Beginning
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba.
51 Mundichitire chifundo, Inu Mulungu,
molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
molingana ndi chifundo chanu chachikulu
mufafanize mphulupulu zanga.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse
ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga,
ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa
ndipo ndachita zoyipa pamaso panu,
Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama
pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa,
wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga;
mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera,
munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo,
mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
9 Mufulatire machimo anga
ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu
ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
11 Musandichotse pamaso panu
kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu
ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu
kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu,
Mulungu wa chipulumutso changa,
ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga,
ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba.
Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka;
mtima wosweka ndi wachisoni
Inu Mulungu simudzawunyoza.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere;
mumange makoma a Yerusalemu.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo,
nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu;
ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”
52 Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?
Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,
iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
2 Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;
lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,
ntchito yako nʼkunyenga.
3 Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.
Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.
Sela
4 Umakonda mawu onse opweteka,
iwe lilime lachinyengo!
5 Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:
iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;
iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
6 Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;
adzamuseka nʼkumanena kuti,
7 “Pano tsopano pali munthu
amene sanayese Mulungu linga lake,
koma anakhulupirira chuma chake chambiri
nalimbika kuchita zoyipa!”
8 Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi
wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;
ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu
kwa nthawi za nthawi.
9 Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;
chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera
pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.
53 Chitsiru chimati mu mtima mwake,
“Kulibe Mulungu.”
Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano
pa ana a anthu
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
wofunafuna Mulungu.
3 Aliyense wabwerera,
iwo onse pamodzi akhala oyipa;
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,
ngakhale mmodzi.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;
anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,
ndipo sapemphera kwa Mulungu?
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu
pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.
Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;
inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!
Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,
lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”
54 Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;
onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 Imvani pemphero langa, Inu Mulungu
mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 Alendo akundithira nkhondo;
anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,
anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;
Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;
mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;
ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,
pakuti ndi labwino.
7 Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,
ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.
55 Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,
musakufulatire kupempha kwanga,
2 mverani ndipo mundiyankhe.
Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3 chifukwa cha mawu a adani anga,
chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;
pakuti andidzetsera masautso
ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4 Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;
mantha a imfa andigwera.
5 Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;
mantha aakulu andithetsa nzeru.
6 Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!
Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7 Ndikanathawira kutali
ndi kukakhala mʼchipululu.
8 Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;
kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9 Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;
pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;
nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;
kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine
ndikanapirira;
akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,
ndikanakabisala.
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,
bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala
pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;
alowe mʼmanda ali amoyo
pakuti choyipa chili pakati pawo.
16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu,
ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 Madzulo, mmawa ndi masana
ndimalira mowawidwa mtima,
ndipo Iye amamva mawu anga.
18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa
pa nkhondo imene yafika kulimbana nane,
ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya,
adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga,
chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa
ndipo saopa Mulungu.
20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake;
iye akuphwanya pangano ake.
21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala
komabe nkhondo ili mu mtima mwake;
mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta,
komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova
ndipo Iye adzakulimbitsani;
Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa
kulowa mʼdzenje lachiwonongeko;
anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo
sadzakhala moyo theka la masiku awo,
koma ine ndimadalira Inu.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati.
56 Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri;
tsiku lonse akundithira nkhondo.
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse,
ambiri akumenyana nane monyada.
3 Ndikachita mantha
ndimadalira Inu.
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,
mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.
Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga;
nthawi zonse amakonza zondivulaza.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira,
amayangʼanitsitsa mayendedwe anga
ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
7 Musalole konse kuti athawe;
mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
8 Mulembe za kulira kwanga,
mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu.
Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo
pamene ndidzalirira kwa Inu.
Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda,
mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha.
Kodi munthu angandichite chiyani?
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu;
ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa
ndi mapazi anga kuti ndingagwe,
kuti ndiyende pamaso pa Mulungu
mʼkuwala kwa moyo.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga.
57 Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo,
pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo.
Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu
mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba,
kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa,
kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri.
Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Ine ndili pakati pa mikango,
ndagona pakati pa zirombo zolusa;
anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi,
malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba;
mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde
ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa.
Anakumba dzenje mʼnjira yanga
koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu
mtima wanga ndi wokhazikika.
Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 Dzuka moyo wanga!
Dzukani zeze ndi pangwe!
Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu,
ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba;
kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba,
mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.