Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 74-77

Ndakatulo ya Asafu.

74 Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu?
    Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale,
    fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola,
    phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya
    chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.

Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe;
    anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo
    kuti adule mitengo mʼnkhalango.
Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo
    zonse zimene tinapachika.
Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi;
    anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.”
    Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa;
    palibe aneneri amene atsala
    ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.

10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu?
    Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja?
    Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!

12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale;
    Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu;
    munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani
    ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje,
    munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso;
    Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi;
    munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.

18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova,
    momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo;
    nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko
    asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi;
    osauka ndi osowa atamande dzina lanu.

22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu;
    kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu,
    chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo.

75 Tikuthokoza Inu Mulungu,
    tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe,
    anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.

Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera,
    ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera,
    ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba.
            Sela
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’
    ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba;
    musayankhule ndi khosi losololoka.’ ”

Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo
    kapena ku chipululu.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza:
    Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho
    chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera;
Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi
    amamwa ndi senga zake zonse.

Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya;
    ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa
    koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu.

76 Mulungu amadziwika mu Yuda;
    dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
Tenti yake ili mu Salemu,
    malo ake okhalamo mu Ziyoni.
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka,
    zishango ndi malupanga, zida zankhondo.
            Sela

Wolemekezeka ndinu,
    wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma,
    Iwowo amagona tulo tawo totsiriza;
palibe mmodzi wamphamvu
    amene angatukule manja ake.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo,
    kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa.
    Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo,
    ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze,
    kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko.
            Sela
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando
    ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.

11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse;
    anthu onse omuzungulira abweretse mphatso
    kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira;
    amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu.

77 Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo;
    ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye;
    usiku ndinatambasula manja mosalekeza
    ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.

Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula;
    ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka.
            Sela
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone
    ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
Ndinaganizira za masiku akale,
    zaka zamakedzana;
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku.
    Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,

“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya?
    Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu?
    Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima?
    Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”

10 Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso:
    zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova;
    Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 Ndidzakumbukira ntchito zanu
    ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”

13 Njira zanu Mulungu ndi zoyera.
    Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa;
    Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu,
    zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe.
            Sela

16 Madzi anakuonani Mulungu,
    madzi anakuonani ndipo anachita mantha;
    nyanja yozama inakomoka.
17 Mitambo inakhuthula madzi ake pansi,
    mu mlengalenga munamveka mabingu;
    mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu,
    mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse;
    dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Njira yanu inadutsa pa nyanja,
    njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu,
    ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.

20 Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa
    mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.