Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Bible in 90 Days

An intensive Bible reading plan that walks through the entire Bible in 90 days.
Duration: 88 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yesaya 29:1-41:18

Tsoka kwa Mzinda wa Davide

29 Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli,
    mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo!
Papite chaka chimodzi kapena ziwiri
    ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli
    ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula,
    mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo;
    ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo
    ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka,
    mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi,
adzamveka ngati a mzukwa.
    Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.

Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti.
    Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo.
Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
    Yehova Wamphamvuzonse adzabwera
ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu,
    kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli
    nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga,
chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto,
    gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya,
    koma podzuka ali nayobe njala;
kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa,
    koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa.
Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse
    chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.

Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa.
    Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya,
ledzerani, koma osati ndi vinyo,
    dzandirani, koma osati ndi mowa.
10 Yehova wakugonetsani tulo tofa nato.
    Watseka maso anu, inu aneneri;
    waphimba mitu yanu, inu alosi.

11 Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.” 12 Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”

13 Ambuye akuti,

“Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo,
    ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo,
    koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.
Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso.
    Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
14 Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira
    kuwachitira ntchito zodabwitsa;
nzeru za anthu anzeru zidzatha,
    luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
15 Tsoka kwa amene amayesetsa
    kubisira Yehova maganizo awo,
amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti,
    “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
16 Inu mumazondotsa zinthu
    ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya.
Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti
    “Sunandipange ndi iwe?”
Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti,
    “Iwe sudziwa chilichonse?”

17 Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde,
    ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
18 Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku,
    ndipo anthu osaona amene
    ankakhala mu mdima adzapenya.
19 Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova;
    ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
20 Koma anthu ankhanza adzazimirira,
    oseka anzawo sadzaonekanso,
    ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
21 Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa,
    kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu
    ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.

22 Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti,

“Anthu anga sadzachitanso manyazi;
    nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
23 Akadzaona ana awo ndi
    ntchito ya manja anga pakati pawo,
adzatamanda dzina langa loyera;
    adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo,
    ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
24 Anthu opusa adzapeza nzeru;
    onyinyirika adzalandira malangizo.”

Tsoka kwa Mtundu Wopanduka

30 Yehova akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira
    amene amachita zowakomera iwo okha osati Ine,
nachita mgwirizano wawowawo
    koma osati motsogozedwa ndi Ine.
    Choncho amanka nachimwirachimwira.
Amapita ku Igupto kukapempha thandizo
    koma osandifunsa;
amathawira kwa Farao kuti awateteze,
    ku Igupto amafuna malo opulumulira.
Koma chitetezo cha Farao chidzakhala manyazi anu,
    malo a mthunzi a ku Igupto mudzachita nawo manyazi.
Ngakhale kuti nduna zawo zili ku Zowani,
    ndipo akazembe awo afika kale ku Hanesi,
aliyense wa ku Yuda adzachita manyazi
    chifukwa cha anthu opanda nawo phindu,
amene sabweretsa thandizo kapena phindu,
    koma manyazi ndi mnyozo.”

Uthenga wonena za nyama za ku Negevi:

Akazembe akuyenda mʼdziko lovuta ndi losautsa,
    mʼmene muli mikango yayimuna ndi yayikazi,
    mphiri ndi njoka zaululu.
Iwo amasenzetsa abulu ndi ngamira chuma chawo,
    kupita nazo kwa mtundu wa anthu
umene sungawathandize.
    Amapita ku Igupto amene thandizo lake ndi lachabechabe.
Nʼchifukwa chake dzikolo ndalitcha
    Rahabe chirombo cholobodoka.

Yehova anandiwuza kuti, “Tsopano pita,
    ukalembe zimenezi mʼbuku iwo akuona
ndipo lidzakhala ngati umboni wosatha
    masiku a mʼtsogolo.
Amenewa ndi anthu owukira, onama ndi
    osafuna kumvera malangizo a Yehova.
10 Iwo amawuza alosi kuti,
    ‘Musationerenso masomphenya!’
Ndipo amanena kwa mneneri kuti,
    ‘Musatinenerenso zoona,’
mutiwuze zotikomera,
    munenere za mʼmutu mwanu.
11 Patukani pa njira ya Yehova,
    lekani kutsata njira ya Yehova;
ndipo tisamvenso mawu
    a Woyerayo uja wa Israeli!”

12 Nʼchifukwa chake Woyerayo wa Israeli akunena kuti,

“Popeza inu mwakana uthenga uwu,
    mumakhulupirira zopondereza anzanu
    ndipo mumadalira kuchita zoyipa,
13 choncho tchimo linalo lidzakhala ngati mingʼalu
    pa khoma lalitali ndi lopendama
    limene linagwa mwadzidzidzi ndi mwamsangamsanga.
14 Lidzaphwanyika ngati mbiya
    imene yanyenyekeratu,
mwakuti pakati pake sipadzapezeka phale ngakhale
    lopalira moto mʼngʼanjo
    kapena lotungira madzi mʼchitsime.”

15 Zimene Ambuye Yehova, Woyerayo wa Israeli ananena ndi izi:

“Ngati mubwerera ndi kupuma mudzapulumuka,
    ngati mukhala chete ndi kukhulupirira mudzakhala amphamvu,
    koma inu munakana zimenezi.
16 Inu mukuti, ‘Ayi ife tidzathawa,
    tidzakwera pa akavalo aliwiro.’
Zoonadi kuti mudzakwera pa akavalo aliwiro,
    koma okuthamangitsani adzakhalanso aliwiro.
17 Anthu 1,000 mwa inu adzathawa
    poona mdani mmodzi;
poona adani asanu okha
    nonsenu mudzathawa.
Otsala anu
    adzakhala ngati mbendera pa phiri,
    ndi ngati chizindikiro cha pa chulu.”

18 Komatu Yehova akufunitsitsa kuti akukomereni mtima,
    iye ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo.
Pakuti Yehova ndi Mulungu wachilungamo.
    Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye!

19 Inu anthu a ku Ziyoni, amene mukhala mu Yerusalemu simudzaliranso. Mulungu adzakukomerani mtima pamene adzamva kulira kwanu kopempha thandizo! Ndipo akadzamva, adzakuyankhani. 20 Ngakhale Ambuye adzakulowetseni mʼmasautso, aphunzitsi anu sadzakhala kakasi; inu mudzawaona ndi maso anuwo. 21 Ngati mudzapatukira kumanja kapena kumanzere, mudzamva mawu kumbuyo kwanu woti, “Njira ndi iyi; yendani mʼmenemo.” 22 Pamenepo mudzawononga mafano anu okutidwa ndi siliva ndiponso zifanizo zanu zokutidwa ndi golide; mudzawataya ngati zinthu zonyansa ndipo mudzati, “Zichoke zonsezi!”

23 Yehova adzakugwetseraninso mvula pa mbewu zanu zimene mukadzale mʼnthaka, ndipo chakudya chimene mudzakolole chidzakhala chabwino ndi chochuluka. Tsiku limenelo ngʼombe zanu zidzadya msipu wochuluka. 24 Ngʼombe ndi abulu amene amalima mʼmunda adzadya chakudya chamchere, chopetedwa ndi foloko ndi fosholo. 25 Pa tsiku limene adani anu adzaphedwa ndi nsanja zawo kugwa, mitsinje ya madzi idzayenda pa phiri lililonse lalikulu ndi pa phiri lililonse lalingʼono. 26 Mwezi udzawala ngati dzuwa, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzawonjezereka kasanu nʼkawiri, ngati kuwala kwa tsiku limodzi. Yehova adzamanga mabala a anthu ake ndi kupoletsa zilonda zimene Iye anachititsa polanga anthu ake.

27 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kutali,
    ndipo mkwiyo wake ndiwonyeka ndi chiweruzo chake chidzakhala chopweteka.
Iye wayankhula mwaukali kwambiri,
    ndipo mawu ake ali ngati moto wonyeka.
28 Mpweya wake uli ngati mtsinje wosefukira,
    wa madzi ofika mʼkhosi.
Iye adzasefa anthu a mitundu ina ndi sefa wosakaza;
    Iye akuyika zitsulo mʼkamwa mwa anthu a mitundu ina ngati akavalo,
    kuti ziwasocheretse.
29 Ndipo inu mudzayimba
    mokondwa monga mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika.
Mudzasangalala
    ngati anthu oyimba zitoliro
popita ku phiri la Yehova,
    thanthwe la Israeli.
30 Anthu adzamva liwu la ulemerero la Yehova
    ndipo adzaona dzanja lake likutsika pa iwo
ndi mkwiyo woopsa, pamodzi ndi moto wonyeketsa,
    mphenzi, namondwe ndi matalala.
31 Asiriya adzaopa liwu la Yehova,
    ndipo Iye adzawakantha ndi ndodo.
32 Yehova akamadzalanga adani ake ndi ndodo,
    anthu ake adzakhala akuvina nyimbo
zoyimbira matambolini ndi azeze,
    Yehova ndiye ati adzamenyane ndi Asiriyawo.
33 Malo otenthera zinthu akonzedwa kale;
    anakonzera mfumu ya ku Asiriya.
Dzenje la motolo ndi lozama ndi lalikulu,
    ndipo muli nkhuni zambiri;
mpweya wa Yehova,
    wangati mtsinje wa sulufule,
    udzayatsa motowo pa nkhunizo.

Tsoka kwa Amene Amadalira Igupto

31 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo,
    amene amadalira akavalo,
nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo
    ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo,
koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli,
    kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga,
    ndipo sasintha chimene wanena.
Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa,
    komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu;
    akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu.
Yehova akangotambasula dzanja lake,
    amene amapereka chithandizo adzapunthwa,
    amene amalandira chithandizocho adzagwa;
    onsewo adzathera limodzi.

Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi:

“Monga mkango kapena msona wamkango umabangula
    ukagwira nyama yake,
ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka
    ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo,
momwemonso palibe chingaletse
    Yehova Wamphamvuzonse
kubwera kudzatchinjiriza
    phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake,
    Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu;
ndi kumupulumutsa,
    iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”

Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu. Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.

“Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu.
    Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga.
Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo
    adzagwira ntchito yathangata.
Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha,
    ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha
kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.”
    Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni,
    ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.

Ufumu Wachilungamo

32 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo,
    ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo
    ndi malo obisalirapo namondwe,
adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu,
    ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.

Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka,
    ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa,
    ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake
    ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru,
    amaganiza kuchita zoyipa:
Iye amachita zoyipira Mulungu,
    ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova;
anjala sawapatsa chakudya
    ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso,
    iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa.
Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake
    ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino,
    Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.

Akazi a ku Yerusalemu

Khalani maso, inu akazi
    amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji
ndipo imvani mawu anga.
    Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono
    inu akazi amatama mudzanjenjemera;
chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika
    ndipo zipatso sizidzaoneka.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu;
    ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu.
Vulani zovala zanu,
    ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde,
    ndi mphesa yawonongeka.
13 Mʼdziko la anthu anga
    mwamera minga ndi mkandankhuku.
Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero
    ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa,
    mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu;
malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya.
    Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake,
    ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde,
    ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama
    ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo;
    zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere,
    mʼnyumba zodalirika,
    ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala
    ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu.
    Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse,
    ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.

Msautso ndi Thandizo

33 Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe,
    amene sunawonongedwepo!
Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri,
    iwe amene sunanyengedwepo!
Iwe ukadzaleka kuwononga,
    udzawonongedwa,
ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga,
    ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.

Inu Yehova, mutikomere mtima ife;
    tikulakalaka Inu.
Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu,
    ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa;
    pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe.
    Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.

Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse
    adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu,
    adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka;
    kuopa Yehova ngati madalitso.

Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu;
    akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu,
    mʼmisewu mulibe anthu a paulendo.
Mdaniyo ndi wosasunga pangano.
    Iye amanyoza mboni.
    Palibe kulemekezana.
Dziko likulira ndipo likunka likutha.
    Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota.
Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala.
    Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.

10 Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka
    ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga,
    ndipo ndidzakwezedwa.
11 Zolingalira zanu nʼzachabechabe
    ngati udzu wamanyowa.
    Mpweya wamoto udzakupserezani.
12 Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza;
    ndi ngati minga yodulidwa.”

13 Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita;
    inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
14 Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha;
    anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera:
Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa?
    Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
15 Angathe kuti ndi amene amachita zolungama
    ndi kuyankhula zoona,
amene amakana phindu lolipeza monyenga
    ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu,
amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo
    ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
16 Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja,
    kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri.
Azidzalandira chakudya chake
    ndipo madzi sadzamusowa.

17 Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola
    ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
18 Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija:
    “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja?
    Ali kuti wokhometsa misonkho uja?
    Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
19 Simudzawaonanso anthu odzikuza aja,
    anthu aja achiyankhulo chosadziwika,
    chachilendo ndi chosamveka.

20 Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu;
    maso anu adzaona Yerusalemu,
    mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa,
zikhomo zake sizidzazulidwa,
    kapena zingwe zake kuduka.
21 Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake
    ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu.
Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo,
    sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
22 Pakuti Yehova ndi woweruza wathu,
    Yehova ndiye wotilamulira,
Yehova ndiye mfumu yathu;
    ndipo ndiye amene adzatipulumutse.

23 Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka,
    sizikutha kulimbitsa mlongoti wake,
    matanga ake sakutheka kutambasuka.
Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri
    ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
24 Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala”
    ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.

Chiweruzo cha Anthu a Mitundu Yonse

34 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve:
    tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse:
Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,
    dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse;
    wapsera mtima magulu awo onse ankhondo.
Iye adzawawononga kotheratu,
    nawapereka kuti aphedwe.
Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja,
    mitembo yawo idzawola ndi kununkha;
    mapiri adzafiira ndi magazi awo.
Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka
    ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala;
nyenyezi zonse zidzayoyoka
    ngati masamba ofota a mphesa,
    ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.

Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba;
    taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu,
    anthu amene ndawawononga kotheratu.”
Lupanga la Yehova lakhuta magazi,
    lakutidwa ndi mafuta;
magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi,
    mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna.
Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira
    ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati,
    ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe.
Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha,
    ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.

Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira
    ndi kulanga adani a Ziyoni.
Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula,
    ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule;
    dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana;
    utsi wake udzafuka kosalekeza.
Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado;
    palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu;
    amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo.
Mulungu adzatambalitsa pa Edomu
    chingwe choyezera cha chisokonezo
    ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko;
    akalonga ake onse adzachotsedwa.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa,
    khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake.
Ankhandwe azidzadya mʼmenemo;
    malo okhalamo akadzidzi.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi,
    ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana.
Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa
    ndi kupeza malo opumulirako.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira,
    adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake;
akamtema adzasonkhananso kumeneko,
    awiriawiri.

16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga:

mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa;
    sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake.
Pakuti Yehova walamula kuti zitero,
    ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
17 Yehova wagawa dziko lawo;
    wapatsa chilichonse chigawo chake.
Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya
    ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.

Chimwemwe cha Opulumutsidwa

35 Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala;
    dziko lowuma lidzakondwa
ndi kuchita maluwa. Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka
    lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe.
Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni,
    maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni.

Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova,
    ukulu wa Mulungu wathu.
Limbitsani manja ofowoka,
    limbitsani mawondo agwedegwede;
nenani kwa a mitima yamantha kuti;
    “Limbani mtima, musachite mantha;
Mulungu wanu akubwera,
    akubwera kudzalipsira;
ndi kudzabwezera chilango adani anu;
    akubwera kudzakupulumutsani.”

Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso
    ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala,
    ndipo osayankhula adzayimba mokondwera.
Akasupe adzatumphuka mʼchipululu
    ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
mchenga wotentha udzasanduka dziwe,
    nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe.
Pamene panali mbuto ya ankhandwe
    padzamera udzu ndi bango.

Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu;
    ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika.
Anthu odetsedwa
    sadzayendamo mʼmenemo;
    zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
Kumeneko sikudzakhala mkango,
    ngakhale nyama yolusa sidzafikako;
    sidzapezeka konse kumeneko.
Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10     Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera.
Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba;
    kumeneko adzakondwa mpaka muyaya.
Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe,
    ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

Senakeribu Awopseza Yerusalemu

36 Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda. Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala. Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.

Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti,

“Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani? Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine? Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira. Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’

“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo! Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo. 10 Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”

11 Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”

12 Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”

13 Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya! 14 Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni! 15 Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’

16 “Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake, 17 mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.

18 “Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya? 19 Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa? 20 Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”

21 Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”

22 Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.

Hezekiya Apempha Thandizo kwa Yehova

37 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova. Iye anatuma Eliyakimu woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo, ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi. Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.’ Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a kazembe amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.”

Akuluakulu a mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya, Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine. Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake, ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’ ”

Kazembe wa ankhondo uja atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.

Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi akubwera kudzachita naye nkhondo. Atamva zimenezi, anatumiza amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa: 10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya ku Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’ 11 Ndithudi iwe unamva zimene mafumu a ku Asiriya akhala akuchitira mayiko onse. Iwo anawawononga kotheratu. Tsono iwe ndiye ndi kupulumuka? 12 Makolo anga anawononga mizinda ya Gozani, Harani, Rezefi ndi anthu a ku Edeni amene ankakhala ku Telasara. Kodi milungu inayi ija anawapulumutsa anthu a mizindayi? 13 Kodi mafumu a ku Hamati, Aripadi, Safaravaimu, Hena ndi Iva ali kuti?”

Pemphero la Hezekiya

14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga nayiwerenga pomwepo. Hezekiya anapita ku Nyumba ya Yehova ndipo anayika kalatayo pamaso pa Yehova. 15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova: 16 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pakati pa akerubi, Inu nokha ndiye Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Munalenga kumwamba ndi dziko lapansi. 17 Inu Yehova tcherani khutu ndipo mumve. Inu Yehova, tsekulani maso anu ndipo muone. Imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza, kunyoza Mulungu wamoyo.

18 “Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu yonse ya anthu ndi mayiko awo. 19 Iwo anaponyera pa moto milungu yawo ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mafano a mitengo ndi miyala, yopangidwa ndi manja a anthu. 20 Tsono Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni mʼdzanja lake kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndiye Mulungu.”

Yehova Ayankha Pemphero la Hezekiya

21 Tsono Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga wochokera kwa Yehova kwa Hezekiya poyankha pemphero lake lokhudza Senakeribu mfumu ya ku Asiriya. 22 Mawu amene Yehova wayankhula motsutsana naye ndi awa:

“Mwana wamkazi wa Ziyoni
    akukunyoza ndi kukuseka.
Mwana wamkazi wa Yerusalemu,
    akupukusa mutu wake pamene iwe ukuthawa.
23 Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira ndani?
    Kodi iwe wafuwulira
ndi kumuyangʼana monyada ndani?
    Watsutsana ndi Woyerayo wa Israeli!
24 Kudzera mwa amithenga ako
    iwe wanyoza Ambuye.
Ndipo wanena kuti,
    ‘Ndi magaleta anga ochuluka
ndafika pamwamba pa mapiri,
    pamwamba penipeni pa mapiri a Lebanoni.
Ndagwetsa mitengo yamkungudza yayitali kwambiri,
    ndi mitengo yabwino kwambiri ya payini.
Ndafika pa msonga pake penipeni,
    nkhalango yake yowirira kwambiri.
25 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo
    ndi kumva madzi akumeneko
ndi mapazi anga
    ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’

26 “Kodi sunamvepo
    kuti zimenezi ndinazikonzeratu kalekale?
Ndinazikonzeratu masiku amakedzana;
    tsopano ndazichitadi,
kuti iwe kwako nʼkusandutsa mizinda yotetezedwa
    kukhala milu ya miyala.
27 Anthu amene ankakhala kumeneko analibenso mphamvu,
    ankada nkhawa ndi kuchititsidwa manyazi.
Anali ngati mbewu za mʼmunda,
    ngati udzu wanthete,
ali ngati udzu omera pa denga,
    umene mphepo imawumitsa usanakule nʼkomwe.

28 “Koma Ine ndimadziwa zonse za iwe;
    ndimadziwa pamene ukuyima ndi pamene ukukhala; ndimadziwa pamene ukutuluka ndi pamene ukulowa,
    ndiponso momwe umandikwiyira Ine.
29 Chifukwa umandikwiyira Ine
    ndi kuti mwano wako wamveka mʼmakutu anga,
ndidzakola mphuno yako ndi mbedza
    ndikuyika chitsulo mʼkamwa mwako,
ndipo ndidzakubweza pokuyendetsa
    njira yomwe unadzera pobwera.

30 “Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi:

“Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha,
    ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha,
koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola,
    mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
31 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsalire
    adzazika mizu yawo pansi ndipo adzabereka zipatso poyera.
32 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala,
    ndi ku phiri la Ziyoni gulu la anthu opulumuka.
Changu cha Yehova Wamphamvuzonse
    chidzachita zimenezi.

33 “Choncho Yehova akunena izi za mfumu ya ku Asiriya:

“Iye sadzalowa mu mzinda umenewu
    kapena kuponyamo muvi uliwonse.
Sadzafika pafupi ndi mzindawu ndi ankhondo ake a zishango
    kapena kuwuzinga ndi mitumbira yankhondo.
34 Adzabwerera potsata njira yomwe anadzera pobwera;
    sadzalowa mu mzinda umenewu,”
            akutero Yehova.
35 “Ine ndidzawuteteza ndi kuwupulumutsa mzindawu,
    chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha pangano ndi mtumiki wanga Davide!”

36 Tsopano mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya nkhondo ya ku Asiriya ndikukapha asilikali 185,000. Podzuka mmawa mwake anthu anangoona mitembo ponseponse! 37 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anasasula misasa nʼkuchoka kubwerera kukakhala ku Ninive.

38 Tsiku lina, pamene ankapembedza mʼnyumba ya mulungu wake, Nisiroki, ana ake awiri, Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga, ndipo anathawira mʼdziko la Ararati. Ndipo mwana wake Esrahadoni analowa ufumu mʼmalo mwake.

Kudwala kwa Hezekiya

38 Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”

Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.

Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti: “Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako. Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.

“ ‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza: Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’ ” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.

Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:

10 Ine ndinaganiza kuti
    ndidzapita ku dziko la akufa
    pamene moyo ukukoma.
11 Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova,
    mʼdziko la anthu amoyo,
sindidzaonanso mtundu wa anthu
    kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 Nyumba yanga yasasuka
    ndipo yachotsedwa.
Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga,
    ngati munthu wowomba nsalu;
    kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa;
    koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango,
    ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba,
    ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula.
Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga.
    Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”

15 Koma ine ndinganene chiyani?
    Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi.
Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga,
    ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu.
    Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu.
Munandichiritsa ndi
    kundikhalitsa ndi moyo.
17 Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere
    kuti ndikhale ndi moyo;
Inu munandisunga
    kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko
chifukwa mwakhululukira
    machimo anga onse.
18 Pakuti akumanda sangathe kukutamandani,
    akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani.
Iwo amene akutsikira ku dzenje
    sangakukhulupirireni.
19 Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani,
    monga mmene ndikuchitira ine lero lino;
abambo amawuza ana awo za
    kukhulupirika kwanu.

20 Yehova watipulumutsa.
    Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe
masiku onse a moyo wathu
    mʼNyumba ya Yehova.

21 Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”

22 Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”

Nthumwi Zochokera ku Babuloni

39 Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira. Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.

Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?”

Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”

Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?”

Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”

Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse: Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe. Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”

Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”

Mawu a Chitonthozo kwa Anthu a Mulungu

40 Atonthozeni, atonthozeni anthu anga,
    akutero Mulungu wanu.
Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu
    ndipo muwawuzitse
kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha,
    tchimo lawo lakhululukidwa.
Ndawalanga mokwanira
    chifukwa cha machimo awo onse.

Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti,
“Konzani njira ya Yehova
    mʼchipululu;
wongolani njira zake;
    msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
Chigwa chilichonse achidzaze.
    Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse;
Dziko lokumbikakumbika alisalaze,
    malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera,
    ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona,
            pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”

Wina ananena kuti, “Lengeza.”
    Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani?

“Pakuti anthu onse ali ngati udzu
    ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota
    chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.”
    Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota,
    koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”

Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni,
    kwera pa phiri lalitali.
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu,
    fuwula kwambiri,
kweza mawu, usachite mantha;
    uza mizinda ya ku Yuda kuti,
    “Mulungu wanu akubwera!”
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu,
    ndipo dzanja lake likulamulira,
taonani akubwera ndi mphotho yake
    watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa:
    Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake
ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake
    ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.

12 Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake,
    kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake?
Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu,
    kapena kuyeza kulemera kwa
    mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
13 Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova
    kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
14 Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya,
    kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru?
Iye anapempha nzeru kwa yani
    ndi njira ya kumvetsa zinthu?

15 Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko.
    Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo;
    mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
16 Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe,
    ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
17 Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake;
    Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu
    ndi cha chabechabe.

18 Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani?
    Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
19 Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga
    ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide
    naliveka mkanda wasiliva.
20 Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere
    amasankha mtengo umene sudzawola,
nafunafuna mʼmisiri waluso woti
    amupangire fano limene silingasunthike.

21 Kodi simukudziwa?
    Kodi simunamve?
Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe?
    Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
22 Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi,
    Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala.
Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga,
    nayikunga ngati tenti yokhalamo.
23 Amatsitsa pansi mafumu amphamvu
    nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
24 Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene
    kapena kufesedwa chapompano,
    ndi kungoyamba kuzika mizu kumene
ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa
    ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.

25 Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani?
    Kapena kodi alipo wofanana nane?”
26 Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani.
    Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi?
Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo,
    nayitana iliyonse ndi dzina lake.
Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri,
    palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.

27 Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena
    ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti,
“Yehova sakudziwa mavuto anga,
    Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
28 Kodi simukudziwa?
    Kodi simunamve?
Yehova ndiye Mulungu wamuyaya,
    ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi.
Iye sadzatopa kapena kufowoka
    ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
29 Iye amalimbitsa ofowoka
    ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
30 Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka,
    ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
31 koma iwo amene amakhulupirira Yehova
    adzalandira mphamvu zatsopano.
Adzawuluka ngati chiwombankhanga;
    adzathamanga koma sadzalefuka,
    adzayenda koma sadzatopa konse.

Mulungu Thandizo la Israeli

41 “Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja!
    Alekeni ayandikire ndi kuyankhula;
tiyeni tikhale pamodzi
    kuti atiweruze.

“Ndani anadzutsa wochokera kummawa
    uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita?
Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake
    ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa
ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi
    nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
Amawalondola namayenda mosavutika,
    mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza,
    si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu?
Ine Yehova, ndine chiyambi
    ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”

Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa;
    anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera.
Akuyandikira pafupi, akubwera;
    aliyense akuthandiza mnzake
    ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide,
    ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo
    amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala.
Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.”
    Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.

“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga,
    Yakobo amene ndakusankha,
    Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi,
    ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi.
Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’
    Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe;
    usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako.
Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza,
    ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

11 “Onse amene akupsera mtima
    adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa;
onse amene akukangana nawe
    sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Udzafunafuna adani ako,
    koma sadzapezeka.
Iwo amene akuchita nawe nkhondo
    sadzakhalanso kanthu.
13 Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako,
    amene ndikukugwira dzanja lako lamanja
ndipo ndikuti, usaope;
    ndidzakuthandiza.
14 Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi,
    iwe wochepa mphamvu Israeli,
chifukwa Ine ndidzakuthandiza,”
    akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 “Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu
    chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri.
Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya,
    ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso
    adzamwazika ndi kamvuluvulu.
Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako,
    ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:

17 “Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi,
    koma sakuwapeza;
    ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu.
Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo;
    Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma,
    ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa.
Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi
    ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.