadikirira usana ndi usiku pa zipata za mzindawo kuti amuphe. 25 Koma ophunzira ake anamutenga usiku, namutsitsira kunja kwa mpandawo mʼdengu.

Saulo ku Yerusalemu

26 Saulo atafika ku Yerusalemu, anayesetsa kulowa mʼgulu la ophunzira koma onse anamuopa chifukwa sanakhulupirire kuti anali wophunziradi. 27 Koma Barnaba anamutenga napita naye kwa atumwi. Iye anawafotokozera iwo za mmene Saulo anaonera Ambuye pa njira paja, ndi kuti Ambuye anamuyankhula, ndi momwe analalikira ku Damasiko mʼdzina la Yesu mosaopa. 28 Kotero Saulo anakhala nawo nayendayenda mwaufulu mu Yerusalemu akulalikira molimba mtima mʼdzina la Ambuye. 29 Anayankhula ndi kutsutsana ndi Ayuda a Chihelene, koma iwo ankafuna kumupha. 30 Abale atadziwa zimenezi, anamutenga Saulo ndi kupita naye ku Kaisareya, ndipo anamutumiza ku Tarisisi.

31 Pamenepo mpingo wa ku Yudeya konse, ku Galileya ndi ku Samariya unakhala pamtendere, unalimbikitsidwa; ndi kupatsidwa mphamvu ndi Mzimu Woyera, unakula mʼchiwerengero, ndi kukhala moopa Ambuye.

Eneya ndi Tabita

32 Pamene Petro amayendera mpingo, anapita kukachezera oyera mtima a ku Luda. 33 Kumeneko anakapeza munthu dzina lake Eneya, wofa ziwalo amene anagona pa mphasa kwa zaka zisanu ndi zitatu. 34 Petro anati kwa iye, “Eneya, Yesu Khristu akukuchiritsa iwe, dzuka ndipo yalula mphasa yako.” Nthawi yomweyo Eneya anayimirira. 35 Anthu onse amene anakhala ku Luda ndi ku Sharoni anamuona ndipo anatembenukira kwa Ambuye.

36 Ku Yopa kunali wophunzira wina dzina lake Tabita (mʼChigriki amati Dorika) amene nthawi zonse ankachita zachifundo ndiponso kuthandiza osauka. 37 Nthawi imeneyi anadwala ndipo anamwalira, anasambitsa thupi lake, namugoneka mʼchipinda chammwamba. 38 Popeza ku Yopa kunali pafupi ndi Luda; pamene ophunzira anamva kuti Petro anali ku Luda, anatuma anthu awiri kuti akamudandaulire kuti, “Chonde bwerani kuno msanga!”

39 Petro ananyamuka, napita nawo, ndipo atafika anamutengera ku chipinda chammwamba. Amasiye onse anayima momuzungulira akulira ndi kumuonetsa mwinjiro ndi zovala zina zimene Dorika ankapanga akanali moyo.

40 Petro anatulutsa anthu onse mʼchipindamo; ndipo anagwada pansi ndi kupemphera. Anatembenukira mtembo uja nati, “Tabita, dzuka,” Tabita anatsekula maso ake, ndipo ataona Petro anakhala pansi. 41 Petro anamugwira dzanja, namuyimiritsa. Ndipo anayitana okhulupirira ndi amasiye namupereka wamoyo. 42 Zimenezi zinadziwika ku Yopa konse, ndipo anthu ambiri anakhulupirira Ambuye. 43 Petro anakhala ku Yopa kwa masiku ambiri kwa munthu wina, dzina lake Simoni, mmisiri wa zikopa.

Yeremiya 18

Ku Nyumba ya Wowumba Mbiya

18 Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.” Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero. Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.

Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya. Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga, ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira. Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu. 10 Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.

11 “Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’ 12 Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’ ”

13 Yehova akuti,

“Uwafunse anthu a mitundu ina kuti:
    Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi?
Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita
    chinthu choopsa kwambiri.
14 Kodi chisanu chimatha pa matanthwe
    otsetsereka a phiri la Lebanoni?
Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera
    ku phiri la Lebanoni adzamphwa?
15 Komatu anthu anga andiyiwala;
    akufukiza lubani kwa mafano achabechabe.
Amapunthwa mʼnjira
    zawo zakale.
Amayenda mʼnjira zachidule
    ndi kusiya njira zabwino.
16 Dziko lawo amalisandutsa chipululu,
    chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse;
onse odutsapo adzadabwa kwambiri
    ndipo adzapukusa mitu yawo.
17 Ngati mphepo yochokera kummawa,
    ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo;
ndidzawafulatira osawathandiza
    pa tsiku la mavuto awo.”

18 Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”

19 Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni;
    imvani zimene adani anga akunena za ine!
20 Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino?
    Komabe iwo andikumbira dzenje.
Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu
    kudzawapempherera
    kuti muwachotsere mkwiyo wanu.
21 Choncho langani ana awo ndi njala;
    aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga.
Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye;
    amuna awo aphedwe ndi mliri,
    anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.
22 Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo
    mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe.
Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo
    ndipo atchera msampha mapazi anga.
23 Koma Inu Yehova, mukudziwa
    ziwembu zawo zonse zofuna kundipha.
Musawakhululukire zolakwa zawo
    kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu.
Agonjetsedwe pamaso panu;
    muwalange muli wokwiya.”

Marko 4

Fanizo la Wofesa Mbewu

Nthawi inanso Yesu atakhala mʼmbali mwa nyanja, anayamba kuphunzitsa. Gulu lalikulu la anthu linasonkhana momuzungulira kotero kuti Iye analowa mʼbwato lomwe linali pa nyanja nakhalamo, anthu onse ali pa mtunda mʼmbali mwa madzi. Anawaphunzitsa zinthu zambiri mʼmafanizo, ndipo mʼchiphunzitso chake anati: “Tamverani! Mlimi anapita kukafesa mbewu zake. Akufesa, mbewu zina zinagwera mʼmbali mwa njira, ndipo mbalame zinabwera ndi kuzidya. Zina zinagwa pa malo a miyala pamene panalibe dothi lambiri. Zinamera mofulumira chifukwa panalibe dothi lambiri. Koma dzuwa litakwera, mbewuzo zinapserera, ndipo zinawuma chifukwa zinalibe mizu. Mbewu zina zinagwa pa minga, ndipo mingayo inayanga ndi kuzirepheretsa kukula. Mbewu zinanso zinagwa pa nthaka yabwino ndipo zinamera, zinakula ndi kubereka zipatso, zina zochuluka makumi atatu, zina makumi asanu ndi limodzi ndi zina 100.”

Pamenepo Yesu anati, “Amene ali ndi makutu akumva, amve.”

10 Ali yekha, ophunzira ndi ena omuzungulira, anamufunsa za mafanizo. 11 Iye anawawuza kuti, “Chinsinsi cha ufumu wa Mulungu chapatsidwa kwa inu. Koma kwa amene ali kunja zinthu zonse zinenedwa mʼmafanizo: 12 kotero kuti,

“ ‘Kupenya mudzapenya koma osaona kanthu,
    kumva mudzamva koma osamvetsetsa,
kuti mwina angatembenuke ndi kukhululukidwa!’ ”

13 Pamenepo Yesu anawawuza kuti, “Kodi simukulimvetsa fanizoli? Kodi nanga mudzazindikira bwanji fanizo lina lililonse? 14 Wofesa amafesa mawu. 15 Anthu ena ali ngati mbewu za mʼmbali mwa njira, mʼmene mawu amafesedwamo. Akangowamva, Satana amabwera ndi kuchotsa mawu amene anafesedwa mwa iwo. 16 Ena, monga mbewu zofesedwa pa miyala, amamva mawu ndipo nthawi yomweyo amawalandira ndi chimwemwe. 17 Koma popeza alibe mizu, amakhala kwa kanthawi kochepa. Mavuto kapena masautso akafika chifukwa cha mawu, amagwa mofulumira. 18 Komabe ena, monga mbewu zofesedwa pakati pa minga, amamva mawu; 19 koma nkhawa zamoyo uno, chinyengo cha chuma ndi zokhumba za zinthu zina zimabwera ndi kutchinga mawu, ndipo amawachititsa kukhala osabala chipatso. 20 Ena, ngati mbewu zofesedwa pa nthaka yabwino, amamva mawu, nawalandira, ndi kubereka zipatso zokwanira makumi atatu, makumi asanu ndi limodzi, kapena ngakhale 100 kuwonjezera pa zomwe zinafesedwa.”

Fanizo la Nyale

21 Iye anawawuza kuti, “Kodi umatenga nyale ndi kuyiika pansi pa mbiya kapena pansi pa bedi? Mʼmalo mwake, kodi simuyika pa choyikapo chake? 22 Pakuti chilichonse chobisika chidzayenera kuwululika, ndi chilichonse chachinsinsi chidzayenera kuonekera poyera. 23 Ngati wina ali ndi makutu akumva, amve.”

24 Anapitiriza nati, “Ganizirani mosamala zimene mukumva, ndi muyeso umene mugwiritsa ntchito, mudzayesedwa nawo, ndipo ngakhale kwambiri. 25 Amene ali nazo adzapatsidwa zochuluka; amene alibe, ngakhale zimene ali nazo zidzachotsedwa kwa iwo.”

Fanizo la Mbewu Imene Ikukula

26 Iye anatinso, “Umu ndi mmene ulili ufumu wa Mulungu. Munthu amafesa mbewu mʼnthaka. 27 Usiku ndi usana, kaya agona kapena adzuka, mbewu imamera ndi kukula, ngakhale sadziwa mmene zimachitikira. 28 Nthaka pa yokha imatulutsa mbewu, umayamba mʼmera, kenaka ngala, kenaka mbewu yokhwima mʼngalayo. 29 Mbewuyo ikangokhwima, amayimweta chifukwa nthawi yokolola yakwana.”

Fanizo la Mbewu ya Mpiru

30 Ndipo anatinso, “Kodi tinene kuti ufumu wa Mulungu ufanana ndi chiyani, kapena ndi fanizo lotani limene tidzagwiritsa ntchito pakuwufotokozera? 31 Uli ngati mbewu ya mpiru imene ndi mbewu yayingʼono kwambiri yomwe mumadzala mʼnthaka. 32 Koma ikadzalidwa, imakula ndi kukhala yayikulu koposa mbewu zina zonse za mʼmunda ndipo mʼnthambi zake zazikulu mbalame zamlengalenga zimadzapuma pa mthunzi wake.”

33 Ndi mafanizo ambiri onga awa Yesu anayankhula mawu kwa iwo, monga mmene akanatha kumvetsa. 34 Iye sananene kanthu kwa iwo osagwiritsa ntchito fanizo. Koma ali yekha ndi ophunzira ake, ankawatanthauzira zonse.

Yesu Aletsa Namondwe

35 Tsiku limenelo atafika madzulo, anawuza ophunzira ake kuti, “Tiyeni tiwolokere tsidya lina.” 36 Atasiya gulu la anthu mʼmbuyo, anamutenga Iye, napita naye monga momwe anali mʼbwatolo. Panalinso mabwato ena pamodzi ndi Iye. 37 Mphepo yamkuntho inabuka, ndipo mafunde anawomba bwatolo, kotero kuti linali pafupi kumira. 38 Pa nthawi imeneyi Yesu anali akugona atatsamira pilo kumbuyo kwa bwato. Ophunzira anamudzutsa nati kwa Iye, “Aphunzitsi, kodi simukusamala kuti timira?”

39 Yesu anauka nadzudzula mphepo nati kwa mafunde, “Chete! Khala bata!” Pamenepo mphepo inaleka ndipo kunachita bata.

40 Iye anati kwa ophunzira ake, “Muli ndi mantha chifukwa chiyani? Kodi mukanalibe chikhulupiriro?”

41 Iwo anachita mantha nafunsana wina ndi mnzake kuti, “Uyu ndani? Ngakhale mphepo ndi nyanja zimumvera Iye!”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.