Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Historical

Read the books of the Bible as they were written historically, according to the estimated date of their writing.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Zefaniya 1-3

Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.

Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi

“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse
    pa dziko lapansi,”
            akutero Yehova.
“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;
    ndidzawononga mbalame zamlengalenga
    ndi nsomba za mʼnyanja.
Ndidzawononga anthu oyipa,
    ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”
            akutero Yehova.

Chenjezo kwa Yuda

Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda
    ndi onse okhala mu Yerusalemu.
Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,
    mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
amene amagwada pa madenga a nyumba zawo
    kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,
amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,
    komanso mʼdzina la Moleki,
amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,
    osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,
    chifukwa tsiku la Yehova layandikira.
Yehova wakonzekera kupereka nsembe;
    wapatula iwo amene wawayitana.
Pa tsiku la nsembe ya Yehova
    ndidzalanga akalonga
    ndi ana aamuna a mfumu
ndi onse amene amavala
    zovala zachilendo.
Pa tsiku limenelo ndidzalanga
    onse amene safuna kuponda pa chiwundo,
amene amadzaza nyumba ya ambuye awo
    ndi chiwawa ndi chinyengo.

10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,
    “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,
    kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,
    ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;
    a malonda anu onse adzapululidwa,
    ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale
    ndi kulanga onse amene sakulabadira,
    amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,
amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,
    chabwino kaya choyipa.’
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa,
    nyumba zawo zidzagwetsedwa.
Adzamanga nyumba,
    koma osakhalamo;
adzadzala minda ya mpesa
    koma sadzamwako vinyo wake.”

Tsiku Lalikulu la Yehova

14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,
    layandikira ndipo lifika msanga.
Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,
    ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,
    tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,
tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,
    tsiku la mdima ndi lachisoni,
    tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,
    tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa
    ndi nsanja za pa ngodya.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu
    ndipo adzayenda ngati anthu osaona,
    chifukwa achimwira Yehova,
magazi awo adzamwazika ngati fumbi
    ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo
    sadzatha kuwapulumutsa
    pa tsiku la ukali wa Yehova.
Dziko lonse lapansi lidzanyeka
    mʼmoto wa nsanje yake
chifukwa adzakantha modzidzimutsa
    onse okhala pa dziko lapansi.
Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,
    inu mtundu wochititsa manyazi,
isanafike nthawi yachiweruzo,
    nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,
usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,
    tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,
    inu amene mumachita zimene amakulamulani.
Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;
    mwina mudzatetezedwa
    pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.

Za Afilisti

Gaza adzasiyidwa
    ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.
Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu
    ndipo Ekroni adzazulidwa.
Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,
    inu mtundu wa Akereti;
mawu a Yehova akutsutsa
    iwe Kanaani, dziko la Afilisti.
“Ndidzakuwononga
    ndipo palibe amene adzatsale.”

Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,
    lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;
    adzapezako msipu.
Nthawi ya madzulo adzagona
    mʼnyumba za Asikeloni.
Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;
    adzabwezeretsa mtendere wawo.

Za Mowabu ndi Amoni

“Ndamva kunyoza kwa Mowabu
    ndi chipongwe cha Amoni,
amene ananyoza anthu anga
    ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
Choncho, pali Ine Wamoyo,”
    akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,
    Amoni adzasanduka ngati Gomora;
malo a zomeramera ndi maenje a mchere,
    dziko la bwinja mpaka muyaya.
Anthu anga otsala adzawafunkha;
    opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”

10 Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,
    chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
11 Yehova adzawachititsa mantha kwambiri
    pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.
Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,
    uliwonse ku dziko la kwawo.

Za Kusi

12 “Inunso anthu a ku Kusi,
    mudzaphedwa ndi lupanga.”

Za Asiriya

13 Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto
    ndi kuwononga Asiriya,
kusiya Ninive atawonongekeratu
    ndi owuma ngati chipululu.
14 Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,
    pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.
Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu
    adzakhala pa nsanamira zake.
Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,
    mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,
    nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
15 Umenewu ndiye mzinda wosasamala
    umene kale unali wotetezedwa.
Unkanena kuti mu mtima mwake,
    “Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”
Taonani lero wasanduka bwinja,
    kokhala nyama zakutchire!
Onse owudutsa akuwunyoza
    ndi kupukusa mitu yawo.

Tsogolo la Yerusalemu

Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,
    owukira ndi odetsedwa!
Sumvera aliyense,
    sulandira chidzudzulo.
Sumadalira Yehova,
    suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,
    olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,
    zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Aneneri ake ndi odzikuza;
    anthu achinyengo.
Ansembe ake amadetsa malo opatulika
    ndipo amaphwanya lamulo.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;
    Iye salakwa.
Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,
    ndipo tsiku lililonse salephera,
    komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu;
    ndagwetsa malinga awo.
Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,
    popanda aliyense wodutsa.
Mizinda yawo yawonongedwa;
    palibe aliyense adzatsalemo.
Ndinati,
    ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa
    ndi kumvera kudzudzula kwanga!’
Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,
    kapena kuwalanganso.
Koma iwo anali okonzeka
    kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
Choncho mundidikire,” akutero Yehova,
    “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.
Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,
    kusonkhanitsa maufumu
ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;
    mkwiyo wanga wonse woopsa.
Dziko lonse lidzatenthedwa
    ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse
    kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova
    ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi
    anthu anga ondipembedza, omwazikana,
    adzandibweretsera zopereka.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi
    chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,
popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu
    amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.
Simudzakhalanso odzikuza
    mʼphiri langa lopatulika.
12 Koma ndidzasiya pakati panu
    anthu ofatsa ndi odzichepetsa,
    amene amadalira dzina la Yehova.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;
    sadzayankhulanso zonama,
    ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.
Adzadya ndi kugona
    ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;
    fuwula mokweza, iwe Israeli!
Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,
    iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 Yehova wachotsa chilango chako,
    wabweza mdani wako.
Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;
    sudzaopanso chilichonse.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,
    “Usaope, iwe Ziyoni;
    usafowoke.
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako,
    ali ndi mphamvu yopulumutsa.
Adzakondwera kwambiri mwa iwe,
    adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,
    adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18 “Ndidzakuchotserani zowawa
    za pa zikondwerero zoyikika;
    nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi
    onse amene anakuponderezani;
ndidzapulumutsa olumala
    ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.
Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu
    mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;
    pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.
Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu
    pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi
pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu
    inu mukuona,”
            akutero Yehova.

Hagai 1-2

Za Kumanga Nyumba ya Yehova

Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:

Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’ ”

Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti, “Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”

Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu. Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”

Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu. Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova. “Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake. 10 Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera. 11 Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”

12 Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.

13 Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova. 14 Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo, 15 pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

Ulemerero wa Nyumba Yatsopano ya Yehova

Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti: “Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti, ‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu? Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’

“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda. Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

Madalitso kwa Anthu Oyipitsidwa

10 Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti: 11 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena: 12 Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’ ”

Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”

13 Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?”

Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”

14 Pamenepo Hagai anati, “ ‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.

15 “ ‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova. 16 Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha. 17 Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova 18 ‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino. 19 Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso.

“ ‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’ ”

Zerubabeli Mphete Yolamulira ya Yehova

20 Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti: 21 “Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi. 22 Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.

23 “ ‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.