Beginning
Mawu a Bilidadi
8 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti?
Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama?
Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu,
Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Koma utayangʼana kwa Mulungu,
ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima
ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako
ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa
koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 “Funsa kwa anthu amvulazakale
ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse,
ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera?
Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho?
Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula;
zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu;
ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka;
zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka;
amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa,
nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala
ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo,
pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Ndithudi chomeracho chimafota,
ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa
kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete
ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Adani ako adzachita manyazi,
ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”
Mawu a Yobu
9 Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona.
Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye,
Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka.
Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa,
ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake
ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala;
Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba
ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana,
nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,
zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona;
akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa?
Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake;
ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji?
Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe;
ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera,
sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho,
ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso
koma akanandichulukitsira zowawa.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi!
Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa;
ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa,
sindidziyenereza ndekha;
moyo wanga ndimawupeputsa.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti,
‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi,
Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa
Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo.
Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro;
masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja,
ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga,
ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 ndikuopabe mavuto anga onse,
popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa
ndivutikirenji popanda phindu?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri
ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 mutha kundiponyabe pa dzala,
kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha,
sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu,
kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine
kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo,
koma monga zililimu, sindingathe.
10 “Ine ndatopa nawo moyo wanga;
choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka
ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa,
koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza,
kunyoza ntchito ya manja anu,
chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu?
Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu,
kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga
ndi kulondola tchimo langa,
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa
ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu.
Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi,
kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale,
suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu
ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu,
ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu,
ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa
ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa!
Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga,
pakuti ndagwidwa ndi manyazi
ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango
ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane
ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi
magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe?
Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
19 Ndikanapanda kubadwa,
kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha?
Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako
ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
22 ku dziko la mdima wandiweyani
ndi chisokonezo,
kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.