Yohane 8
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
8 1 Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi. 2 Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa. 3 Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo 4 anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo. 5 Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?” 6 Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye.
Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake. 7 Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.” 8 Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.
9 Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo. 10 Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”
11 Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.”
“Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”
Za Umboni wa Yesu
12 Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”
13 Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”
14 Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita. 15 Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense. 16 Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma. 17 Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka. 18 Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”
19 Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?”
Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.” 20 Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.
Mkangano Woti Yesu Ndani
21 Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”
22 Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’ ”
23 Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino. 24 Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”
25 Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?”
Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi, 26 ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”
27 Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake. 28 Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa. 29 Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.” 30 Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.
Ana a Abrahamu
31 Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga. 32 Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”
33 Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’ ”
34 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo. 35 Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. 36 Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu. 37 Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu. 38 Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”
39 Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.”
Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita. 40 Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi. 41 Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.”
Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”
Ana a Mdierekezi
42 Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha. 43 Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga. 44 Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza. 45 Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine! 46 Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira? 47 Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”
Zomwe Yesu Ananena za lye Mwini
48 Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”
49 Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza. 50 Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza. 51 Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.”
52 Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ 53 Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”
54 Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine. 55 Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake. 56 Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”
57 Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”
58 Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!” 59 Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.
John 8
King James Version
8 Jesus went unto the mount of Olives.
2 And early in the morning he came again into the temple, and all the people came unto him; and he sat down, and taught them.
3 And the scribes and Pharisees brought unto him a woman taken in adultery; and when they had set her in the midst,
4 They say unto him, Master, this woman was taken in adultery, in the very act.
5 Now Moses in the law commanded us, that such should be stoned: but what sayest thou?
6 This they said, tempting him, that they might have to accuse him. But Jesus stooped down, and with his finger wrote on the ground, as though he heard them not.
7 So when they continued asking him, he lifted up himself, and said unto them, He that is without sin among you, let him first cast a stone at her.
8 And again he stooped down, and wrote on the ground.
9 And they which heard it, being convicted by their own conscience, went out one by one, beginning at the eldest, even unto the last: and Jesus was left alone, and the woman standing in the midst.
10 When Jesus had lifted up himself, and saw none but the woman, he said unto her, Woman, where are those thine accusers? hath no man condemned thee?
11 She said, No man, Lord. And Jesus said unto her, Neither do I condemn thee: go, and sin no more.
12 Then spake Jesus again unto them, saying, I am the light of the world: he that followeth me shall not walk in darkness, but shall have the light of life.
13 The Pharisees therefore said unto him, Thou bearest record of thyself; thy record is not true.
14 Jesus answered and said unto them, Though I bear record of myself, yet my record is true: for I know whence I came, and whither I go; but ye cannot tell whence I come, and whither I go.
15 Ye judge after the flesh; I judge no man.
16 And yet if I judge, my judgment is true: for I am not alone, but I and the Father that sent me.
17 It is also written in your law, that the testimony of two men is true.
18 I am one that bear witness of myself, and the Father that sent me beareth witness of me.
19 Then said they unto him, Where is thy Father? Jesus answered, Ye neither know me, nor my Father: if ye had known me, ye should have known my Father also.
20 These words spake Jesus in the treasury, as he taught in the temple: and no man laid hands on him; for his hour was not yet come.
21 Then said Jesus again unto them, I go my way, and ye shall seek me, and shall die in your sins: whither I go, ye cannot come.
22 Then said the Jews, Will he kill himself? because he saith, Whither I go, ye cannot come.
23 And he said unto them, Ye are from beneath; I am from above: ye are of this world; I am not of this world.
24 I said therefore unto you, that ye shall die in your sins: for if ye believe not that I am he, ye shall die in your sins.
25 Then said they unto him, Who art thou? And Jesus saith unto them, Even the same that I said unto you from the beginning.
26 I have many things to say and to judge of you: but he that sent me is true; and I speak to the world those things which I have heard of him.
27 They understood not that he spake to them of the Father.
28 Then said Jesus unto them, When ye have lifted up the Son of man, then shall ye know that I am he, and that I do nothing of myself; but as my Father hath taught me, I speak these things.
29 And he that sent me is with me: the Father hath not left me alone; for I do always those things that please him.
30 As he spake these words, many believed on him.
31 Then said Jesus to those Jews which believed on him, If ye continue in my word, then are ye my disciples indeed;
32 And ye shall know the truth, and the truth shall make you free.
33 They answered him, We be Abraham's seed, and were never in bondage to any man: how sayest thou, Ye shall be made free?
34 Jesus answered them, Verily, verily, I say unto you, Whosoever committeth sin is the servant of sin.
35 And the servant abideth not in the house for ever: but the Son abideth ever.
36 If the Son therefore shall make you free, ye shall be free indeed.
37 I know that ye are Abraham's seed; but ye seek to kill me, because my word hath no place in you.
38 I speak that which I have seen with my Father: and ye do that which ye have seen with your father.
39 They answered and said unto him, Abraham is our father. Jesus saith unto them, If ye were Abraham's children, ye would do the works of Abraham.
40 But now ye seek to kill me, a man that hath told you the truth, which I have heard of God: this did not Abraham.
41 Ye do the deeds of your father. Then said they to him, We be not born of fornication; we have one Father, even God.
42 Jesus said unto them, If God were your Father, ye would love me: for I proceeded forth and came from God; neither came I of myself, but he sent me.
43 Why do ye not understand my speech? even because ye cannot hear my word.
44 Ye are of your father the devil, and the lusts of your father ye will do. He was a murderer from the beginning, and abode not in the truth, because there is no truth in him. When he speaketh a lie, he speaketh of his own: for he is a liar, and the father of it.
45 And because I tell you the truth, ye believe me not.
46 Which of you convinceth me of sin? And if I say the truth, why do ye not believe me?
47 He that is of God heareth God's words: ye therefore hear them not, because ye are not of God.
48 Then answered the Jews, and said unto him, Say we not well that thou art a Samaritan, and hast a devil?
49 Jesus answered, I have not a devil; but I honour my Father, and ye do dishonour me.
50 And I seek not mine own glory: there is one that seeketh and judgeth.
51 Verily, verily, I say unto you, If a man keep my saying, he shall never see death.
52 Then said the Jews unto him, Now we know that thou hast a devil. Abraham is dead, and the prophets; and thou sayest, If a man keep my saying, he shall never taste of death.
53 Art thou greater than our father Abraham, which is dead? and the prophets are dead: whom makest thou thyself?
54 Jesus answered, If I honour myself, my honour is nothing: it is my Father that honoureth me; of whom ye say, that he is your God:
55 Yet ye have not known him; but I know him: and if I should say, I know him not, I shall be a liar like unto you: but I know him, and keep his saying.
56 Your father Abraham rejoiced to see my day: and he saw it, and was glad.
57 Then said the Jews unto him, Thou art not yet fifty years old, and hast thou seen Abraham?
58 Jesus said unto them, Verily, verily, I say unto you, Before Abraham was, I am.
59 Then took they up stones to cast at him: but Jesus hid himself, and went out of the temple, going through the midst of them, and so passed by.
John 8
English Standard Version
8 1 but Jesus went to the Mount of Olives. 2 (A)Early in the morning he came again to the temple. All the people came to him, and (B)he sat down and taught them. 3 The scribes and the Pharisees brought a woman who had been caught in adultery, and placing her in the midst 4 they said to him, “Teacher, this woman has been caught in the act of adultery. 5 Now (C)in the Law, Moses commanded us (D)to stone such women. So what do you say?” 6 This they said (E)to test him, (F)that they might have some charge to bring against him. Jesus bent down and wrote with his finger on the ground. 7 And as they continued to ask him, he stood up and said to them, (G)“Let him who is without sin among you (H)be the first to throw a stone at her.” 8 And once more he bent down and wrote on the ground. 9 But when they heard it, they went away one by one, beginning with the older ones, and Jesus was left alone with the woman standing before him. 10 Jesus stood up and said to her, “Woman, where are they? Has no one condemned you?” 11 She said, “No one, Lord.” And Jesus said, (I)“Neither do I condemn you; go, and from now on (J)sin no more.”]]
I Am the Light of the World
12 (K)Again Jesus spoke to them, saying, (L)“I am the light of the world. Whoever (M)follows me will not (N)walk in darkness, but will have the light of life.” 13 So the Pharisees said to him, (O)“You are bearing witness about yourself; your testimony is not true.” 14 Jesus answered, “Even if I do bear witness about myself, (P)my testimony is true, for I know (Q)where I came from and (R)where I am going, but (S)you do not know where I come from or where I am going. 15 (T)You judge according to the flesh; (U)I judge no one. 16 Yet even if I do judge, (V)my judgment is true, for (W)it is not I alone who judge, but I and the Father[a] who sent me. 17 (X)In your Law it is written that the testimony of two people is true. 18 I am the one who bears witness about myself, and (Y)the Father who sent me bears witness about me.” 19 They said to him therefore, “Where is your Father?” Jesus answered, (Z)“You know neither me nor my Father. (AA)If you knew me, you would know my Father also.” 20 These words he spoke in (AB)the treasury, as he taught in the temple; but (AC)no one arrested him, because (AD)his hour had not yet come.
21 So he said to them again, (AE)“I am going away, and (AF)you will seek me, and (AG)you will die in your sin. Where I am going, you cannot come.” 22 So the Jews said, (AH)“Will he kill himself, since he says, ‘Where I am going, you cannot come’?” 23 He said to them, (AI)“You are from below; I am from above. (AJ)You are of this world; (AK)I am not of this world. 24 I told you that you (AL)would die in your sins, for (AM)unless you believe that (AN)I am he you will die in your sins.” 25 So they said to him, (AO)“Who are you?” Jesus said to them, “Just what I have been telling you from the beginning. 26 I have much to say about you and much to judge, but (AP)he who sent me is true, and I declare (AQ)to the world (AR)what I have heard from him.” 27 They did not understand that (AS)he had been speaking to them about the Father. 28 So Jesus said to them, “When you have (AT)lifted up the Son of Man, (AU)then you will know that (AV)I am he, and that (AW)I do nothing on my own authority, but (AX)speak just as the Father taught me. 29 And (AY)he who sent me is with me. (AZ)He has not left me alone, for (BA)I always do the things that are pleasing to him.” 30 As he was saying these things, (BB)many believed in him.
The Truth Will Set You Free
31 So Jesus said to the Jews who had believed him, (BC)“If you abide in my word, you are truly my disciples, 32 and you will (BD)know the truth, and the truth (BE)will set you free.” 33 They answered him, (BF)“We are offspring of Abraham and have never been enslaved to anyone. How is it that you say, ‘You will become free’?”
34 Jesus answered them, “Truly, truly, I say to you, (BG)everyone who practices sin is a slave[b] to sin. 35 (BH)The slave does not remain in the house forever; (BI)the son remains forever. 36 So if the Son sets you free, you will be free indeed. 37 I know that you are offspring of Abraham; yet (BJ)you seek to kill me because my word finds no place in you. 38 (BK)I speak of what I have seen with my Father, and you do what you have heard (BL)from your father.”
You Are of Your Father the Devil
39 They answered him, (BM)“Abraham is our father.” Jesus said to them, (BN)“If you were Abraham's children, you would be doing the works Abraham did, 40 but now (BO)you seek to kill me, a man who has told you the truth (BP)that I heard from God. This is not what Abraham did. 41 You are doing the works your father did.” They said to him, (BQ)“We were not born of sexual immorality. We have (BR)one Father—even God.” 42 Jesus said to them, (BS)“If God were your Father, you would love me, for (BT)I came from God and (BU)I am here. (BV)I came not of my own accord, but (BW)he sent me. 43 (BX)Why do you not understand what I say? It is because you cannot (BY)bear to hear my word. 44 (BZ)You are of your father the devil, and your will is to do your father's desires. (CA)He was a murderer from the beginning, and (CB)does not stand in the truth, because there is no truth in him. (CC)When he lies, he speaks out of his own character, for he is a liar and the father of lies. 45 But because I tell the truth, you do not believe me. 46 Which one of you convicts me of sin? If I tell the truth, why do you not believe me? 47 (CD)Whoever is of God hears the words of God. (CE)The reason why you do not hear them is that (CF)you are not of God.”
Before Abraham Was, I Am
48 The Jews answered him, “Are we not right in saying that you are a Samaritan and (CG)have a demon?” 49 Jesus answered, “I do not have a demon, but (CH)I honor my Father, and you dishonor me. 50 Yet (CI)I do not seek my own glory; there is One who seeks it, and he is the judge. 51 Truly, truly, (CJ)I say to you, if anyone keeps my word, he will never (CK)see death.” 52 The Jews said to him, “Now we know that you have a demon! (CL)Abraham died, as did the prophets, yet (CM)you say, ‘If anyone keeps my word, he will never (CN)taste death.’ 53 (CO)Are you greater than our father Abraham, who died? And the prophets died! Who do you make yourself out to be?” 54 Jesus answered, (CP)“If I glorify myself, my glory is nothing. (CQ)It is my Father who glorifies me, (CR)of whom you say, ‘He is our God.’[c] 55 But (CS)you have not known him. (CT)I know him. If I were to say that I do not know him, I would be (CU)a liar (CV)like you, but I do know him and I keep his word. 56 (CW)Your father Abraham (CX)rejoiced (CY)that he would see my day. (CZ)He saw it and was glad.” 57 So the Jews said to him, “You are not yet fifty years old, and have you seen Abraham?”[d] 58 Jesus said to them, “Truly, truly, I say to you, before Abraham was, (DA)I am.” 59 So (DB)they picked up stones to throw at him, but Jesus hid himself and went out of the temple.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The ESV® Bible (The Holy Bible, English Standard Version®), © 2001 by Crossway, a publishing ministry of Good News Publishers. ESV Text Edition: 2025.
