Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Chronological

Read the Bible in the chronological order in which its stories and events occurred.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 17

Pemphero la Davide.

17 Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo;
    mverani kulira kwanga.
Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa
    popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu;
    maso anu aone chimene ndi cholungama.

Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku,
    ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu;
    Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Kunena za ntchito za anthu,
    monga mwa mawu a pakamwa panu,
Ine ndadzisunga ndekha
    posatsata njira zachiwawa.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu;
    mapazi anga sanaterereke.

Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha;
    tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu,
    Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja
    iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Mundisunge ine ngati mwanadiso;
    mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine,
    kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.

10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo,
    ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 Andisaka, tsopano andizungulira
    ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama;
    ngati mkango waukulu wokhala mobisala.

13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi;
    landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere,
    kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno.

Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu;
    ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri,
    ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu;
    pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

Masalimo 35

Salimo la Davide.

35 Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;
    mumenyane nawo amene akumenyana nane.
Tengani chishango ndi lihawo;
    dzukani ndipo bwerani mundithandize.
Tengani mkondo ndi nthungo,
    kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa.
Uzani moyo wanga kuti,
    “Ine ndine chipulumutso chako.”

Iwo amene akufunafuna moyo wanga
    anyozedwe ndi kuchita manyazi;
iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke
    abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo
    pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera
    pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa
    ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa
    ukonde umene iwo abisa uwakole,
    agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova
    ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
10 Thupi langa lidzafuwula mokondwera,
    “Ndani angafanane nanu Yehova?
Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri,
    osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”

11 Mboni zopanda chisoni zinayimirira,
    zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
12 Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino
    ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
13 Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli
    ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya.
Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
14     ndinayendayenda ndi kulira maliro,
    kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga.
Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima
    kukhala ngati ndikulira amayi anga.
15 Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;
    ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa.
    Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
16 Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;
    anandikukutira mano awo.
17 Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?
    Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo,
    moyo wanga wopambana ku mikango.
18 Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;
    pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.

19 Musalole adani anga onyenga
    akondwere chifukwa cha masautso anga;
musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa
    andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
20 Iwowo sayankhula mwamtendere,
    koma amaganizira zonamizira
    iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
21 Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!
    Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”

22 Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.
    Ambuye musakhale kutali ndi ine.
23 Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!
    Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
24 Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.
    Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
25 Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”
    Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”

26 Onse amene amakondwera ndi masautso anga
    achite manyazi ndi kusokonezeka.
Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana,
    avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
27 Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,
    afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo.
Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke,
    Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
28 Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu
    ndi za matamando anu tsiku lonse.

Masalimo 54

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

54 Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;
    onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu
    mvetserani mawu a pakamwa panga.

Alendo akundithira nkhondo;
    anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,
    anthu amene salabadira za Mulungu.

Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;
    Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;
    mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;
    ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,
    pakuti ndi labwino.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,
    ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

Masalimo 63

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

63 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,
    moona mtima ine ndimakufunafunani;
moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,
    thupi langa likulakalaka inu,
mʼdziko lowuma ndi lotopetsa
    kumene kulibe madzi.

Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika
    ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
Chifukwa chikondi chanu
    ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,
    ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.
    Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

Pa bedi panga ndimakumbukira inu;
    ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
Chifukwa ndinu thandizo langa,
    ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
Moyo wanga umakangamira Inu;
    dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;
    adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga
    ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;
    onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,
    koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.