Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

M’Cheyne Bible Reading Plan

The classic M'Cheyne plan--read the Old Testament, New Testament, and Psalms or Gospels every day.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Numeri 3

Alevi

Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.

Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara. Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe. Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.

Yehova anati kwa Mose, “Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira. Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema. Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti. Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu. 10 Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”

11 Yehova anawuzanso Mose kuti, 12 “Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga, 13 pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”

14 Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti, 15 “Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.” 16 Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.

17 Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa:

Geresoni, Kohati ndi Merari.

18 Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa:

Libini ndi Simei.

19 Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa:

Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.

20 Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa:

Mali ndi Musi.

Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.

21 Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni. 22 Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500. 23 Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema. 24 Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli. 25 Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano, 26 ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.

27 Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati. 28 Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika. 29 Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema. 30 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli. 31 Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito. 32 Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.

33 Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari. 34 Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200. 35 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema. 36 Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito, 37 pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.

38 Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.

39 Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.

40 Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo. 41 Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”

42 Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira. 43 Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.

44 Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti, 45 “Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova. 46 Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi, 47 utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri. 48 Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”

49 Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi. 50 Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli. 51 Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.

Masalimo 37

Salimo la Davide.

37 Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa
    kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga,
    ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.

Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino;
    khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova
    ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.

Pereka njira yako kwa Yehova;
    dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha,
    chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.

Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa;
    usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo,
    pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.

Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali,
    usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa,
    koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.

10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso;
    ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko
    ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.

12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama
    ndipo amawakukutira mano;
13 koma Ambuye amaseka oyipa
    pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.

14 Oyipa amasolola lupanga
    ndi kupinda uta
kugwetsa osauka ndi osowa,
    kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe,
    ndipo mauta awo anathyoka.

16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo
    ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka,
    koma Yehova amasunga olungama.

18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova,
    ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota;
    mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.

20 Koma oyipa adzawonongeka;
    adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo,
    iwo adzazimirira ngati utsi.

21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza
    koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko,
    koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.

23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu,
    amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa,
    pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.

25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba
    koma sindinaonepo olungama akusiyidwa
    kapena ana awo akupempha chakudya.
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu;
    ana awo adzadalitsika.

27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;
    pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama
    ndipo sadzasiya okhulupirika ake.

Iwo adzatetezedwa kwamuyaya,
    koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 olungama adzalandira dziko
    ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.

30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru,
    ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake;
    mapazi ake saterereka.

32 Oyipa amabisala kudikira olungama;
    kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo
    kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.

34 Khulupirira Yehova,
    ndipo sunga njira yake;
Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako;
    udzaona anthu oyipa akuwonongeka.

35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo
    akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso;
    ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.

37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama;
    udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka;
    iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.

39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova;
    Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa;
    Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa,
    pakuti amathawira kwa Iye.

Nyimbo ya Solomoni 1

Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.

Mkazi

Undipsompsone ndi milomo yako
    chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;
    dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.
    Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!
    Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.

Abwenzi

Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,
    tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.

Mkazi

Amachita bwinotu potamanda iwe!

Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,
    inu akazi a ku Yerusalemu,
    ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,
    ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,
    ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.
Alongo anga anandikwiyira
    ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;
    munda wangawanga sindinawusamalire.
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako
    ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.
Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere
    pambali pa ziweto za abwenzi ako?

Abwenzi

Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,
    ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa
ndipo udyetse ana ambuzi
    pambali pa matenti a abusa.

Mwamuna

Iwe bwenzi langa,
    uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,
    khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide
    zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.

Mkazi

12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,
    mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,
    kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,
    ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.

Mwamuna

15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!
    Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,
    maso ako ali ngati nkhunda.

Mkazi

16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!
    Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!
    Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.

Mwamuna

17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,
    phaso lake ndi la mtengo wa payini.

Ahebri 1

Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo

Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.

Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,

“Iwe ndiwe mwana wanga;
    Ine lero ndakhala Atate ako.”

Kapena kunenanso kuti,

“Ine ndidzakhala abambo ake;
    iye adzakhala mwana wanga.”

Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,

“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”

Iye ponena za angelo akuti,

“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,
    amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”

Koma za Mwana wake akuti,

“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,
    ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.
Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;
    Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu
    pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”

10 Mulungu akutinso,

“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;
    ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.
11 Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.
    Izo zidzatha ngati zovala.
12 Mudzazipindapinda ngati chofunda;
    ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.
Koma Inu simudzasintha,
    ndipo zaka zanu sizidzatha.”

13 Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,

“Khala kudzanja langa lamanja
    mpaka nditapanga adani ako
    kukhale chopondapo mapazi ako.”

14 Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.