Chronological
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide.
5 Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova,
ganizirani za kusisima kwanga
2 Mverani kulira kwanga kofuna thandizo,
Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,
pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
3 Mmawa, Yehova mumamva mawu anga;
Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu
ndi kudikira mwachiyembekezo.
4 Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa;
choyipa sichikhala pamaso panu.
5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu;
Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
6 Mumawononga iwo amene amanena mabodza;
anthu akupha ndi achinyengo,
Yehova amanyansidwa nawo.
7 Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu,
ndidzalowa mʼNyumba yanu;
mwa ulemu ndidzaweramira pansi
kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
8 Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu
chifukwa cha adani anga ndipo
wongolani njira yanu pamaso panga.
9 Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike;
mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko.
Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;
ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu!
Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo.
Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri,
pakuti awukira Inu.
11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere;
lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe.
Aphimbeni ndi chitetezo chanu,
iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama;
mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.
Salimo la Davide. Kupempha.
38 Yehova musandidzudzule mutapsa mtima
kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa,
ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa;
mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja
ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha
chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri;
tsiku lonse ndimangolira.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika,
mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu;
ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye,
kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha;
ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga;
anansi anga akhala kutali nane.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo,
oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga;
tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve,
monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 Ndakhala ngati munthu amene samva,
amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 Ndikudikira Inu Yehova;
mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere
kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 Pakuti ndili pafupi kugwa,
ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga;
ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu;
amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino
amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 Inu Yehova, musanditaye;
musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 Bwerani msanga kudzandithandiza,
Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
41 Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka;
Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake;
Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko
ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala
ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo;
chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti,
“Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
6 Pamene wina abwera kudzandiona,
amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe;
kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane,
iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
8 “Matenda owopsa amugwira;
sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira,
iye amene amadya pamodzi ndi ine
watukula chidendene chake kulimbana nane.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo,
dzutseni kuti ndiwabwezere.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane,
pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga
ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli
kuchokera muyaya mpaka muyaya.
Ameni ndi Ameni.
BUKU LACHIWIRI
Masalimo 42–72
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.
42 Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi,
kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
2 Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo.
Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
3 Misozi yanga yakhala chakudya changa
usana ndi usiku,
pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti,
“Mulungu wako ali kuti?”
4 Zinthu izi ndimazikumbukira
pamene ndikukhuthula moyo wanga:
momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu,
kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu
ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko
pakati pa anthu a pa chikondwerero.
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga?
Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?
Yembekezera Mulungu,
pakuti ndidzamulambirabe,
Mpulumutsi wanga ndi 6 Mulungu wanga.
Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga
kotero ndidzakumbukira Inu
kuchokera ku dziko la Yorodani,
ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
7 Madzi akuya akuyitana madzi akuya
mu mkokomo wa mathithi anu;
mafunde anu onse obwera mwamphamvu
andimiza.
8 Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake,
nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane;
pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.
9 Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa,
“Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala?
Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,
woponderezedwa ndi mdani?”
10 Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo
pamene adani anga akundinyoza,
tsiku lonse akunena kuti,
“Mulungu wako ali kuti?”
11 Bwanji ukumva chisoni,
iwe mtima wanga?
Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga?
Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso,
Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.