Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Mlaliki 5-8

Lemekeza Mulungu

Uzisamala mayendedwe ako pamene ukupita ku nyumba ya Mulungu. Upite pafupi kuti ukamvetsere mʼmalo mopereka nsembe ya zitsiru zimene sizizindikira kuti zikuchita zolakwa.

Usamafulumire kuyankhula,
    usafulumire mu mtima mwako
    kunena chilichonse pamaso pa Mulungu.
Mulungu ali kumwamba
    ndipo iwe uli pa dziko lapansi,
    choncho mawu ako akhale ochepa.
Kuchuluka kwa mavuto mu mtima kumabweretsa maloto oyipa,
    ndipo kuchuluka kwa mawu kumadzetsa uchitsiru.

Pamene ulumbira kwa Mulungu usachedwe kukwaniritsa chimene walumbiracho. Iye sakondweretsedwa ndi chitsiru; kwaniritsa lumbiro lako. Kuli bwino kusalumbira kusiyana ndi kulumbira koma osakwaniritsa lumbirolo. Pakamwa pako pasakuchimwitse. Ndipo usanene kwa mthenga wa mʼNyumba ya Mulungu kuti, “Ndinalakwitsa polumbira.” Chifukwa chiyani ukufuna Mulungu akwiye ndi mawu ako ndiponso ntchito ya manja ako? Maloto ochuluka ndi mawu ochuluka ndi zinthu zopandapake. Kotero lemekeza Mulungu.

Chuma Nʼchopandapake

Ngati uwona anthu osauka akuzunzika mʼdziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzawo ndi kuwalanda ufulu wawo, usadabwe ndi zinthu zimenezi; pakuti woyangʼanira ali naye wina womuyangʼanira wamkulu, ndipo pamwamba pa awiriwa pali ena akuluakulu owaposa. Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.

10 Aliyense amene amakonda ndalama sakhutitsidwa ndi ndalamazo;
    aliyense amene amakonda chuma sakhutitsidwa ndi zimene amapeza.
    Izinso ndi zopandapake.

11 Chuma chikachuluka
    akudya nawo chumacho amachulukanso.
Nanga mwini wake amapindulapo chiyani
    kuposa kumangochiyangʼana ndi maso ake?

12 Wantchito amagona tulo tabwino
    ngakhale adye pangʼono kapena kudya kwambiri,
koma munthu wolemera, chuma
    sichimulola kuti agone.

13 Ine ndinaona choyipa chomvetsa chisoni pansi pano:

chuma chokundikidwa chikupweteka mwini wake yemwe,
14     kapena chuma chowonongedwa pa nthawi yatsoka,
kotero kuti pamene wabereka mwana
    alibe kanthu koti amusiyire.
15 Munthu anabadwa wamaliseche kuchokera mʼmimba mwa amayi ake,
    ndipo monga iye anabadwira, adzapitanso choncho.
Pa zonse zimene iye anakhetsera thukuta
    palibe nʼchimodzi chomwe chimene adzatenge mʼmanja mwake.

16 Izinso ndi zoyipa kwambiri:

munthu adzapita monga momwe anabwerera,
    ndipo iye amapindula chiyani,
    pakuti amagwira ntchito yolemetsa yopanda phindu?
17 Masiku ake onse ndi odzaza ndi mdima,
    kukhumudwa kwakukulu, masautso ndi nkhawa.

18 Tsono ndinazindikira kuti nʼchabwino ndi choyenera kuti munthu azidya ndi kumwa, ndi kukhutitsidwa ndi ntchito yake yolemetsa imene amayigwira pansi pano pa nthawi yake yochepa imene Mulungu amamupatsa, poti ichi ndiye chake. 19 Komatu pamene Mulungu apereka chuma kwa munthu aliyense ndi zinthu zina, ndi kulola kuti akondwere ndi chumacho, munthuyo alandire chumacho ndi kusangalala ndi ntchito yake, imene ndi mphatso yochokera kwa Mulungu. 20 Munthu wotereyu saganizirapo za masiku a moyo wake, chifukwa Mulungu amamutanganidwitsa ndi chisangalalo cha mu mtima mwake.

Ine ndinaona choyipa china pansi pano, ndipo chimasautsa anthu kwambiri: Mulungu amapereka chuma, zinthu ndi ulemu kwa munthu, kotero kuti munthuyo sasowa kanthu kalikonse kamene akukalakalaka, koma Mulungu samulola kuti adyerere zinthuzo, ndipo mʼmalo mwake amadyerera ndi mlendo. Izi ndi zopandapake, ndi zoyipa kwambiri.

Ngakhale munthu atabereka ana 100 ndi kukhala ndi moyo zaka zambiri; komatu ngakhale atakhala zaka zambiri chotani, ngati iye sangadyerere chuma chake ndi kuyikidwa mʼmanda mwaulemu, ine ndikuti mtayo umamuposa iyeyo. Mtayo umangopita pachabe ndipo umapita mu mdima, ndipo mu mdimamo dzina lake limayiwalika. Ngakhale kuti mtayowo sunaone dzuwa kapena kudziwa kanthu kalikonse, koma umapumula kuposa munthu uja, ngakhale munthuyo atakhala ndi moyo zaka 2,000, koma ndi kulephera kudyerera chuma chake. Kodi onsewa sapita malo amodzi?

Ntchito yonse ya munthu imathera pakamwa pake,
    komatu iye sakhutitsidwa ndi pangʼono pomwe.
Kodi munthu wanzeru
    amaposa motani chitsiru?
Kodi munthu wosauka amapindula chiyani
    podziwa kukhala bwino pamaso pa anthu ena?
Kuli bwino kumangoona zinthu ndi maso
    kusiyana ndi kumangozilakalaka mu mtima.
Izinso ndi zopandapake,
    nʼkungodzivuta chabe.

10 Chilichonse chimene chilipo anachitchula kale dzina,
    za mmene munthu alili nʼzodziwika;
sangathe kutsutsana ndi munthu
    amene ali wamphamvu kupambana iyeyo.
11 Mawu akachuluka
    zopandapake zimachulukanso,
    nanga munthu zimamupindulira chiyani?

12 Pakuti ndani amene amadziwa chomwe ndi chabwino pa moyo wa munthu, pakuti moyo wake ndi wa masiku ochepa ndi opandapake, umangopitira ngati mthunzi. Ndani amene angamufotokozere zimene zidzachitika pansi pano iye atapita?

Nzeru

Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino,
    ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro
    kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero:
Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense;
    anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka,
    pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa,
    koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru
    kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
Kuseka kwa zitsiru kuli ngati
    kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika,
    izinso ndi zopandapake.

Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru,
    ndipo chiphuphu chimawononga mtima.

Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake,
    ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako,
    pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.

10 Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?”
    pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.

11 Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino
    ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
12 Nzeru ndi chitetezo,
    monganso ndalama zili chitetezo,
koma phindu la chidziwitso ndi ili:
    kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.

13 Taganizirani zimene Mulungu wazichita:

ndani angathe kuwongola chinthu
    chimene Iye anachipanga chokhota?
14 Pamene zinthu zili bwino, sangalala;
    koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino:
Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo,
    ndiponso nthawi imene si yabwinoyo.
Choncho munthu sangathe kuzindikira
    chilichonse cha mʼtsogolo mwake.

15 Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi:

munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake,
    ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
16 Usakhale wolungama kwambiri
    kapena wanzeru kwambiri,
    udziwonongerenji wekha?
17 Usakhale woyipa kwambiri,
    ndipo usakhale chitsiru,
    uferenji nthawi yako isanakwane?
18 Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi,
    ndipo usataye njira inayo.
    Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.

19 Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru
    kupambana olamulira khumi a mu mzinda.

20 Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi
    amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.

21 Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula,
    mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
22 pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako
    kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.

23 Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati,

“Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,”
    koma nzeruyo inanditalikira.
24 Nzeru zimene zilipo,
    zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri,
    ndani angathe kuzidziwa?
25 Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe,
    ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira
ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru
    ndiponso kupusa kwake kwa misala.

26 Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa,
    mkazi amene ali ngati khoka,
amene mtima wake uli ngati khwekhwe,
    ndipo manja ake ali ngati maunyolo.
Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo,
    koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.

27 Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi:

“Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
28     pamene ine ndinali kufufuzabe
    koma osapeza kanthu,
ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000,
    koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
29 Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi:
    Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama,
    koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”
Ndani angafanane ndi munthu wanzeru?
    Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu?
Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu
    ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.

Za Kumvera Mfumu

Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu. Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho. Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”

Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse,
    ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse,
    ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.

Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo,
    ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga,
    choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake.
Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa,
    kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.

Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza. 10 Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.

11 Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa. 12 Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu. 13 Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.

14 Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino. 15 Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.

16 Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku, 17 pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.