Add parallel Print Page Options

Mawu a Bilidadi

Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti?
    Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama?
    Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu,
    Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Koma utayangʼana kwa Mulungu,
    ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima
    ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako
    ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa
    koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.

“Funsa kwa anthu amvulazakale
    ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse,
    ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera?
    Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho?
    Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula;
    zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu;
    ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka;
    zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka;
    amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa,
    nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala
    ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo,
    pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Ndithudi chomeracho chimafota,
    ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.

20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa
    kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete
    ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Adani ako adzachita manyazi,
    ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

Bildad Speaks: Job Should Repent

Then (A)Bildad the Shuhite answered and said:

“How long will you say these things,
    and the words of your mouth be a (B)great wind?
(C)Does God pervert justice?
    Or does the Almighty pervert the right?
If your (D)children have sinned against him,
    he has delivered them into the hand of their transgression.
If you will seek God
    and (E)plead with the Almighty for mercy,
if you are pure and upright,
    surely then he will (F)rouse himself for you
    and (G)restore your rightful habitation.
And though your beginning was small,
    (H)your latter days will be very great.

“For (I)inquire, please, of bygone ages,
    and consider what (J)the fathers have searched out.
For we are but of yesterday and know nothing,
    for our days on earth are (K)a shadow.
10 Will they not teach you and tell you
    and utter words out of their understanding?

11 “Can papyrus grow where there is no marsh?
    Can reeds flourish where there is no water?
12 While yet in flower and not cut down,
    they (L)wither before any other plant.
13 Such are the paths of all who (M)forget God;
    (N)the hope of (O)the godless shall perish.
14 His confidence is severed,
    and his trust is (P)a spider's web.[a]
15 He leans against his (Q)house, but it does not stand;
    he lays hold of it, but it does not endure.
16 He is a lush plant before the sun,
    and his (R)shoots spread over his garden.
17 His roots entwine the stone heap;
    he looks upon a house of stones.
18 If he is destroyed from his (S)place,
    then it will deny him, saying, ‘I have never (T)seen you.’
19 Behold, this is the joy of his way,
    and out of (U)the soil others will spring.

20 “Behold, God will not reject a blameless man,
    nor take the hand of evildoers.
21 He will yet (V)fill your mouth with laughter,
    and your lips with shouting.
22 Those who hate you will be (W)clothed with shame,
    and the tent of the wicked will be no more.”

Footnotes

  1. Job 8:14 Hebrew house