Beginning
Mtumiki wa Yehova
49 Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba
tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali:
Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe,
ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
2 Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa,
anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake;
Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa
ndipo anandibisa mʼchimake.
3 Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli.
Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
4 Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito
ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe,
koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova,
ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
5 Yehova anandiwumba ine
mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake
kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye
ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye,
choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova,
ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
6 Yehovayo tsono akuti,
“Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga,
kuti udzutse mafuko a Yakobo
ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka.
Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira,
udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
7 Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula,
Woyerayo wa Israeli akunena,
amene mitundu ya anthu inamuda,
amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti,
“Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira.
Akalonga nawonso adzagwada pansi.
Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika
ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
Kubwezeretsedwa kwa Israeli
8 Yehova akuti,
“Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha,
ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza;
ndinakusunga ndi kukusandutsa
kuti ukhale pangano kwa anthu,
kuti dziko libwerere mwakale
ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
9 Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke
ndi a mu mdima kuti aonekere poyera.
“Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira
ndi msipu pa mʼmalo owuma.
10 Iwo sadzamva njala kapena ludzu,
kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza;
chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera
ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
11 Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo,
ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
12 Taonani, anthu anga adzachokera kutali,
ena kumpoto, ena kumadzulo,
enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga;
kondwera, iwe dziko lapansi;
imbani nyimbo inu mapiri!
Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,
ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya,
Ambuye wandiyiwala.”
15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere
ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni?
Ngakhale iye angathe kuyiwala,
Ine sindidzakuyiwala iwe!
16 Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga;
makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
17 Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira,
ndipo amene anakupasula akuchokapo.
18 Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane
ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe.
Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo,
anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa
chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
19 “Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa
ndipo dziko lako ndi kusakazidwa,
chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera
ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
20 Ana obadwa nthawi yako yachisoni
adzanena kuti,
‘Malo ano atichepera,
tipatse malo ena woti tikhalemo.’
21 Tsono iwe udzadzifunsa kuti,
‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa?
Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena;
ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa.
Ndani anawalera ana amenewa?
Ndinatsala ndekha,
nanga awa, achokera kuti?’ ”
22 Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi,
“Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere.
Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere.
Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo
ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
23 Mafumu adzakhala abambo wongokulera
ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera.
Iwo adzagwetsa nkhope
zawo pansi.
Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova;
iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
24 Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo,
kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
25 Koma zimene Yehova akunena ndi izi,
“Ankhondo adzawalanda amʼndende awo,
ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo;
ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu,
ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
26 Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe;
adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo.
Zikadzatero anthu onse adzadziwa
kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu,
Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”
Tchimo la Israeli, Kumvera kwa Mtumiki
50 Yehova akuti,
“Kalata imene ndinasudzulira amayi
anu ili kuti?
Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole,
ndinakugulitsani kwa ati?
Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu;
amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
2 Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu?
Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha?
Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani?
Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani?
Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu,
mitsinje ndinayisandutsa chipululu;
nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi;
ndipo zinafa ndi ludzu.
3 Ndinaphimba thambo ndi mdima
ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
4 Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula
kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka.
Mmawa mulimonse amandidzutsa,
amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
5 Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga,
ndipo sindinakhale munthu wowukira
ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
6 Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya
masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu;
sindinawabisire nkhope yanga
anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
7 Popeza Ambuye Yehova amandithandiza,
sindidzachita manyazi.
Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi,
chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
8 Wondikhalira kumbuyo ali pafupi,
ndaninso amene adzandiyimba mlandu?
Abwere kuti tionane maso ndi maso!
Mdani wanga ndi ndani?
Abweretu kuti tilimbane!
9 Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza.
Ndaninso amene adzanditsutsa?
Onse adzatha ngati chovala
chodyedwa ndi njenjete.
10 Ndani mwa inu amaopa Yehova
ndi kumvera mawu a mtumiki wake?
Aliyense woyenda mu mdima,
popanda chomuwunikira,
iye akhulupirire dzina la Yehova
ndi kudalira Mulungu wake.
11 Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto
ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu,
lowani mʼmoto wanu womwewo.
Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa.
Ndipo ine Yehova
ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.
Chipulumutso Chamuyaya cha Ziyoni
51 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso
ndiponso amene mumafunafuna Yehova:
Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa
ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu,
ndi Sara, amene anakubalani.
Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana,
koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni,
ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse;
Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni,
malo ake owuma ngati munda wa Yehova.
Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda
ndi kundiyamika.
4 “Mverani Ine, anthu anga:
tcherani khutu, inu mtundu wanga:
malangizo adzachokera kwa Ine;
cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga.
Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga;
ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse.
Mayiko akutali akundiyembekezera.
Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
6 Kwezani maso anu mlengalenga,
yangʼanani pansi pa dziko;
mlengalenga udzazimirira ngati utsi,
dziko lapansi lidzatha ngati chovala
ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe.
Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya,
chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi,
anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu;
musaope kudzudzulidwa ndi anthu
kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala;
mbozi idzawadya ngati thonje.
Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya,
chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe,
Inu Yehova;
dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana,
monga nthawi ya mibado yakale.
Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe,
amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu,
madzi ozama kwambiri aja?
Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama,
kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera
nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa;
chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo.
Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe,
chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima.
Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa?
Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu,
amene anayala za mlengalenga
ndi kuyika maziko a dziko lapansi.
Inu nthawi zonse mumaopsezedwa
chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani
amene angofuna kukuwonongani.
Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa;
sadzalowa mʼmanda awo,
kapena kusowa chakudya.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma.
Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu
ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa.
Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga,
ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi,
ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’ ”
Kutha kwa Mavuto A Yerusalemu
17 Dzambatuka, dzambatuka!
Imirira iwe Yerusalemu.
Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo
chimene Yehova anakupatsa.
Iwe amene unagugudiza
chikho chochititsa chizwezwe.
18 Mwa ana onse amene anabereka,
panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera;
mwa ana onse amene analera,
panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe.
Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga.
Ndani angakumvere chisoni?
Ndani angakutonthoze?
20 Ana ako akomoka;
ali lambalamba pa msewu,
ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde.
Ukali wa Yehova
ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika,
iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
22 Ambuye Yehova wanu,
Mulungu amene amateteza anthu ake akuti,
“Taona, ndachotsa mʼdzanja lako
chikho chimene chimakuchititsa kudzandira;
sudzamwanso chikho
cha ukali wanga.
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza,
amene ankakuwuza kuti,
‘gona pansi tikuyende pa msana.’
Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo,
ngati msewu woti ayendepo.”
52 Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni,
vala zilimbe.
Vala zovala zako zokongola,
iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika.
Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa
sadzalowanso pa zipata zako.
2 Sasa fumbi lako;
imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu.
Inu omangidwa a ku Ziyoni,
masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
3 Pakuti Yehova akuti,
“Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani,
choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
4 Pakuti Ambuye Yehova akuti,
“Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto;
nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
5 Tsopano Ine Yehova ndikuti,
“Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu,
amene amawalamulira amawanyoza,”
akutero Yehova.
“Ndipo tsiku lonse, akungokhalira
kuchita chipongwe dzina langa.
6 Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa;
kotero adzadziwa
kuti ndi Ine amene ndikuyankhula,
Indedi, ndine.”
7 Ngokongoladi mapazi a
amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri.
Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere,
chisangalalo ndi chipulumutso.
Iwo akubwera kudzawuza anthu
a ku Ziyoni kuti,
“Mulungu wako ndi mfumu!”
8 Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo;
akuyimba pamodzi mwachimwemwe.
Popeza akuona chamaso
kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
9 Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe,
inu mabwinja a Yerusalemu,
pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,
wapulumutsa Yerusalemu.
10 Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika
pamaso pa anthu a mitundu yonse,
ndipo anthu onse a dziko lapansi
adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
11 Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko!
Musakhudze kanthu kodetsedwa!
Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova
tulukanimo ndipo mudziyeretse.
12 Koma simudzachoka mofulumira
kapena kuchita chothawa;
pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu,
Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
Kuzunzika ndi Ulemerero wa Mtumiki
13 Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake
adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
14 Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka,
chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu.
Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
15 Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye,
ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye.
Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona,
ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.
53 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi;
kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake,
ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma.
Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira,
analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu,
munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa,
ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona.
Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife;
ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu.
Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga,
kumukantha ndi kumusautsa.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu,
ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu;
iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere,
ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera,
aliyense mwa ife akungodziyendera;
ndipo Yehova wamusenzetsa
zoyipa zathu zonse.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa,
koma sanayankhule kanthu.
Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira,
kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta,
momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha.
Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake,
poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo?
Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa
ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma,
ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa,
kapena kuyankhula za chinyengo.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa.
Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa.
Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali,
ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Atatha mazunzo a moyo wake,
adzaona kuwala, ndipo adzakhutira.
Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri,
popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu,
adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu,
popeza anapereka moyo wake mpaka kufa,
ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe.
Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri,
ndipo anawapempherera anthu olakwa.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.