Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Chronological

Read the Bible in the chronological order in which its stories and events occurred.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 7

Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini.

Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu;
    pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
mwina angandikadzule ngati mkango,
    ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.

Inu Yehova Mulungu wanga,
    ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere,
    kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira,
    lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi
    ndipo mundigoneke pa fumbi.
            Sela

Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu;
    nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga.
    Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani.
    Alamulireni muli kumwambako;
    Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo.
Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa,
    monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
Inu Mulungu wolungama,
    amene mumasanthula maganizo ndi mitima,
thetsani chiwawa cha anthu oyipa
    ndipo wolungama akhale motetezedwa.

10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba,
    amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Mulungu amaweruza molungama,
    Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Ngati munthu satembenuka,
    Mulungu adzanola lupanga lake,
    Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa;
    Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.

14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse.
    Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa
    amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini;
    chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.

17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake;
    ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

Masalimo 27

Salimo la Davide.

27 Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;
    ndidzaopa yani?
Yehova ndi linga la moyo wanga;
    ndidzachita mantha ndi yani?
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane
    kudzadya mnofu wanga,
pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo,
    iwo adzapunthwa ndi kugwa.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge,
    mtima wanga sudzaopa.
Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane,
    ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.

Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,
    ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:
kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova
    masiku onse a moyo wanga,
ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,
    ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
Pakuti pa tsiku la msautso
    Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;
adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake
    ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa
    kuposa adani anga amene andizungulira;
pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe;
    ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.

Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova
    mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!”
    Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
Musandibisire nkhope yanu,
    musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo;
    mwakhala muli thandizo langa.
Musandikane kapena kunditaya,
    Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya
    Yehova adzandisamala.
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova,
    munditsogolere mʼnjira yowongoka
    chifukwa cha ondizunza.
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga,
    pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane
    ndipo zikundiopseza.

13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi;
    ndidzaona ubwino wa Yehova
    mʼdziko la anthu amoyo.
14 Dikirani pa Yehova;
    khalani anyonga ndipo limbani mtima
    nimudikire Yehova.

Masalimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

31 Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;
    musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;
    mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
Tcherani khutu lanu kwa ine,
    bwerani msanga kudzandilanditsa;
mukhale thanthwe langa lothawirapo,
    linga lolimba kundipulumutsa ine.
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,
    chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera
    pakuti ndinu pothawirapo panga.
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;
    womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;
    ine ndimadalira Yehova.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu
    popeza Inu munaona masautso anga
    ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
Inu simunandipereke kwa mdani
    koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;
    maso anga akulefuka ndi chisoni,
    mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima
    ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;
mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,
    ndipo mafupa anga akulefuka.
11 Chifukwa cha adani anga onse,
    ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;
ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.
    Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;
    ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;
    zoopsa zandizungulira mbali zonse;
iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,
    kuti atenge moyo wanga.

14 Koma ndikudalira Inu Yehova;
    ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 Masiku anga ali mʼmanja mwanu;
    ndipulumutseni kwa adani anga
    ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;
    pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 Yehova musalole kuti ndichite manyazi,
    pakuti ndalirira kwa Inu;
koma oyipa achititsidwe manyazi
    ndipo agone chete mʼmanda.
18 Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,
    pakuti chifukwa cha kunyada
    ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19 Ndi waukulu ubwino wanu
    umene mwawasungira amene amakuopani,
umene mumapereka anthu akuona
    kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,
    kuwateteza ku ziwembu za anthu;
mʼmalo anu okhalamo mumawateteza
    kwa anthu owatsutsa.

21 Matamando akhale kwa Yehova,
    pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine
    pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,
    “Ine ndachotsedwa pamaso panu!”
Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga
    pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23 Kondani Yehova oyera mtima ake onse!
    Yehova amasunga wokhulupirika
    koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,
    inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

Masalimo 34

Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka.

34 Ndidzayamika Yehova nthawi zonse;
    matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Moyo wanga udzanyadira Yehova;
    anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine;
    tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.

Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha;
    anandilanditsa ku mantha anga onse.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira;
    nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva;
    Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye
    ndi kuwalanditsa.

Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino;
    wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake,
    pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala
    koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.

11 Bwerani ana anga, mundimvere;
    ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake
    ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 asunge lilime lake ku zoyipa
    ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;
    funafuna mtendere ndi kuwulondola.

15 Maso a Yehova ali pa olungama
    ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa,
    kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.

17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva;
    Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima
    ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.

19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri,
    Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Iye amateteza mafupa ake onse,
    palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.

21 Choyipa chidzapha anthu oyipa;
    adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Yehova amawombola atumiki ake;
    aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

Masalimo 52

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”

52 Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?
    Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,
    iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;
    lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,
    ntchito yako nʼkunyenga.
Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.
    Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.
            Sela
Umakonda mawu onse opweteka,
    iwe lilime lachinyengo!

Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:
    iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;
    iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;
    adzamuseka nʼkumanena kuti,
“Pano tsopano pali munthu
    amene sanayese Mulungu linga lake,
koma anakhulupirira chuma chake chambiri
    nalimbika kuchita zoyipa!”

Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi
    wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;
ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu
    kwa nthawi za nthawi.
Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;
    chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera
    pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.