Add parallel Print Page Options

33 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga;
    mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Tsopano ndiyamba kuyankhula;
    mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama;
    pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba,
    mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
Mundiyankhe ngati mungathe;
    konzekani tsopano kuti munditsutse.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu;
    nanenso ndinachokera ku dothi.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi,
    Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.

“Koma inu mwayankhula ine ndikumva,
    ndamva mawu anuwo onena kuti,
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo;
    ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo;
    Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo,
    akulonda mayendedwe anga onse.’

12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi,
    pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye
    kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana,
    ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku,
    pamene anthu ali mʼtulo tofa nato
    pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 amawanongʼoneza mʼmakutu
    ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa,
    ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 kumulanditsa munthu ku manda,
    kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.

19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake,
    nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya,
    ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Thupi lake limawonda
    ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Munthuyo amayandikira ku manda,
    moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.

23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi,
    mmodzi mwa ambirimbiri oterewa,
    adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti,
    ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda;
    ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana;
    ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa.
    Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe
    ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti,
    ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama,
    koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda,
    ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’

29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu
    kawirikawiri,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda,
    kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.

31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere;
    khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni;
    yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere;
    khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

33 “But now, Job, listen(A) to my words;
    pay attention to everything I say.(B)
I am about to open my mouth;
    my words are on the tip of my tongue.
My words come from an upright heart;(C)
    my lips sincerely speak what I know.(D)
The Spirit(E) of God has made me;(F)
    the breath of the Almighty(G) gives me life.(H)
Answer me(I) then, if you can;
    stand up(J) and argue your case before me.(K)
I am the same as you in God’s sight;(L)
    I too am a piece of clay.(M)
No fear of me should alarm you,
    nor should my hand be heavy on you.(N)

“But you have said in my hearing—
    I heard the very words—
‘I am pure,(O) I have done no wrong;(P)
    I am clean and free from sin.(Q)
10 Yet God has found fault with me;
    he considers me his enemy.(R)
11 He fastens my feet in shackles;(S)
    he keeps close watch on all my paths.’(T)

12 “But I tell you, in this you are not right,
    for God is greater than any mortal.(U)
13 Why do you complain to him(V)
    that he responds to no one’s words[a]?(W)
14 For God does speak(X)—now one way, now another(Y)
    though no one perceives it.(Z)
15 In a dream,(AA) in a vision(AB) of the night,(AC)
    when deep sleep(AD) falls on people
    as they slumber in their beds,
16 he may speak(AE) in their ears
    and terrify them(AF) with warnings,(AG)
17 to turn them from wrongdoing
    and keep them from pride,(AH)
18 to preserve them from the pit,(AI)
    their lives from perishing by the sword.[b](AJ)

19 “Or someone may be chastened(AK) on a bed of pain(AL)
    with constant distress in their bones,(AM)
20 so that their body finds food(AN) repulsive
    and their soul loathes the choicest meal.(AO)
21 Their flesh wastes away to nothing,
    and their bones,(AP) once hidden, now stick out.(AQ)
22 They draw near to the pit,(AR)
    and their life to the messengers of death.[c](AS)
23 Yet if there is an angel at their side,
    a messenger,(AT) one out of a thousand,
    sent to tell them how to be upright,(AU)
24 and he is gracious to that person and says to God,
    ‘Spare them from going down to the pit;(AV)
    I have found a ransom for them(AW)
25 let their flesh be renewed(AX) like a child’s;
    let them be restored as in the days of their youth’(AY)
26 then that person can pray to God and find favor with him,(AZ)
    they will see God’s face and shout for joy;(BA)
    he will restore them to full well-being.(BB)
27 And they will go to others and say,
    ‘I have sinned,(BC) I have perverted what is right,(BD)
    but I did not get what I deserved.(BE)
28 God has delivered(BF) me from going down to the pit,(BG)
    and I shall live to enjoy the light of life.’(BH)

29 “God does all these things to a person(BI)
    twice, even three times(BJ)
30 to turn them back(BK) from the pit,(BL)
    that the light of life(BM) may shine on them.(BN)

31 “Pay attention, Job, and listen(BO) to me;(BP)
    be silent,(BQ) and I will speak.
32 If you have anything to say, answer me;(BR)
    speak up, for I want to vindicate you.(BS)
33 But if not, then listen to me;(BT)
    be silent,(BU) and I will teach you wisdom.(BV)

Footnotes

  1. Job 33:13 Or that he does not answer for any of his actions
  2. Job 33:18 Or from crossing the river
  3. Job 33:22 Or to the place of the dead