Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yobu 35-37

35 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,

“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza?
    Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani,
    ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’

“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu
    pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone
    mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani?
    Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani?
    Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo,
    ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.

“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa;
    akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga,
    amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi
    ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye
    chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake;
    Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti
    Iye saona zimene zikuchitika.
Iye adzaweruza molungama ngati
    inu mutamudikira
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango,
    zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake,
    mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

36 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:

“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani
    kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali;
    ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Ndithudi mawu anga si abodza;
    wanzeru zangwiro ali ndi inu.

“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu;
    Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo
    koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama;
    amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu
    ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo,
    ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
Iye amawafotokozera zomwe anachita,
    kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake
    ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira,
    adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere,
    adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Koma ngati samvera,
    adzaphedwa ndi lupanga
    ndipo adzafa osadziwa kanthu.

13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo;
    akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Amafa akanali achinyamata,
    pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo;
    Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.

16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso,
    kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani,
    kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu;
    chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma;
    musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Kodi chuma chanu
    kapena mphamvu zanu zonse
    zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere,
    pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo,
    chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.

22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu.
    Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite,
    kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake
    zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo;
    anthuwo amaziona ali kutali.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe!
    Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.

27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo,
    timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 mitambo imagwetsa mvulayo
    ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera,
    momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse,
    zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu
    ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani,
    ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho;
    ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

37 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso
    ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,
    kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse
    ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.
    Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.
Pamene wabangula,
    palibe chimene amalephera kuchita.
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa
    Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’
    ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.
    Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
Zirombo zimakabisala
    ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,
    kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi
    ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,
    amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo
    mozungulirazungulira dziko lonse lapansi
    kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,
    kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.

14 “Abambo Yobu, tamvani izi;
    imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo
    ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,
    ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta
    pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo
    limene ndi lolimba ngati chitsulo?

19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;
    sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?
    Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,
    ndi kunyezimira mlengalenga,
    kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;
    Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;
    pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,
    kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.