Add parallel Print Page Options

31 “Ndinachita pangano ndi maso anga
    kuti sindidzapenya namwali momusirira.
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani?
    Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa,
    tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Kodi Mulungu saona zochita zanga,
    ndi kudziwa mayendedwe anga?

“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso,
    kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama
    ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
ngati mayendedwe anga asempha njira,
    ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona,
    kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala,
    ndipo zomera zanga zizulidwe.

“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi,
    ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya,
    ndipo amuna ena azigona naye.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi,
    tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko;
    ukanapsereza zokolola zanga.

13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi,
    pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa?
    Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo?
    Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?

16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba,
    kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha,
    wosagawirako mwana wamasiye,
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake,
    ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa,
    kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo
    chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye,
    poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke,
    mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu,
    ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.

24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma
    kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri,
    zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala,
    kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo
    nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo,
    chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.

29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga,
    kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga
    potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti,
    ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse,
    pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena,
    kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 chifukwa choopa gulu la anthu,
    ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko
    kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.

35 “Aa, pakanakhala wina wondimva!
    Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe;
    mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa,
    ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita;
    ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.

38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine
    ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama
    kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu
    ndi udzu mʼmalo mwa barele.”

Mawu a Yobu athera pano.

31 “I made a covenant with my eyes(A)
    not to look lustfully at a young woman.(B)
For what is our lot(C) from God above,
    our heritage from the Almighty on high?(D)
Is it not ruin(E) for the wicked,
    disaster(F) for those who do wrong?(G)
Does he not see my ways(H)
    and count my every step?(I)

“If I have walked with falsehood
    or my foot has hurried after deceit(J)
let God weigh me(K) in honest scales(L)
    and he will know that I am blameless(M)
if my steps have turned from the path,(N)
    if my heart has been led by my eyes,
    or if my hands(O) have been defiled,(P)
then may others eat what I have sown,(Q)
    and may my crops be uprooted.(R)

“If my heart has been enticed(S) by a woman,(T)
    or if I have lurked at my neighbor’s door,
10 then may my wife grind(U) another man’s grain,
    and may other men sleep with her.(V)
11 For that would have been wicked,(W)
    a sin to be judged.(X)
12 It is a fire(Y) that burns to Destruction[a];(Z)
    it would have uprooted my harvest.(AA)

13 “If I have denied justice to any of my servants,(AB)
    whether male or female,
    when they had a grievance against me,(AC)
14 what will I do when God confronts me?(AD)
    What will I answer when called to account?(AE)
15 Did not he who made me in the womb make them?(AF)
    Did not the same one form us both within our mothers?(AG)

16 “If I have denied the desires of the poor(AH)
    or let the eyes of the widow(AI) grow weary,(AJ)
17 if I have kept my bread to myself,
    not sharing it with the fatherless(AK)
18 but from my youth I reared them as a father would,
    and from my birth I guided the widow(AL)
19 if I have seen anyone perishing for lack of clothing,(AM)
    or the needy(AN) without garments,
20 and their hearts did not bless me(AO)
    for warming them with the fleece(AP) from my sheep,
21 if I have raised my hand against the fatherless,(AQ)
    knowing that I had influence in court,(AR)
22 then let my arm fall from the shoulder,
    let it be broken off at the joint.(AS)
23 For I dreaded destruction from God,(AT)
    and for fear of his splendor(AU) I could not do such things.(AV)

24 “If I have put my trust in gold(AW)
    or said to pure gold, ‘You are my security,’(AX)
25 if I have rejoiced over my great wealth,(AY)
    the fortune my hands had gained,(AZ)
26 if I have regarded the sun(BA) in its radiance
    or the moon(BB) moving in splendor,
27 so that my heart was secretly enticed(BC)
    and my hand offered them a kiss of homage,(BD)
28 then these also would be sins to be judged,(BE)
    for I would have been unfaithful to God on high.(BF)

29 “If I have rejoiced at my enemy’s misfortune(BG)
    or gloated over the trouble that came to him(BH)
30 I have not allowed my mouth to sin
    by invoking a curse against their life(BI)
31 if those of my household have never said,
    ‘Who has not been filled with Job’s meat?’(BJ)
32 but no stranger had to spend the night in the street,
    for my door was always open to the traveler(BK)
33 if I have concealed(BL) my sin as people do,[b]
    by hiding(BM) my guilt in my heart
34 because I so feared the crowd(BN)
    and so dreaded the contempt of the clans
    that I kept silent(BO) and would not go outside—

35 (“Oh, that I had someone to hear me!(BP)
    I sign now my defense—let the Almighty answer me;
    let my accuser(BQ) put his indictment in writing.
36 Surely I would wear it on my shoulder,(BR)
    I would put it on like a crown.(BS)
37 I would give him an account of my every step;(BT)
    I would present it to him as to a ruler.(BU))—

38 “if my land cries out against me(BV)
    and all its furrows are wet(BW) with tears,
39 if I have devoured its yield without payment(BX)
    or broken the spirit of its tenants,(BY)
40 then let briers(BZ) come up instead of wheat
    and stinkweed(CA) instead of barley.”

The words of Job are ended.(CB)

Footnotes

  1. Job 31:12 Hebrew Abaddon
  2. Job 31:33 Or as Adam did