Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yobu 29-31

29 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:

“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi,
    masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
pamene nyale yake inkandiwunikira
    ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri,
    pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane,
    ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka,
    ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.

“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda
    ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
anyamata amati akandiona ankapatuka
    ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
atsogoleri ankakhala chete
    ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 anthu otchuka ankangoti duu,
    ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga,
    ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo,
    ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa;
    ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa;
    chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya;
    ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi;
    ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa
    ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.

18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga,
    masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi,
    ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine,
    ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’

21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi,
    ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso;
    mawu anga ankawagwira mtima.
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula
    ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira;
    kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu;
    ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo;
    ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

30 “Koma tsopano akundinyoza,
    ana angʼonoangʼono kwa ine,
anthu amene makolo awo sindikanawalola
    kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine,
    pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Anali atatheratu kuwonda ndi njala,
    ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi,
    mʼchipululu usiku.
Ankathyola therere ndi masamba owawa,
    ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo,
    akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma,
    pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
Ankalira ngati nyama kuthengo
    ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina,
    anathamangitsidwa mʼdziko.

“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe;
    ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa;
    akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa,
    iwowo analekeratu kundiopa.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane;
    andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda,
    andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 Iwo anditsekera njira;
    akufuna kundichititsa ngozi,
    popanda wina aliyense wowaletsa.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka,
    iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu;
    ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo,
    chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.

16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo;
    ndili mʼmasiku amasautso.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti
    zowawa zanga sizikuleka.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa;
    Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 Wandiponya mʼmatope,
    ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.

20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha;
    ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza;
    mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo;
    mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa,
    kumalo kumene amoyo onse adzapitako.

24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima,
    amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto?
    Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera;
    pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka;
    ndili mʼmasiku amasautso.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa;
    ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe,
    mnzawo wa akadzidzi.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka;
    thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro,
    ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

31 “Ndinachita pangano ndi maso anga
    kuti sindidzapenya namwali momusirira.
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani?
    Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa,
    tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Kodi Mulungu saona zochita zanga,
    ndi kudziwa mayendedwe anga?

“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso,
    kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama
    ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
ngati mayendedwe anga asempha njira,
    ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona,
    kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala,
    ndipo zomera zanga zizulidwe.

“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi,
    ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya,
    ndipo amuna ena azigona naye.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi,
    tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko;
    ukanapsereza zokolola zanga.

13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi,
    pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa?
    Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo?
    Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?

16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba,
    kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha,
    wosagawirako mwana wamasiye,
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake,
    ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa,
    kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo
    chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye,
    poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke,
    mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu,
    ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.

24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma
    kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri,
    zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala,
    kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo
    nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo,
    chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.

29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga,
    kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga
    potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti,
    ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse,
    pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena,
    kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 chifukwa choopa gulu la anthu,
    ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko
    kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.

35 “Aa, pakanakhala wina wondimva!
    Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe;
    mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa,
    ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita;
    ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.

38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine
    ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama
    kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu
    ndi udzu mʼmalo mwa barele.”

Mawu a Yobu athera pano.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.