Beginning
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide.
9 Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse;
ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu;
Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 Adani anga amathawa,
iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga;
Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa;
Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani,
mwafafaniza mizinda yawo;
ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 Yehova akulamulira kwamuyaya;
wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo;
adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima,
linga pa nthawi ya mavuto.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu,
pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni;
lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira;
Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira!
Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 kuti ndilengeze za matamando anu
pa zipata za ana aakazi a Ziyoni,
kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba;
mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake;
oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo.
Higayoni. Sela
17 Oyipa amabwerera ku manda,
mitundu yonse imene imayiwala Mulungu.
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse,
kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane;
mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova;
mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba.
Sela
10 Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali?
Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
2 Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka,
amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
3 Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake;
amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
4 Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu;
mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
5 Zinthu zake zimamuyendera bwino;
iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali;
amanyogodola adani ake onse.
6 Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze.
Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
7 Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza;
zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
8 Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi,
kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa,
amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
9 Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba.
Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu;
amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
10 Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka;
amakhala pansi pa mphamvu zake.
11 Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala,
wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
12 Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu.
Musayiwale anthu opanda mphamvu.
13 Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu?
Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake,
“Iye sandiyimba mlandu?”
14 Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa,
mumaganizira zochitapo kanthu.
Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti
Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
15 Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa;
muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake
zimene sizikanadziwika.
16 Yehova ndi Mfumu kwamuyaya;
mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
17 Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa;
mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
18 Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa,
ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
11 Mwa Yehova ine ndimathawiramo.
Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti,
“Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
2 Pakuti taona oyipa akunga mauta awo;
ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta,
pobisala pawo kuti alase
olungama mtima.
3 Tsono ngati maziko awonongeka,
olungama angachite chiyani?”
4 Yehova ali mʼNyumba yake yoyera;
Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba.
Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu;
maso ake amawayesa.
5 Yehova amayesa olungama,
koma moyo wake umadana ndi oyipa,
amene amakonda zachiwawa.
6 Iye adzakhuthulira pa oyipa
makala amoto ndi sulufule woyaka;
mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
7 Pakuti Yehova ndi wolungama,
Iye amakonda chilungamo;
ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide.
12 Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika;
okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
2 Aliyense amanamiza mʼbale wake;
ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
3 Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo
ndi pakamwa paliponse podzikuza.
4 Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu;
pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
5 “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu
ndi kubuwula kwa anthu osowa,
Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova,
“Ndidzawateteza kwa owazunza.”
6 Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro
monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi,
oyengedwa kasanu nʼkawiri.
7 Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo
mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
8 Oyipa amangoyendayenda ponseponse
anthu akamayamikira zochita zawo.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
13 Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale?
Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
2 Ndidzalimbana ndi maganizo anga
ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti?
Mpaka liti adani anga adzandipambana?
3 Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga.
Walitsani maso anga kuti ndingafe;
4 mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,”
ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
5 Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika;
mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
6 Ine ndidzayimbira Yehova
pakuti wandichitira zokoma.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
14 Chitsiru chimati mu mtima mwake,
“Kulibe Mulungu.”
Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa;
palibe amene amachita zabwino.
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi,
kuyangʼana anthu onse
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
amene amafunafuna Mulungu.
3 Onse atembenukira kumbali,
onse pamodzi asanduka oyipa;
palibe amene amachita zabwino,
palibiretu ndi mmodzi yemwe.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse?
Akudya anthu anga ngati chakudya chawo
ndipo satamanda Yehova?
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu,
pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka,
koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni!
Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake,
Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
Salimo la Davide.
15 Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?
Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
2 Munthu wa makhalidwe abwino,
amene amachita zolungama,
woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,
amene sachitira choyipa mnansi wake
kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.
Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,
amene amakwaniritsa zomwe walonjeza
ngakhale pamene zikumupweteka,
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja
ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.
Iye amene amachita zinthu zimenezi
sadzagwedezeka konse.
Mikitamu ya Davide.
16 Ndisungeni Inu Mulungu,
pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
2 Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga;
popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
3 Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko,
amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
4 Anthu amene amathamangira kwa milungu ina
mavuto awo adzachulukadi.
Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi
kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
5 Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa;
mwateteza kolimba gawo langa.
6 Malire a malo anga akhala pabwino;
ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
7 Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu;
ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
8 Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.
Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja,
sindidzagwedezeka.
9 Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera;
thupi langanso lidzakhala pabwino,
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda,
simudzalola kuti woyera wanu avunde.
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo;
mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu,
ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.