Chronological
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati.
56 Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri;
tsiku lonse akundithira nkhondo.
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse,
ambiri akumenyana nane monyada.
3 Ndikachita mantha
ndimadalira Inu.
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,
mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.
Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga;
nthawi zonse amakonza zondivulaza.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira,
amayangʼanitsitsa mayendedwe anga
ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
7 Musalole konse kuti athawe;
mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
8 Mulembe za kulira kwanga,
mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu.
Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo
pamene ndidzalirira kwa Inu.
Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda,
mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha.
Kodi munthu angandichite chiyani?
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu;
ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa
ndi mapazi anga kuti ndingagwe,
kuti ndiyende pamaso pa Mulungu
mʼkuwala kwa moyo.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
120 Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,
ndipo Iye amandiyankha.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,
ndi kwa anthu achinyengo.
3 Kodi adzakuchitani chiyani,
ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,
ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,
kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati
pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 Ine ndine munthu wamtendere;
koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
140 Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;
tetezeni kwa anthu ankhanza,
2 amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa
ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
3 Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;
pa milomo yawo pali ululu wa mamba.
Sela
4 Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;
tchinjirizeni kwa anthu ankhanza
amene amakonza zokola mapazi anga.
5 Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;
iwo atchera zingwe za maukonde awo
ndipo anditchera misampha pa njira yanga.
Sela
6 Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
Imvani kupempha kwanga Yehova.
7 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,
mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
8 Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;
musalole kuti zokonza zawo zitheke,
mwina iwo adzayamba kunyada.
Sela
9 Mitu ya amene andizungulira
iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
10 Makala amoto agwere pa iwo;
aponyedwe pa moto,
mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;
choyipa chilondole anthu ankhanza.
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,
ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,
ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Salimo la Davide.
141 Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
2 Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;
kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
3 Yehova ikani mlonda pakamwa panga;
londerani khomo la pa milomo yanga.
4 Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;
kuchita ntchito zonyansa
pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;
musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
5 Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;
andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.
Mutu wanga sudzakana zimenezi.
Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
6 Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,
ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
7 Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,
ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”
8 Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;
ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
9 Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,
ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
10 Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,
mpaka ine nditadutsa mwamtendere.
Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.
142 Ndikulirira Yehova mofuwula;
ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.
2 Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;
ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.
3 Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,
ndinu amene mudziwa njira yanga.
Mʼnjira imene ndimayendamo
anthu anditchera msampha mobisa.
4 Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;
palibe amene akukhudzika nane.
Ndilibe pothawira;
palibe amene amasamala za moyo wanga.
5 Ndilirira Inu Yehova;
ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,
gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”
6 Mverani kulira kwanga
pakuti ndathedwa nzeru;
pulumutseni kwa amene akundithamangitsa
pakuti ndi amphamvu kuposa ine.
7 Tulutseni mʼndende yanga
kuti nditamande dzina lanu.
Ndipo anthu olungama adzandizungulira
chifukwa cha zabwino zanu pa ine.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.