Book of Common Prayer
BUKU LACHIWIRI
Masalimo 42–72
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.
42 Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi,
kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
2 Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo.
Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
3 Misozi yanga yakhala chakudya changa
usana ndi usiku,
pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti,
“Mulungu wako ali kuti?”
4 Zinthu izi ndimazikumbukira
pamene ndikukhuthula moyo wanga:
momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu,
kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu
ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko
pakati pa anthu a pa chikondwerero.
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga?
Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?
Yembekezera Mulungu,
pakuti ndidzamulambirabe,
Mpulumutsi wanga ndi 6 Mulungu wanga.
Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga
kotero ndidzakumbukira Inu
kuchokera ku dziko la Yorodani,
ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
7 Madzi akuya akuyitana madzi akuya
mu mkokomo wa mathithi anu;
mafunde anu onse obwera mwamphamvu
andimiza.
8 Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake,
nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane;
pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.
9 Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa,
“Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala?
Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,
woponderezedwa ndi mdani?”
10 Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo
pamene adani anga akundinyoza,
tsiku lonse akunena kuti,
“Mulungu wako ali kuti?”
11 Bwanji ukumva chisoni,
iwe mtima wanga?
Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga?
Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso,
Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.
43 Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;
ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;
mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.
Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?
Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,
woponderezedwa ndi mdani?
3 Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu
kuti zinditsogolere;
mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,
kumalo kumene inu mumakhala.
4 Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,
kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.
Ndidzakutamandani ndi zeze,
Inu Mulungu wanga.
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?
Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?
Khulupirira Mulungu,
pakuti ndidzamutamandabe Iye,
Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.
Pemphero la Hana
2 Ndipo Hana anapemphera nati,
“Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova;
Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova.
Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola.
Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova,
palibe wina koma inu nokha,
palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
3 “Musandiyankhulenso modzitama,
pakamwa panu pasatuluke zonyada,
pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru,
ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka
koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya,
koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala.
Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri,
koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo,
amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso.
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa,
amatsitsa ndipo amakweza.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi,
ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala.
Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu,
amawapatsa mpando waulemu.
“Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova,
anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika
koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima.
“Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa.
Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba;
Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi.
“Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake,
adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
Ana a Abrahamu
31 Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga. 32 Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”
33 Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’ ”
34 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo. 35 Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. 36 Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora.
48 Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando
mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Lokongola mu utali mwake,
chimwemwe cha dziko lonse lapansi.
Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni,
mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 Mulungu ali mu malinga ake;
Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi,
pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri;
anathawa ndi mantha aakulu.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera,
ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi
zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 Monga momwe tinamvera,
kotero ife tinaona
mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse,
mu mzinda wa Mulungu wathu.
Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu,
ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu,
matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi
dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera,
midzi ya Yuda ndi yosangalala
chifukwa cha maweruzo anu.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo,
werengani nsanja zake.
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake,
penyetsetsani malinga ake,
kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha;
Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
Salimo la Ana a Kora.
87 Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2 Yehova amakonda zipata za Ziyoni
kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3 Za ulemerero wako zimakambidwa,
Iwe mzinda wa Mulungu:
Sela
4 “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni
pakati pa iwo amene amandidziwa.
Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,
ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”
5 Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,
“Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,
ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6 Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:
“Uyu anabadwira mʼZiyoni.”
Sela
7 Oyimba ndi ovina omwe adzati,
“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
3 Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye. 2 Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili. 3 Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.
4 Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo. 5 Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo. 6 Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.
7 Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama. 8 Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.