Chronological
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu.
81 Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu;
Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini
imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano,
ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
4 ili ndi lamulo kwa Israeli,
langizo la Mulungu wa Yakobo.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe
pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto,
kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo;
Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani,
ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu;
ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba.
Sela
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani
ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu;
musadzagwadire mulungu wina.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.
Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
11 “Koma anthu anga sanandimvere;
Israeli sanandigonjere.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo
kuti atsate zimene ankafuna.
13 “Anthu anga akanangondimvera,
Israeli akanatsatira njira zanga,
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo
ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake,
ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri;
ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara.
88 Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa,
usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Pemphero langa lifike pamaso panu;
tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri
ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda.
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje;
ndine munthu wopanda mphamvu.
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa,
monga ophedwa amene agona mʼmanda,
amene Inu simuwakumbukiranso,
amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni,
mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri,
mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse.
Sela
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni
ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo.
Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 maso anga ada ndi chisoni.
Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse;
ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa?
Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu?
Sela
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda,
za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima,
kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo;
mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana
ndi kundibisira nkhope yanu?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa;
ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 Ukali wanu wandimiza;
zoopsa zanu zandiwononga.
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula;
zandimiza kwathunthu.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga;
mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.
92 Nʼkwabwino kutamanda Yehova
ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa,
ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi
ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova;
Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova,
maganizo anu ndi ozamadi!
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa,
zitsiru sizizindikira,
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu
ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula,
adzawonongedwa kwamuyaya.
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 Zoonadi adani anu Yehova,
zoonadi adani anu adzawonongeka;
onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati;
mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane,
makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa,
adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova,
adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo,
adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama;
Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
93 Yehova akulamulira, wavala ulemerero;
Yehova wavala ulemerero ndipo wadzimangirira mphamvu,
dziko lonse lakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
2 Mpando wanu waufumu unakhazikika kalekale;
Inu ndinu wamuyaya.
3 Nyanja zakweza Inu Yehova,
nyanja zakweza mawu ake;
nyanja zakweza mafunde ake ochita mkokomo.
4 Yehova ndi wamphamvu kupambana mkokomo wa madzi ambiri,
ndi wamphamvu kupambana mafunde a nyanja,
Yehova mmwamba ndi wamphamvu.
5 Malamulo anu Yehova ndi osasinthika;
chiyero chimakongoletsa nyumba yanu
mpaka muyaya.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.