Add parallel Print Page Options

Yesu Acheza ndi Mayi wa ku Samariya

Yesu atazindikira kuti Afarisi amva zoti Iye ankapeza ndi kubatiza ophunzira ambiri kupambana Yohane, (ngakhale kuti Yesuyo sankabatiza, koma ophunzira ake). Iye anachoka ku Yudeya ndi kubwereranso ku Galileya.

Ndipo Iye anayenera kudutsa mu Samariya. Iye anafika mʼmudzi wa Asamariya wotchedwa Sukari, pafupi ndi malo amene Yakobo anapatsa mwana wake Yosefe. Chitsime cha Yakobo chinali pamenepo ndipo Yesu atatopa ndi ulendo anakhala pansi pambali pa chitsimecho. Nthawi inali pafupifupi ora lachisanu ndi chimodzi masana.

Mayi wa Chisamariya atabwera kudzatunga madzi, Yesu anati kwa iye, “Kodi ungandipatse madzi akumwa.” (Ophunzira ake nʼkuti atapita mʼmudzi kukagula chakudya).

Mayiyo anati kwa Iye, “Inu ndinu Myuda ndipo ine ndine Msamariya. Bwanji mukundipempha madzi akumwa?” (Popeza Ayuda ndi Asamariya sankayanjana).

10 Yesu anamuyankha kuti, “Koma iwe ukanadziwa mphatso ya Mulungu ndi Iye amene akukupempha madzi akumwa, ukanamupempha ndipo akanakupatsa madzi amoyo.”

11 Mayiyo anati, “Ambuye, Inu mulibe kanthu kotungira madzi ndipo chitsime ndi chakuya. Kodi madzi amoyowo mungawatenge kuti? 12 Kodi Inu ndinu wamkulu kuposa kholo lathu Yakobo, amene anatipatsa chitsimechi ndipo iye ankamwanso monga anachita ana ake ndi ziweto zake?”

13 Yesu anayankha kuti, “Aliyense amene amamwa madzi awa amamvanso ludzu, 14 koma aliyense amene adzamwa madzi amene Ine ndidzamupatsa sadzamvanso ludzu. Ndithudi, madzi amene ndidzamupatsa adzakhala kasupe wamadzi wotumphukira ku moyo wosatha.”

15 Mayiyo anati kwa Iye, “Ambuye, patseni madzi amenewo kuti ndisadzamvenso ludzu ndi kumabwerabe kuno kudzatunga madzi.”

16 Iye anamuwuza kuti, “Pita kayitane mwamuna wako ndipo ubwere naye.”

17 Iye anayankha kuti, “Ine ndilibe mwamuna.”

Yesu anati kwa iye, “Wakhoza ponena kuti ulibe mwamuna. 18 Zoona nʼzakuti iwe wakhala pa banja ndi amuna asanu, ndipo mwamuna amene uli naye tsopano si wako. Zimene wanenazi ndi zoona.”

19 Mayiyo anati, “Ambuye, ine ndazindikira kuti Inu ndinu mneneri. 20 Makolo athu ankapembedza mʼphiri ili koma inu Ayuda mumati malo amene tiyenera kupembedzera ali ku Yerusalemu.”

21 Yesu anati, “Mayi inu khulupirira Ine. Nthawi ikubwera pamene inu simudzapembedza Atate mʼphiri ili kapena mu Yerusalemu. 22 Inu Asamariya mumapembedza chimene simukuchidziwa. Ife timapembedza chimene tikuchidziwa, pakuti chipulumutso nʼchochokera kwa Ayuda. 23 Koma nthawi ikubwera ndipo yafika kale tsopano pamene opembedza woona adzapembedza Atate mu mzimu ndi mʼchoonadi, pakuti opembedza otere ndiwo amene Atate akuwafuna. 24 Mulungu ndi Mzimu, ndipo omupembedza Iye ayenera kumupembedza mu mzimu ndi mʼchoonadi.”

25 Mayiyo anati, “Ine ndikudziwa kuti Mesiya (wotchedwa Khristu) akubwera. Akabwera, Iye adzafotokoza zonse kwa ife.”

26 Ndipo Yesu anamuwuza kuti, “Amene ndikukuyankhulane, ndine amene.”

Ophunzira Abweranso kwa Yesu

27 Pa nthawi yomweyo ophunzira ake anabwerera ndipo anadabwa kupeza Iye akuyankhula ndi mayi. Koma palibe amene anamufunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” kapena, “Nʼchifukwa chiyani mukuyankhula naye?”

28 Kenaka mayiyo anasiya mtsuko wamadzi, nabwerera ku mzinda ndipo anati kwa anthu, 29 “Tiyeni mukaone munthu amene wandiwuza ine zilizonse zimene ndinazichita. Kodi ameneyu sangakhale Khristu?” 30 Iwo anatuluka mʼmudziwo ndi kupita kumene kunali Iye.

31 Pa nthawi imeneyi ndi kuti ophunzira ake akumukakamiza kuti, “Rabi idyani.”

32 Koma Iye anawawuza kuti, “Ine ndili ndi chakudya choti ndidye chimene inu simukuchidziwa.”

33 Ndipo ophunzira ake anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi alipo wina amene anamubweretsera Iye chakudya?”

34 Yesu anati, “Chakudya changa ndikuchita chifuniro cha Iye amene anandituma Ine ndi kumaliza ntchito yake. 35 Kodi inu simunena kuti, ‘Kwatsala miyezi inayi ndipo kenaka kukolola?’ Ine ndikukuwuzani kuti, tsekulani maso anu ndipo muyangʼane mʼminda! Mbewu zacha kale kuti zikololedwe. 36 Ngakhale tsopano amene akukolola akulandira malipiro ake, ndipo akututa mbewu ku moyo wosatha kuti wofesa ndi wokolola asangalale pamodzi. 37 Nʼchifukwa chake mawu akuti, ‘Wina amafesa ndipo wina amakolola’ ndi woona. 38 Ine ndinakutumani kukakolola zimene simunagwirire ntchito. Ena anagwira ntchito yolemetsa ndipo inu mwatuta phindu la ntchito yawo.”

Asamariya Ambiri Akhulupirira

39 Asamariya ambiri ochokera mʼmudziwo anakhulupirira Iye chifukwa cha umboni wa mayiyo wakuti, “Iye anandiwuza ine zonse ndinazichita.” 40 Choncho Asamariya atabwera kwa Iye, anamuwumiriza Iye kuti akhale nawo, ndipo Iye anakhala nawo masiku awiri. 41 Ndipo chifukwa cha mawu ake, ena ambiri anakhulupirira.

42 Iwo anati kwa mayiyo, “Ife sitikukhulupirira chifukwa cha mawu ako okha, koma tsopano ife tadzimvera tokha, ndipo tikudziwa kuti munthu uyu ndithu ndi Mpulumutsi wa dziko lapansi.”

Yesu Achiritsa Mwana wa Nduna ya Mfumu

43 Patatha masiku awiri Iye anachoka napita ku Galileya. 44 (Tsopano Yesu mwini ananena kale kuti mneneri salandira ulemu mʼdziko lake). 45 Iye atafika ku Galileya, Agalileya anamulandira. Iwo anali ataona zonse zimene anazichita mu Yerusalemu pa phwando la Paska, pakuti iwonso anali komweko.

46 Iye anakafikanso ku Kana wa ku Galileya, kumene anasanduliza madzi kukhala vinyo. Ndipo kumeneko kunali nduna ina ya mfumu imene mwana wake wamwamuna anali chigonere akudwala ku Kaperenawo. 47 Munthu uyu atamva kuti Yesu wafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya, anapita kwa Iye, namupempha kuti apite akachiritse mwana wakeyo, amene anali pafupi kufa.

48 Yesu anawawuza iwo kuti, “Anthu inu pokhapokha mutaona zizindikiro zodabwitsa, simudzakhulupirira.”

49 Nduna ya mfumuyo inati, “Ambuye tiyeni mwana wanga asanafe.”

50 Yesu anayankha kuti, “Pita. Mwana wako adzakhala ndi moyo.”

Munthuyo anakhulupirira mawu a Yesu ndipo ananyamuka. 51 Iye ali pa njira, antchito ake anakumana naye, namuwuza kuti mwana wanu uja wachira. 52 Iye atafunsa kuti ndi nthawi yanji imene mwana wake anapeza bwino, iwo anati kwa iye, “Malungo anamusiya iye dzulo pa ora lachisanu ndi chiwiri.”

53 Ndipo bamboyo anazindikira kuti iyi inali nthawi yomweyo imene Yesu anati kwa iye, “Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Choncho iye ndi onse a pa banja lake anakhulupirira.

54 Ichi ndiye chinali chizindikiro chodabwitsa chachiwiri chimene Yesu anachita atafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya.

Jesus and the Woman of Samaria

Now when Jesus learned that the Pharisees had heard that Jesus was making and (A)baptizing more disciples than John (although Jesus himself did not baptize, but only his disciples), he left Judea and departed (B)again for Galilee. (C)And he had to pass through Samaria. So he came to a town of Samaria called Sychar, near the field (D)that Jacob had given to his son Joseph. Jacob's well was there; so Jesus, (E)wearied as he was from his journey, was sitting beside the well. It was about the sixth hour.[a]

A woman from Samaria came to draw water. Jesus said to her, (F)“Give me a drink.” (For his disciples had gone away into the city to buy food.) The Samaritan woman said to him, “How is it that you, a Jew, ask for a drink from me, a woman of Samaria?” ((G)For Jews have no dealings with Samaritans.) 10 Jesus answered her, “If you knew the gift of God, and who it is that is saying to you, ‘Give me a drink,’ you would have asked him, and he would have given you (H)living water.” 11 The woman said to him, “Sir, you have nothing to draw water with, and the well is deep. Where do you get that living water? 12 (I)Are you greater than our father Jacob? (J)He gave us the well and drank from it himself, as did his sons and his livestock.” 13 Jesus said to her, “Everyone who drinks of this water will be thirsty again, 14 but (K)whoever drinks of the water that I will give him (L)will never be thirsty again.[b] The water that I will give him will become (M)in him a spring of water welling up to eternal life.” 15 The woman said to him, “Sir, (N)give me this water, so that I will not be thirsty or have to come here to draw water.”

16 Jesus said to her, “Go, (O)call your husband, and come here.” 17 The woman answered him, “I have no husband.” Jesus said to her, “You are right in saying, ‘I have no husband’; 18 for you have had five husbands, and the one you now have is not your husband. What you have said is true.” 19 The woman said to him, “Sir, I perceive that (P)you are (Q)a prophet. 20 (R)Our fathers worshiped on (S)this mountain, but you say that (T)in Jerusalem is (U)the place where people ought to worship.” 21 Jesus said to her, (V)“Woman, believe me, (W)the hour is coming when (X)neither on this mountain nor in Jerusalem will you worship the Father. 22 (Y)You worship what you do not know; (Z)we worship what we know, for (AA)salvation is (AB)from the Jews. 23 But (AC)the hour is coming, and is now here, when the true worshipers will worship the Father (AD)in spirit and (AE)truth, for the Father (AF)is seeking such people to worship him. 24 God is spirit, and those who worship him must worship in spirit and truth.” 25 The woman said to him, “I know that (AG)Messiah is coming (he who is called Christ). When he comes, (AH)he will tell us all things.” 26 Jesus said to her, (AI)“I who speak to you am he.”

27 Just then (AJ)his disciples came back. They marveled that he was talking with a woman, but no one said, “What do you seek?” or, “Why are you talking with her?” 28 So the woman left her water jar and went away into town and said to the people, 29 “Come, see a man (AK)who told me all that I ever did. Can this be the Christ?” 30 They went out of the town and were coming to him.

31 Meanwhile the disciples were urging him, saying, (AL)“Rabbi, eat.” 32 But he said to them, “I have food to eat that you do not know about.” 33 So the disciples said to one another, (AM)“Has anyone brought him something to eat?” 34 Jesus said to them, (AN)“My food is (AO)to do the will of him who sent me and (AP)to accomplish his work. 35 Do you not say, ‘There are yet four months, then comes the harvest’? Look, I tell you, lift up your eyes, and see that (AQ)the fields are white for harvest. 36 Already the one who reaps is receiving wages and gathering fruit for eternal life, so that (AR)sower and (AS)reaper (AT)may rejoice together. 37 For here the saying holds true, (AU)‘One sows and another reaps.’ 38 I sent you to reap (AV)that for which you did not labor. Others have labored, (AW)and you have entered into their labor.”

39 Many Samaritans (AX)from that town believed in him (AY)because of (AZ)the woman's testimony, “He told me all that I ever did.” 40 So when the Samaritans came to him, they asked him to stay with them, and he stayed there two days. 41 And many more believed (BA)because of his word. 42 They said to the woman, “It is no longer because of what you said that we believe, for we have heard for ourselves, (BB)and we know that this is indeed (BC)the Savior (BD)of the world.”

43 After (BE)the two days he departed for Galilee. 44 (For Jesus himself had testified (BF)that a prophet has no honor in his own hometown.) 45 So when he came to Galilee, the Galileans welcomed him, (BG)having seen all that he had done in Jerusalem at the feast. For (BH)they too had gone to the feast.

Jesus Heals an Official's Son

46 So he came again to (BI)Cana in Galilee, (BJ)where he had made the water wine. And at Capernaum there was an official whose son was ill. 47 When this man heard that Jesus (BK)had come from Judea to Galilee, he went to him and asked him to come down and heal his son, for he was at the point of death. 48 So Jesus said to him, (BL)“Unless you[c] see signs and wonders you will not believe.” 49 The official said to him, “Sir, come down (BM)before my child dies.” 50 Jesus said to him, “Go; your son will live.” The man believed the word that Jesus spoke to him and went on his way. 51 As he was going down, his servants[d] met him and told him that his son was recovering. 52 So he asked them the hour when he began to get better, and they said to him, “Yesterday at the seventh hour[e] the fever left him.” 53 The father knew that was the hour when Jesus had said to him, “Your son will live.” And he himself believed, (BN)and all his household. 54 (BO)This was now the second sign that Jesus did when he had come from Judea to Galilee.

Footnotes

  1. John 4:6 That is, about noon
  2. John 4:14 Greek forever
  3. John 4:48 The Greek for you is plural; twice in this verse
  4. John 4:51 Or bondservants
  5. John 4:52 That is, at 1 p.m.