Beginning
Fuko la Isakara
7 Ana a Isakara anali awa:
Tola, Puwa, Yasubu ndi Simironi ndipo onse analipo anayi.
2 Ana a Tola ndi awa:
Uzi, Refaya, Yerieli, Yahimai, Ibisamu ndi Samueli. Awa anali atsogoleri a mabanja awo. Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide zidzukulu za Tola zomwe zinali anthu odziwa kumenya nkhondo zinalipo 22,600.
3 Mwana wa Uzi anali
Izirahiya.
Ana a Izirahiya anali:
Mikayeli, Obadiya, Yoweli ndi Isiya. Onse asanu anali atsogoleri a mabanja. 4 Monga mwa chiwerengero cha mabanja awo, panali anthu 36,000 odziwa kumenya nkhondo, pakuti iwo anali ndi akazi ndi ana ambiri.
5 Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo.
Fuko la Benjamini
6 Ana atatu a Benjamini anali awa:
Bela, Bekeri ndi Yediaeli.
7 Ana a Bela anali awa:
Eziboni, Uzi, Uzieli, Yerimoti ndi Iri. Iwowa anali atsogoleri a mabanja awo ndipo onse pamodzi analipo asanu. Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali anthu 22,034 odziwa kumenya nkhondo.
8 Ana a Bekeri anali awa:
Zemira, Yowasi, Eliezara, Eliyoenai, Omiri, Yeremoti, Abiya, Anatoti ndi Alemeti. Onsewa anali ana a Bekeri. 9 Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali atsogoleri a mabanja ndi anthu 20,200 odziwa kumenya nkhondo.
10 Mwana wa Yediaeli anali
Bilihani.
Ana a Bilihani anali awa:
Yeusi, Benjamini, Ehudi, Kenaana, Zetani, Tarisisi ndi Ahisahara. 11 Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo.
12 Asupi ndi Ahupi anali zidzukulu za Iri, ndipo Ahusimu anali zidzukulu za Aheri.
Fuko la Nafutali
13 Ana a Nafutali anali awa:
Yahazieli, Guni, Yezeri ndi Salumu, zidzukulu za Biliha.
Fuko la Manase
14 Ana a Manase anali awa:
Asirieli ndi mwana amene anabereka kwa mzikazi wake wa ku Aramu. Mzikazi yemweyo anaberekanso Makiri abambo ake a Giliyadi. 15 Makiri anatenga mkazi wa banja la Ahupi ndi Asupi. Mlongo wake anali Maaka.
Mwana wake wina anali Zelofehadi, amene anabereka ana aakazi okhaokha.
16 Maaka mkazi wa Makiri anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Perezi. Mʼbale wake anamutcha Seresi, ndipo ana ake anali Ulamu ndi Rakemu.
17 Mwana wa Ulamu anali
Bedani.
Awa anali ana a Giliyadi mwana wa Makiri, mwana wa Manase. 18 Mlongo wake Hamoleketi anabereka Isihodi, Abiezeri ndi Mahila.
19 Ana a Semida anali:
Ahiyani, Sekemu, Likihi ndi Aniyamu.
Fuko la Efereimu
20 Ana a Efereimu anali awa:
Sutela, Beredi,
Tahati, Eliada,
Tahati, 21 Zabadi,
Sutela.
Ezeri ndi Eladi anaphedwa ndi anthu a ku Gati, pamene anabwera kudzalanda zoweta zawo. 22 Efereimu, abambo awo, anawalira masiku ambiri, ndipo abale ake anabwera kudzamutonthoza. 23 Kenaka anagona ndi mkazi wake, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Beriya, chifukwa tsoka linagwera banja lake. 24 Mwana wake wamkazi anali Seera, amene anamanga mzinda wa Beti-Horoni Wakumunsi, Wakumtunda kudzanso Uzeni-Seera.
25 Mwana wina wa Efereimu anali Refa amene zidzukulu zake zinali Resefu,
Tela, Tahani,
26 Ladani, Amihudi,
Elisama, 27 Nuni
ndi Yoswa.
28 Malo amene ankakhala anali Beteli ndi midzi yozungulira, cha kummawa kunali Naarani, Gezeri ndi midzi yake ya kumadzulo ndi Sekemu ndi midzi yake mpaka ku Aya ndi midzi yake. 29 Mʼmbali mwa malire a Manase munali Beti-Seani, Taanaki, Megido ndi Dori, pamodzi ndi midzi yake. Zidzukulu za Yosefe mwana wa Israeli zimakhala mʼmizinda imeneyi.
Fuko la Aseri
30 Ana a Aseri anali awa:
Imuna, Isiva, Isivi ndi Beriya. Mlongo wawo anali Sera.
31 Ana a Beriya anali awa:
Heberi ndi Malikieli amene anabereka Birizaiti.
32 Heberi anabereka Yafuleti, Someri, Hotamu ndi Suwa, mlongo wawo.
33 Ana a Yafuleti anali awa:
Pasaki, Bimuhali ndi Asivati.
Awa anali ana a Yafuleti.
34 Ana a Someri anali awa:
Ahi, Rohiga, Yehuba ndi Aramu.
35 Ana a mʼbale wake Helemu anali awa:
Zofa, Imuna, Selesi ndi Amali.
36 Ana a Zofa anali awa:
Suwa, Harineferi, Suwali, Beri, Imula, 37 Bezeri, Hodi, Sama, Silisa, Itirani ndi Bera.
38 Ana a Yeteri anali awa:
Yefune, Pisipa ndi Ara.
39 Ana a Ula anali awa:
Ara, Hanieli ndi Riziya.
40 Onsewa anali zidzukulu za Aseri, atsogoleri a mabanja, anthu omveka, ankhondo olimba mtima, ndi akuluakulu pakati pa atsogoleri anzawo. Chiwerengero cha anthu odziwa kumenya nkhondo chomwe chinalembedwa chinali 26,000.
Adzukulu a Benjamini ndi Sauli
8 Benjamini anabereka Bela mwana wake woyamba,
wachiwiri Asibeli, wachitatu Ahara,
2 wachinayi Noha ndipo wachisanu Rafa.
3 Ana a Bela anali awa:
Adari, Gera, Abihudi, 4 Abisuwa, Naamani, Ahowa, 5 Gera, Sefufani ndi Hiramu.
6 Zidzukulu za Ehudi, zimene zinali atsogoleri a mabanja a amene amakhala ku Geba ndipo zinasamutsidwa kupita ku Manahati zinali izi:
7 Naamani, Ahiya ndi Gera, amene anawasamutsa ndipo anabereka Uza ndi Ahihudi.
8 Saharaimu anabereka ana ku Mowabu atalekana ndi akazi ake, Husimu ndi Baara. 9 Mwa mkazi wake Hodesi anabereka Yobabu, Zibiya, Mesa, Malikamu, 10 Yeusi, Sakiya ndi Mirima. Awa ndiye ana ake, atsogoleri a mabanja awo. 11 Mwa mkazi wake Husimu anabereka Abitubi ndi Elipaala.
12 Ana a Elipaala anali awa:
Eberi, Misamu, Semedi (amene anamanga mizinda ya Ono ndi Lodi ndi midzi yake yozungulira) 13 ndiponso Beriya ndi Sema, amene anali atsogoleri a mabanja a amene ankakhala ku Ayaloni ndipo anathamangitsa nzika za ku Gati.
14 Ahiyo, Sasaki, Yeremoti, 15 Zebadiya, Aradi, Ederi, 16 Mikayeli, Isipa ndi Yoha anali ana a Beriya.
17 Zebadiya, Mesulamu, Hiziki, Heberi, 18 Isimerai, Iziliya ndi Yobabu anali ana a Elipaala.
19 Yakimu, Zikiri, Zabidi, 20 Elienai, Ziletai, Elieli, 21 Adaya, Beraya ndi Simirati anali ana a Simei.
22 Isipani, Eberi, Elieli, 23 Abidoni, Zikiri, Hanani, 24 Hananiya, Elamu, Anitotiya, 25 Ifideya ndi Penueli anali ana a Sasaki.
26 Samuserai, Sehariya, Ataliya, 27 Yaaresiya, Eliya ndi Zikiri anali ana a Yerohamu.
28 Onsewa anali atsogoleri a mabanja, anthu otchuka potsata mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.
29 Yeiyeli amene amabereka Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni.
Dzina la mkazi wake linali Maaka, 30 ndipo mwana wake woyamba anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu, 31 Gedori, Ahiyo, Zekeri 32 ndi Mikiloti, amene anabereka Simea. Iwowa ankakhalanso ku Yerusalemu ndi abale awo.
33 Neri anabereka Kisi. Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.
34 Mwana wa Yonatani anali
Meri-Baala, amene anabereka Mika.
35 Ana a Mika anali awa:
Pitoni, Meleki, Tareya ndi Ahazi.
36 Ahazi anabereka Yehoyada, Yehoyada anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimuri anabereka Moza. 37 Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Rafa, Eleasa ndi Azeli.
38 Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi, ndipo mayina awo anali awa:
Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Onsewa anali ana a Azeli.
39 Ana a Eseki mʼbale wake anali awa:
Mwana wake woyamba Ulamu, wachiwiri Yeusi ndipo wachitatu Elifeleti. 40 Ana a Ulamu anali asilikali olimba mtima amene amadziwa kugwiritsa ntchito uta. Iwo anali ndi ana ndi adzukulu ambiri ndipo onse analipo 150.
Onsewa anali adzukulu a Benjamini.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.