Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

M’Cheyne Bible Reading Plan

The classic M'Cheyne plan--read the Old Testament, New Testament, and Psalms or Gospels every day.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Eksodo 40

Adzutsa Chihema

40 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Imika chihema, tenti ya msonkhano, tsiku loyamba la mwezi. Uyikemo bokosi la umboni ndipo uphimbe bokosilo ndi katani. Ulowetsemo tebulo ndi kuyika zimene zimakhala pamenepo. Kenaka ulowetse choyikapo nyale ndipo uyikepo nyale zake. Uyike guwa lofukiza la golide patsogolo pa bokosi la umboni ndipo uyike katani ya pa chipata cha chihema.

“Uyike guwa lansembe yopsereza patsogolo pa chipata cha chihema, tenti ya msonkhano. Uyike beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo uyikemo madzi. Upange bwalo lozungulira chihemacho ndipo uyike katani ya pa chipata cha bwalolo.

“Utenge mafuta wodzozera ndipo udzoze chihema ndi chilichonse chili mʼmenemo ndipo zidzakhala zoyeretsedwa. 10 Kenaka udzoze guwa lansembe lopsereza ndi ziwiya zake zonse. Ulipatule guwalo ndipo lidzakhala loyera kwambiri. 11 Udzoze beseni ndi miyendo yake ndipo uzipatule.

12 “Ubwere ndi Aaroni ndi ana ake pa chipata cha tenti ya msonkhano ndipo uwasambitse ndi madzi. 13 Kenaka umuveke Aaroni zovala zopatulika, umudzoze ndi kumupatula kotero kuti athe kunditumikira monga wansembe. 14 Ubweretse ana ake ndipo uwaveke minjiro. 15 Uwadzoze monga momwe unadzozera abambo awo, kotero kuti anditumikire monga ansembe. Kudzozedwako kudzakhala unsembe wawo pa mibado ndi mibado” 16 Mose anachita zonse monga Yehova anamulamulira.

17 Kotero anayimika chihema tsiku loyamba la mwezi woyamba mʼchaka chachiwiri. 18 Nthawi imene Mose anayimika chihema, anayika matsinde mʼmalo ake, kuyimitsa maferemu, kulowetsa mitanda ndi kuyika nsichi. 19 Kenaka anayika tenti pamwamba pa chihema ndipo anayika chophimba pa tenti monga momwe Yehova analamulira Mose.

20 Iye anatenga miyala ya umboni nayika mʼbokosi lija ndi kuyika chivundikiro pamwamba pake. 21 Kenaka analowetsa bokosilo mʼchihema ndipo anapachika katani ndi kubisa bokosi la umboni monga momwe Yehova analamulira iye.

22 Mose anayika tebulo mu tenti ya msonkhano kumpoto kwa chihema, kunja kwa katani, 23 ndipo anayikapo buledi pamaso pa Yehova, monga momwe Yehova analamulira Mose.

24 Iye anayikanso choyikapo nyale mu tenti ya msonkhano moyangʼanana ndi tebulo mbali yakummwera kwa chihema. 25 Ndipo anayikapo nyale zija pamaso pa Yehova, monga Yehova analamulira Mose.

26 Mose anayika guwa la golide mu tenti ya msonkhano patsogolo pa katani 27 ndipo anapserezapo lubani wonunkhira monga Yehova anamulamulira. 28 Kenaka anayika katani ya pa chipata cha chihema.

29 Iye anayika guwa lansembe yopsereza pafupi ndi chipata cha chihema, tenti ya msonkhano, ndipo anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya ufa monga Yehova anamulamulira.

30 Iye anayika beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo anathiramo madzi wosamba, 31 ndipo Mose, Aaroni ndi ana ake amasamba manja ndi mapazi awo. 32 Iwo amasamba nthawi zonse akamalowa mu tenti ya msonkhano kapena kuyandikira guwa lansembe monga Yehova analamulira Mose.

33 Kenaka Mose anamanga bwalo kuzungulira chihema ndi guwa lansembe ndipo anayika katani ya pa chipata cha bwalo. Kotero Mose anamaliza ntchito.

Ulemerero wa Yehova

34 Kenaka mtambo unaphimba tenti ya msonkhano, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho. 35 Mose sanathe kulowa mu tenti ya msonkhano chifukwa mtambo unali utakhazikika pa chihemacho, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho.

36 Pa maulendo awo onse, mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso pamene analipo. 37 Koma ngati mtambo sunachoke, iwo sankasamukanso mpaka tsiku limene udzachoke. 38 Kotero mtambo wa Yehova unkakhala pamwamba pa chihema usana, ndi mtambo wamoto umakhala usiku, pamaso pa nyumba yonse ya Israeli pa masiku onse aulendo wawo.

Yohane 19

Yesu Aweruzidwa kuti Aphedwe

19 Kenaka Pilato anatenga Yesu namukwapula mwankhanza. Asilikali analuka nkhata yaminga ndi kumuveka pamutu pake. Kenaka anamuveka mkanjo wapepo ndipo ankapita kwa Iye mobwerezabwereza ndi kumanena kuti, “Moni mfumu ya Ayuda?” Ndipo amamumenya makofi.

Pilato anatulukanso ndipo anati kwa Ayuda, “Taonani, ine ndikumubweretsa kuti inu mudziwe kuti ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu.” Pamenepo Yesu anatuluka atavala nkhata yaminga ndi mkanjo wapepo ndipo Pilato anawawuza kuti, “Nayu munthu uja!”

Atangomuona Iye akulu a ansembe ndi akuluakulu ena anafuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!”

Koma Pilato anayankha kuti, “Inu mutengeni ndi kumupachika. Koma ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu.”

Ayuda anayimirira nati, “Ife tili ndi lamulo, ndipo molingana ndi lamulolo, Iyeyu ayenera kuphedwa chifukwa akudzitcha kuti ndi Mwana wa Mulungu.”

Pilato atamva zimenezi, anachita mantha kwambiri, ndipo anabwereranso mʼnyumba yaufumu. Iye anafunsa Yesu kuti, “Kodi umachokera kuti?” Koma Yesu sanayankhe. 10 Pilato anati, “Kodi ukukana kundiyankhula ine? Kodi sukuzindikira kuti ine ndili ndi mphamvu yokumasula ndiponso mphamvu yokupachika?”

11 Yesu anayankha kuti, “Inu simukanakhala ndi mphamvu pa Ine akanapanda kukupatsani kumwamba. Nʼchifukwa chake amene wandipereka Ine kwa inu ndiye wochimwa kwambiri.”

12 Kuyambira pamenepo Pilato anayesa kuti amumasule Yesu, koma Ayuda anapitirira kufuwula kuti, “Ngati mumumasula munthuyu kuti apite, inu si bwenzi la Kaisara.”

13 Pilato atamva zimenezi, iye anamutulutsa Yesu kunja ndi kukhala pansi pa mpando wa woweruza pamalo otchedwa Mwala Wowaka (umene pa Chiaramaiki ndi Gabata). 14 Linali tsiku lokonzekera Sabata la Paska ndipo nthawi inali ora lachisanu ndi chimodzi masana.

Pilato anati kwa Ayuda, “Nayi mfumu yanu.”

15 Koma iwo anafuwula kuti, “Choka nayeni! Choka nayeni! Mpachikeni!”

Pilato anafunsa kuti, “Kodi ine ndipachike mfumu yanuyi?”

Akulu a ansembe anayankha kuti, “Ife tilibe mfumu ina koma Kaisara.”

16 Pomaliza Pilato anamupereka kwa iwo kuti akapachikidwe. Choncho asilikali anamutenga Yesu.

Kupachikidwa kwa Yesu

17 Atanyamula mtanda wake, anapita kumalo otchedwa “Malo a Bade” (mʼChiaramaiki amatchedwa Gologota). 18 Pamenepo iwo anamupachika Iye pamodzi ndi anthu ena awiri, mmodzi mbali ina ndi wina mbali inanso ndipo Yesu pakati.

19 Pilato analemba chikwangwani chomwe anachikhoma pa mtandapo. Panalembedwa mawu akuti, yesu wa ku nazareti, mfumu ya ayuda. 20 Ayuda ambiri anawerenga chikwangwanichi, pakuti pamalo pamene Yesu anapachikidwapo panali pafupi ndi mzinda ndipo chikwangwanicho chinalembedwa mu Chiaramaiki, Chilatini ndi Chigriki. 21 Kenaka mkulu wa ansembe wa Ayuda anakadandaula kwa Pilato nati, “Musalembe kuti ‘Mfumu ya Ayuda,’ koma kuti munthuyu amadzitcha kuti ndi mfumu ya Ayuda.”

22 Pilato anayankha kuti, “Chimene ine ndalemba, ndalemba.”

23 Asilikali atamupachika Yesu, anatenga zovala zake ndi kuzigawa zigawo zinayi, gawo limodzi la aliyense wa iwo, ndi kutsala mwinjiro wamʼkati wokha. Chovala ichi chinawombedwa kuyambira pamwamba mpaka pansi wopanda msoko.

24 Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni tisachingʼambe koma tichite maere kuti tione amene achitenge.”

Izi zinachitika kuti malemba akwaniritsidwe amene anati,

“Iwo anagawana zovala zanga pakati pawo
    ndi kuchita maere pa zovala zangazo.”

Choncho izi ndi zimene asilikali anachita.

25 Pafupi ndi mtanda wa Yesu panayima amayi ake, mngʼono wa amayi ake, Mariya mkazi wa Kaliyopa ndi Mariya wa ku Magadala. 26 Yesu ataona amayi ake pamenepo ndi wophunzira amene Iye anamukonda atayima pafupipo, Iye anati kwa amayi ake, “Amayi nayu mwana wanu.” 27 Anawuzanso wophunzirayo kuti, “Nawa amayi ako.” Kuyambira nthawi imeneyo, wophunzirayo anatenga amayiwo kupita nawo kwawo.

Imfa ya Yesu

28 Atadziwa kuti zonse zatha tsopano komanso kuti malemba akwaniritsidwe, Yesu anati, “Ine ndili ndi ludzu.” 29 Pomwepo panali mtsuko wodzaza ndi vinyo wosasa, choncho iwo ananyika chinkhupule ndi kuchisomeka ku mtengo wa hisope nachifikitsa kukamwa kwa Yesu. 30 Yesu atalandira chakumwachi anati, “Kwatha.” Ndipo Iye anaweramitsa mutu wake napereka mzimu wake.

31 Popeza linali Tsiku Lokonzekera ndipo tsiku linalo linali Sabata lapadera; Ayuda sanafune kuti mitembo ikhale pa mtanda pa Sabata, iwo anapempha Pilato kuti akathyole miyendo ndi kutsitsa mitemboyo. 32 Chifukwa chake asilikali anabwera ndi kuthyola miyendo ya munthu oyamba amene anapachikidwa ndi Yesu ndipo kenaka ya winayo. 33 Koma atafika pa Yesu ndi kupeza kuti anali atamwalira kale, iwo sanathyole miyendo yake. 34 Mʼmalo mwake, mmodzi wa asilikaliwo anamubaya Yesu ndi mkondo mʼnthiti, ndipo nthawi yomweyo munatuluka magazi ndi madzi. 35 Munthu amene anaona izi wapereka umboni ndipo umboni wake ndi woona. Iye akudziwa kuti akunena choonadi kuti inunso mukhulupirire. 36 Zinthu izi zinachitika kuti malemba akwaniritsidwe: “Palibe limodzi la mafupa limene lidzathyoledwa,” 37 ndi monga lemba linanso linena, “Iwo adzayangʼana Iye amene iwo anamubaya.”

Yesu Ayikidwa Mʼmanda

38 Kenaka, Yosefe wa ku Arimateyu anakapempha mtembo wa Yesu kwa Pilato. Tsono Yosefe anali wophunzira wa Yesu koma mobisa chifukwa iye ankaopa Ayuda. Atalandira chilolezo kwa Pilato, anakatsitsa mtembo wa Yesu. 39 Nekodimo, munthu amene poyamba pake anabwera kwa Yesu usiku, anatenga mafuta osakaniza ndi mure ndi aloe wolemera pafupifupi makilogalamu 32. 40 Pamenepo anatenga mtembo wa Yesu nawukulunga pamodzi ndi zonunkhiritsa mu nsalu za mtundu woyera monga mwa mwambo wa maliro wa Ayuda. 41 Pamalo pamene anapachikidwa Yesu panali munda ndipo mʼmundamo munali manda atsopano mʼmene munali simunayikidwemo aliyense. 42 Chifukwa linali Tsiku la Ayuda Lokonzekera ndi kuti mandawo anali pafupipo, iwo anayika Yesu mʼmenemo.

Miyambo 16

16 Zolinga za mu mtima ndi za munthu,
    koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.

Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake,
    koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.

Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova,
    ndipo zolinga zako zidzachitikadi.

Yehova amachita zonse ndi cholinga chake,
    ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.

Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova.
    Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.

Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake;
    chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.

Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova,
    ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.

Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo,
    kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.

Mtima wa munthu umalingalira zochita,
    koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.

10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu;
    ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.

11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova;
    miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.

12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu,
    pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.

13 Mawu owona amakondweretsa mfumu.
    Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.

14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa,
    koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.

15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo;
    ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.

16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide.
    Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.

17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa;
    wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.

18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko,
    ndipo munthu wodzikuza adzagwa.

19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa,
    kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.

20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino,
    ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.

21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu,
    ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.

22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako,
    koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.

23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru,
    ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.

24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi,
    amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.

25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu
    koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.

26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira;
    njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.

27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa
    ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.

28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano,
    ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.

29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake,
    ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.

30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota;
    amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.

31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero;
    munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.

32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo,
    munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.

33 Maere amaponyedwa pa mfunga,
    koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

Afilipi 3

Osakhulupirira za Thupi

Abale anga, ndikupitiriza kunena kuti, kondwani mwa Ambuye! Sizondivuta kuti ndilembenso mawu omwewo, ndipo zimenezi nʼzokuthandizani inuyo.

Chenjerani ndi agalu amenewa, anthu ochita zoyipa, anthu amene amadula thupi lawo. Pakuti ochita mdulidwe weniweni ndife. Ife amene timatumikira Mulungu motsogozedwa ndi Mzimu. Ife amene timanyadira Khristu, ndipo sitidalira zinthu za thupi ngakhale kuti ineyo ndili ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupizo.

Ngati pali winanso amene akuganiza kuti ali ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupi, ineyo ndili ndi zifukwa zoposa pamenepo. Ndinachita mdulidwe pa tsiku lachisanu ndi chitatu nditangobadwa. Ndine wa mtundu wa Israeli, wa fuko la Benjamini, Mhebri wa Ahebri, kunena za malamulo, ndinali Mfarisi. Kunena za changu changa, ndinkazunza mpingo. Kunena za chilungamo chopezeka chifukwa chotsata malamulo, ineyo ndinali wopanda cholakwa.

Koma zonse zimene ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziona kuti nʼzosapindulitsa chifukwa cha Khristu. Kuwonjeza pamenepo, ndikuziona zonse kuti nʼzopanda phindu poyerekeza ndi phindu lopambana la kudziwa Khristu Yesu Ambuye anga. Nʼchifukwa cha Yesuyo ndataya zinthu zonse ndipo ndikuziyesa zinyalala kuti ndipindule Khristu ndi kuti ndipezeke mwa Iyeyo, osati ndi chilungamo changa chobwera chifukwa chotsata malamulo, koma chimene chimabwera chifukwa chokhulupirira Khristu. Chilungamochi nʼchochokera kwa Mulungu, timachilandira mwachikhulupiriro. 10 Ine ndikufuna kudziwa Khristu, ndithu, kudziwa mphamvu zake za kuuka kwa akufa. Ndikufuna kuyanjana naye mʼmasautso ake, kufanana naye pa imfa yake 11 kuti nanenso ndidzaukitsidwe kwa akufa.

Kuthamanga Mpaka Kumapeto pa Mpikisano wa Liwiro

12 Sikuti ndazipeza kale zonsezi, kapena kuti ndakhala kale wangwiro, koma ndikuthamangabe ndi kuyesetsa kuti ndipeze chimene Khristu Yesu anandiyitanira. 13 Abale, sindidziyesera ndekha kuti ndachipeza kale chimenechi. Koma chinthu chimodzi chimene ndimachita, nʼkuyiwala zamʼmbuyo ndi kuthamangira molimbika zinthu zimene zili mʼtsogolo mwanga. 14 Ndikuthamangira kokathera mpikisanowo kuti ndikalandire mphotho imeneyi kumwamba, imene Mulungu anandiyitanira mwa Khristu Yesu.

Kutsanzira Paulo

15 Choncho ife tonse amene tili okhwima pa moyo wauzimu, tikhale ndi maganizo omwewa. Ndipo ngati pena ndi pena muli ndi maganizo osiyana ndi amenewa, pameneponso Mulungu adzakuwunikirani. 16 Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.

17 Abale, nonsenu pamodzi mudzinditsanzira ine, ndipo monga inu muli ndi chitsanzo, phunzirani kwa amene akukhala moyo motsatira momwe timakhalira. 18 Pakuti monga ndakhala ndikukuwuzani kawirikawiri mʼmbuyomu, ndipo tsopano ndikunenanso ndi misozi kuti, anthu ambiri akukhala monga adani a mtanda wa Khristu. 19 Mapeto awo ndi chiwonongeko, mulungu wawo ndi mimba zawo, ndipo ulemerero wawo ndi manyazi awo. Mtima wawo uli pa zinthu za dziko lapansi. 20 Koma ife ndife nzika za kumwamba ndipo tikudikirira mwachidwi Mpulumutsi wochokera kumeneko, Ambuye Yesu Khristu. 21 Iyeyo, ndi mphamvu imene imamuthandiza kukhazikitsa zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, adzasintha matupi athu achabewa kuti akhale ofanana ndi thupi lake la ulemerero.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.