Add parallel Print Page Options

33 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga;
    mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Tsopano ndiyamba kuyankhula;
    mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama;
    pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba,
    mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
Mundiyankhe ngati mungathe;
    konzekani tsopano kuti munditsutse.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu;
    nanenso ndinachokera ku dothi.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi,
    Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.

“Koma inu mwayankhula ine ndikumva,
    ndamva mawu anuwo onena kuti,
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo;
    ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo;
    Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo,
    akulonda mayendedwe anga onse.’

12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi,
    pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye
    kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana,
    ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku,
    pamene anthu ali mʼtulo tofa nato
    pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 amawanongʼoneza mʼmakutu
    ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa,
    ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 kumulanditsa munthu ku manda,
    kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.

19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake,
    nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya,
    ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Thupi lake limawonda
    ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Munthuyo amayandikira ku manda,
    moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.

23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi,
    mmodzi mwa ambirimbiri oterewa,
    adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti,
    ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda;
    ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana;
    ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa.
    Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe
    ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti,
    ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama,
    koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda,
    ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’

29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu
    kawirikawiri,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda,
    kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.

31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere;
    khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni;
    yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere;
    khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”