Beginning
Lamedi
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya;
akhazikika kumwambako.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse;
Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino,
pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa,
ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu,
pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni;
pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge,
koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire,
koma malamulo anu alibe malire konse.
Memu
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu!
Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga,
popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse
popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba,
popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa
kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu,
pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa,
otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu;
kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Nuni
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga
ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza,
kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Ndazunzika kwambiri;
Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga,
ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi,
sindidzayiwala malamulo anu.
110 Anthu oyipa anditchera msampha,
koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya;
Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu
mpaka kumapeto kwenikweni.
Samekhi
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri,
koma ndimakonda malamulo anu.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa;
chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa,
kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa;
nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu,
pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala;
nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu;
ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Ayini
121 Ndachita zolungama ndi zabwino;
musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino,
musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu,
kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa,
kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu;
malamulo anu akuswedwa.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu
kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka,
ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Pe
129 Maumboni anu ndi odabwitsa
nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika;
ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu,
kufunafuna malamulo anu.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo,
monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu;
musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza,
kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga,
chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Tsade
137 Yehova ndinu wolungama,
ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;
ndi odalirika ndithu.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga
chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri
nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,
sindiyiwala malangizo anu.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya,
ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera,
koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Kofu
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova,
ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni
ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;
chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,
kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira,
koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi,
malamulo anu onse ndi woona.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu
kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Reshi
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola;
sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa,
pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu;
sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri,
koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro,
popeza samvera mawu anu.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu;
sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Mawu anu onse ndi owona;
malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Sini ndi Shini
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa,
koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu,
ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho,
koma ndimakonda malamulo anu.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku
pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu,
ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova,
ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Ndimamvera umboni wanu
pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu,
pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Tawu
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova;
patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu;
pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga,
pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu,
popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza
pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova,
ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,
ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika,
funafunani mtumiki wanu,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.