Add parallel Print Page Options

11 Tsekula zitseko zako, iwe Lebanoni,
    kuti moto unyeketse mikungudza yako!
Lira mwachisoni, iwe mtengo wa payini, pakuti mkungudza wagwa;
    mtengo wamphamvu wawonongeka!
Lirani mwachisoni, inu mitengo ya thundu ya Basani;
    nkhalango yowirira yadulidwa!
Imvani kulira mwachisoni kwa abusa;
    msipu wawo wobiriwira wawonongeka!
Imvani kubangula kwa mikango;
    nkhalango yowirira ya ku Yorodani yawonongeka!

Abusa Awiri

Yehova Mulungu wanga akuti, “Dyetsa nkhosa zimene zikukaphedwa. Amene amagula nkhosazo amazipha ndipo salangidwa. Amene amazigulitsa amanena kuti, ‘Alemekezeke Yehova, ine ndalemera!’ Abusa ake omwe sazimvera chisoni nkhosazo. Pakuti Ine sindidzamveranso chisoni anthu okhala mʼdziko,” akutero Yehova. “Ndidzapereka munthu aliyense mʼmanja mwa mnansi wake ndi mwa mfumu yake. Iwo adzazunza dziko, ndipo Ine sindidzawapulumutsa mʼmanja mwawo.”

Choncho ine ndinadyetsa nkhosa zokaphedwa, makamaka nkhosa zoponderezedwa. Pamenepo ndinatenga ndodo ziwiri ndipo yoyamba ndinayitcha Kukoma mtima ndipo yachiwiri ndinayitcha Umodzi ndipo ndinadyetsa nkhosazo. Pa mwezi umodzi ndinachotsa abusa atatu.

Abusawo anadana nane, ndipo ndinatopa nawo. Ndinawuza gulu la nkhosalo kuti, “Sindidzakhalanso mʼbusa wanu. Imene ikufa, ife, ndipo imene ikuwonongeka, iwonongeke, zimene zatsala zizidyana.”

10 Kenaka ndinatenga ndodo yanga yotchedwa Kukoma mtima ndi kuyithyola, kuphwanya pangano limene ndinachita ndi mitundu yonse ya anthu. 11 Linaphwanyidwa tsiku limenelo ndipo nkhosa zosautsidwa zimene zimandiyangʼanitsitsa zinadziwa kuti anali mawu a Yehova.

12 Ndinawawuza kuti, “Ngati mukuganiza kuti zili bwino, patseni malipiro anga; koma ngati si choncho, sungani malipirowo.” Kotero anandipatsa ndalama zasiliva makumi atatu.

13 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ziponye kwa wowumba mbiya,” mtengo woyenera umene anapereka pondigula Ine! Choncho ndinatenga ndalama zasiliva makumi atatu ndi kuziponya mʼnyumba ya Yehova kwa wowumba mbiya.

14 Kenaka ndinathyola ndodo yanga yachiwiri yotchedwa Umodzi, kuthetsa ubale pakati pa Yuda ndi Israeli.

15 Pamenepo Yehova anayankhula nane kuti, “Tenganso zida za mʼbusa wopusa. 16 Pakuti ndidzawutsa mʼbusa mʼdzikomo amene sadzasamalira zotayika, kapena kufunafuna zazingʼono, kapena zovulala, kapena kudyetsa nkhosa zabwino, koma iye adzadya nyama ya nkhosa zonenepa, nʼkumakukuta ndi ziboda zomwe.

17 “Tsoka kwa mʼbusa wopandapake,
    amene amasiya nkhosa!
Lupanga limukanthe pa mkono wake ndi pa diso lake lakumanja!
    Mkono wake ufote kotheratu,
    diso lake lamanja lisaonenso.”

11 Open your doors, Lebanon,(A)
    so that fire(B) may devour your cedars!
Wail, you juniper, for the cedar has fallen;
    the stately trees are ruined!
Wail, oaks(C) of Bashan;
    the dense forest(D) has been cut down!(E)
Listen to the wail of the shepherds;
    their rich pastures are destroyed!
Listen to the roar of the lions;(F)
    the lush thicket of the Jordan is ruined!(G)

Two Shepherds

This is what the Lord my God says: “Shepherd the flock marked for slaughter.(H) Their buyers slaughter them and go unpunished. Those who sell them say, ‘Praise the Lord, I am rich!’ Their own shepherds do not spare them.(I) For I will no longer have pity on the people of the land,” declares the Lord. “I will give everyone into the hands of their neighbors(J) and their king. They will devastate the land, and I will not rescue anyone from their hands.”(K)

So I shepherded the flock marked for slaughter,(L) particularly the oppressed of the flock. Then I took two staffs and called one Favor and the other Union, and I shepherded the flock. In one month I got rid of the three shepherds.

The flock detested(M) me, and I grew weary of them and said, “I will not be your shepherd. Let the dying die, and the perishing perish.(N) Let those who are left eat(O) one another’s flesh.”

10 Then I took my staff called Favor(P) and broke it, revoking(Q) the covenant I had made with all the nations. 11 It was revoked on that day, and so the oppressed of the flock who were watching me knew it was the word of the Lord.

12 I told them, “If you think it best, give me my pay; but if not, keep it.” So they paid me thirty pieces of silver.(R)

13 And the Lord said to me, “Throw it to the potter”—the handsome price at which they valued me! So I took the thirty pieces of silver(S) and threw them to the potter at the house of the Lord.(T)

14 Then I broke my second staff called Union, breaking the family bond between Judah and Israel.

15 Then the Lord said to me, “Take again the equipment of a foolish shepherd. 16 For I am going to raise up a shepherd over the land who will not care for the lost, or seek the young, or heal the injured, or feed the healthy, but will eat the meat of the choice sheep, tearing off their hooves.

17 “Woe to the worthless shepherd,(U)
    who deserts the flock!
May the sword strike his arm(V) and his right eye!
    May his arm be completely withered,
    his right eye totally blinded!”(W)