M’Cheyne Bible Reading Plan
Mwambo Wodzoza Aaroni ndi Ana Ake
8 Yehova anawuza Mose kuti, 2 “Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti, 3 ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.” 4 Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
5 Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.” 6 Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi. 7 Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo. 8 Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu. 9 Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
10 Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula. 11 Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula. 12 Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula. 13 Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo. 15 Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo. 16 Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo. 17 Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
18 Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake. 19 Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo. 20 Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta. 21 Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
22 Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake. 23 Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja. 24 Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo. 25 Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja. 26 Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija. 27 Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula. 28 Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova. 29 Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
30 Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
31 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’ 32 Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche. 33 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri. 34 Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu. 35 Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.” 36 Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide.
9 Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse;
ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu;
Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 Adani anga amathawa,
iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga;
Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa;
Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani,
mwafafaniza mizinda yawo;
ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 Yehova akulamulira kwamuyaya;
wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo;
adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima,
linga pa nthawi ya mavuto.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu,
pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni;
lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira;
Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira!
Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 kuti ndilengeze za matamando anu
pa zipata za ana aakazi a Ziyoni,
kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba;
mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake;
oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo.
Higayoni. Sela
17 Oyipa amabwerera ku manda,
mitundu yonse imene imayiwala Mulungu.
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse,
kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane;
mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova;
mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba.
Sela
23 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira,
uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 ngati ndiwe munthu wadyera
udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Usasirire zakudya zake,
pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma,
ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo.
Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi
ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo,
usalakalake zakudya zake zokoma;
7 paja iye ndi munthu amene
nthawi zonse amaganizira za mtengo wake
ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,”
koma sakondweretsedwa nawe.
8 Udzasanza zimene wadyazo
ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva,
pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale
kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu;
iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo
ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Usaleke kumulangiza mwana;
ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa
udzapulumutsa moyo wake.
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru,
inenso mtima wanga udzakondwera.
16 Mtima wanga udzakondwera
pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa,
koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo
ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru,
mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera
kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi
ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Mvera abambo ako amene anakubala,
usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse;
ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu;
Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale;
amene anakubereka akondwere!
26 Mwana wanga, undikhulupirire
ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama;
ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba,
ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni?
Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo?
Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa,
amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo,
pamene akuwira mʼchikho
pamene akumweka bwino!
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka,
ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo
ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja,
kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe!
Andimenya koma sindinamve kanthu!
Kodi ndidzuka nthawi yanji?
Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
Utumiki wa Paulo ku Atesalonika
2 Abale, mukudziwa kuti kudzacheza kwathu kwa inu sikunali kosapindulitsa. 2 Monga mukudziwa, ife nʼkuti titazunzika ndi kunyozedwa ku Filipi. Koma mothandizidwa ndi Mulungu wathu, tinalimba mtima mpaka kukulalikirani uthenga wake wabwino ngakhale ambiri ankatsutsana nafe. 3 Pakuti kulalikira kumene tikuchita, sitikuchita ndi maganizo olakwika kapena zolinga zoyipa, kapenanso kufuna kukunamizani. 4 Koma timayankhula monga anthu ovomerezeka ndi Mulungu ndi osungitsidwa Uthenga Wabwino. Ife sitikufuna kukondweretsa anthu koma Mulungu, amene amasanthula mitima yathu. 5 Monga mukudziwa kuti sitinagwiritse ntchito mawu oshashalika kapena mtima wofuna phindu, Mulungu ndiye mboni yathu. 6 Ife sitinafune kutamidwa ndi anthu, kapena ndi inu, kapena wina aliyense mwa inu. 7 Ngati atumwi a Khristu tikanatha kukhala cholemetsa kwa inu, mʼmalo mwake tinali ngati ana aangʼono pakati panu.
Monga mmene amayi amasamalira ana awo angʼono, 8 moteronso tinakusamalirani. Chifukwa tinakukondani kwambiri, tinali okondwa kugawana nanu osati Uthenga Wabwino wa Mulungu wokha, komanso miyoyo yathu. 9 Abale, pakuti mukumbukira kugwira ntchito kwathu kwambiri ndi kuvutika; ife tinagwira ntchito usana ndi usiku ndi cholinga chakuti tisakhale cholemetsa, kwa aliyense pamene ife tinkalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu kwa inu.
10 Inu ndinu mboni, ndiponso Mulungu, kuti tinali oyera mtima, olungama ndi wopanda chifukwa pakati panu amene munakhulupirira. 11 Monga mudziwa kuti ife tinkasamala aliyense wa inu monga abambo amasamalira ana ake, 12 kulimbikitsa, kutonthoza ndi kukupemphani kuti mukhale moyo oyenera Mulungu amene anakuyitanani kuti mulowe mu ufumu wake ndi ulemerero.
13 Ndipo ifenso tikuyamika Mulungu kosalekeza chifukwa mutalandira Mawu a Mulungu, amene munawamva kuchokera kwa ife, munawalandira osati ngati mawu a anthu, koma monga momwe alili, Mawu a Mulungu, amene akugwira ntchito mwa inu amene mukhulupirira. 14 Pakuti inu abale, munakhala otsanzira mipingo ya Mulungu ya ku Yudeya, imene ili mwa Khristu Yesu. Munasautsidwa kuchokera kwa anthu a mtundu wanu, zinthu zomwezo zimene mipingo imeneyi inasautsidwa ndi Ayuda, 15 amene anapha Ambuye Yesu ndi aneneri ndipo anatithamangitsanso ife. Iwo sakondweretsa Mulungu ndipo amadana ndi anthu onse 16 ndikutiretsa ife kuti tisayankhule ndi a mitundu ina kuti angapulumuke. Motero iwo amadziwunjikira okha machimo awo. Mkwiyo wa Mulungu wa afikira tsopano.
Paulo Afunitsitsa Kuonanso Atesalonika
17 Koma abale, titasiyana kwa nthawi pangʼono (mʼthupi osati mʼmaganizo), tinayesetsa koposa kuti tikuoneni. 18 Pakuti ife tinafuna kubweranso kwa inu, makamaka ine Paulo, ndinayesa kangapo koma Satana anatiletsa. 19 Nanga chiyembekezo chathu, chimwemwe chathu kapena chaufumu chimene ife tidzanyadira pamaso pa Ambuye athu Yesu Khristu pamene abwere ndi chiyani? Kodi si inu? 20 Indedi, inu ndinu ulemerero wathu ndi chimwemwe.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.