Chronological
Miyambo Ina ya Solomoni
25 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu;
ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi,
ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva
ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu;
ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu,
ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,”
kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa.
Chimene wachiona ndi maso ako,
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu
nanga udzachita chiyani pa mapeto pake
ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako,
koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi
ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera
ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide
kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola
kwa anthu amene amutuma;
iye amaziziritsa mtima bwana wake.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka
ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu,
ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira,
kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako
ukawirikiza kupita, udzadana naye.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama,
ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto,
kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni
kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira
kapena kuthira mchere pa chilonda.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye;
ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake,
ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula,
chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga
kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali
ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa
ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
27 Sibwino kudya uchi wambiri,
sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
28 Munthu amene samatha kudziretsa
ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
26 Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola,
ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira,
ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu,
choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake,
kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake,
kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga
kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu
ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 Kupereka ulemu kwa chitsiru
zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa
ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda,
ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake
chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo
kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango,
mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake,
momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale;
zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru
kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 Munthu wongolowera mikangano imene si yake
ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 Monga munthu wamisala amene
akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake,
amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Pakasowa nkhuni, moto umazima;
chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto,
ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma;
chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi
ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 Munthu wachidani amayankhula zabwino
pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire,
pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Ngakhale amabisa chidani mochenjera,
koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha;
ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka,
ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.