Yobu 34
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
34 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru;
tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 Pakuti khutu limayesa mawu
monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera;
tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa,
koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima,
akundiyesa wabodza;
ngakhale ndine wosachimwa,
mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani,
amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa;
amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu
poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu.
Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe,
Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake;
Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa,
kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani?
Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo
oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu
ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi;
mvetserani zimene ndikunena.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira?
Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’
ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 Iye sakondera akalonga
ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka,
pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku;
anthu amachita mantha ndipo amamwalira;
munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu;
amaona mayendedwe ake onse.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani
kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu,
kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu
ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo
amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo,
pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 Chifukwa anasiya kumutsata
ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake,
kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa?
Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe?
Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza,
kuti asatchere anthu misampha.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti,
‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona
ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira,
pamene inu mukukana kulapa?
Chisankho nʼchanu, osati changa;
tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana,
anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru;
mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto
chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira;
amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu,
ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Job 34
New International Version
34 Then Elihu said:
2 “Hear my words, you wise men;
listen to me,(A) you men of learning.
3 For the ear tests words
as the tongue tastes food.(B)
4 Let us discern for ourselves what is right;(C)
let us learn together what is good.(D)
5 “Job says, ‘I am innocent,(E)
but God denies me justice.(F)
6 Although I am right,
I am considered a liar;(G)
although I am guiltless,(H)
his arrow inflicts an incurable wound.’(I)
7 Is there anyone like Job,
who drinks scorn like water?(J)
8 He keeps company with evildoers;
he associates with the wicked.(K)
9 For he says, ‘There is no profit
in trying to please God.’(L)
10 “So listen to me,(M) you men of understanding.(N)
Far be it from God to do evil,(O)
from the Almighty to do wrong.(P)
11 He repays everyone for what they have done;(Q)
he brings on them what their conduct deserves.(R)
12 It is unthinkable that God would do wrong,(S)
that the Almighty would pervert justice.(T)
13 Who appointed(U) him over the earth?
Who put him in charge of the whole world?(V)
14 If it were his intention
and he withdrew his spirit[a](W) and breath,(X)
15 all humanity would perish(Y) together
and mankind would return to the dust.(Z)
16 “If you have understanding,(AA) hear this;
listen to what I say.(AB)
17 Can someone who hates justice govern?(AC)
Will you condemn the just and mighty One?(AD)
18 Is he not the One who says to kings, ‘You are worthless,’
and to nobles,(AE) ‘You are wicked,’(AF)
19 who shows no partiality(AG) to princes
and does not favor the rich over the poor,(AH)
for they are all the work of his hands?(AI)
20 They die in an instant, in the middle of the night;(AJ)
the people are shaken and they pass away;
the mighty are removed without human hand.(AK)
21 “His eyes are on the ways of mortals;(AL)
he sees their every step.(AM)
22 There is no deep shadow,(AN) no utter darkness,(AO)
where evildoers can hide.(AP)
23 God has no need to examine people further,(AQ)
that they should come before him for judgment.(AR)
24 Without inquiry he shatters(AS) the mighty(AT)
and sets up others in their place.(AU)
25 Because he takes note of their deeds,(AV)
he overthrows them in the night(AW) and they are crushed.(AX)
26 He punishes them for their wickedness(AY)
where everyone can see them,
27 because they turned from following him(AZ)
and had no regard for any of his ways.(BA)
28 They caused the cry of the poor to come before him,
so that he heard the cry of the needy.(BB)
29 But if he remains silent,(BC) who can condemn him?(BD)
If he hides his face,(BE) who can see him?
Yet he is over individual and nation alike,(BF)
30 to keep the godless(BG) from ruling,(BH)
from laying snares for the people.(BI)
31 “Suppose someone says to God,
‘I am guilty(BJ) but will offend no more.
32 Teach me what I cannot see;(BK)
if I have done wrong, I will not do so again.’(BL)
33 Should God then reward you on your terms,
when you refuse to repent?(BM)
You must decide, not I;
so tell me what you know.
34 “Men of understanding declare,
wise men who hear me say to me,
35 ‘Job speaks without knowledge;(BN)
his words lack insight.’(BO)
36 Oh, that Job might be tested to the utmost
for answering like a wicked man!(BP)
37 To his sin he adds rebellion;
scornfully he claps his hands(BQ) among us
and multiplies his words(BR) against God.”(BS)
Footnotes
- Job 34:14 Or Spirit
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.