Add parallel Print Page Options

Mawu a Bilidadi

Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti?
    Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama?
    Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu,
    Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Koma utayangʼana kwa Mulungu,
    ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima
    ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako
    ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa
    koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.

“Funsa kwa anthu amvulazakale
    ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse,
    ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera?
    Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho?
    Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula;
    zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu;
    ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka;
    zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka;
    amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa,
    nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala
    ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo,
    pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Ndithudi chomeracho chimafota,
    ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.

20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa
    kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete
    ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Adani ako adzachita manyazi,
    ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”