Add parallel Print Page Options

Mawu a Yobu

16 Pamenepo Yobu anayankha kuti,

“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi;
    nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha?
    Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu,
    inuyo mukanakhala monga ndilili inemu;
Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu
    ndi kukupukusirani mutu wanga.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani;
    chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.

“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa;
    ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu;
    mwawononga banja langa lonse.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni;
    kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane,
    amachita kulumira mano;
    mdani wanga amandituzulira maso.
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza;
    amandimenya pa tsaya mwachipongwe
    ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa
    ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya;
    anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya.
Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13     anthu ake oponya mauta andizungulira.
Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga
    ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 Akundivulaza kawirikawiri,
    akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.

15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa
    ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 Maso anga afiira ndi kulira,
    ndipo zikope zanga zatupa;
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa
    ndipo pemphero langa ndi lolungama.

18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga;
    kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba;
    wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa,
    pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu
    monga munthu amadandaulira bwenzi lake.

22 “Pakuti sipapita zaka zambiri
    ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

Job

16 Then Job replied:

“I have heard many things like these;
    you are miserable comforters,(A) all of you!(B)
Will your long-winded speeches never end?(C)
    What ails you that you keep on arguing?(D)
I also could speak like you,
    if you were in my place;
I could make fine speeches against you
    and shake my head(E) at you.
But my mouth would encourage you;
    comfort(F) from my lips would bring you relief.(G)

“Yet if I speak, my pain is not relieved;
    and if I refrain, it does not go away.(H)
Surely, God, you have worn me out;(I)
    you have devastated my entire household.(J)
You have shriveled me up—and it has become a witness;
    my gauntness(K) rises up and testifies against me.(L)
God assails me and tears(M) me in his anger(N)
    and gnashes his teeth at me;(O)
    my opponent fastens on me his piercing eyes.(P)
10 People open their mouths(Q) to jeer at me;(R)
    they strike my cheek(S) in scorn
    and unite together against me.(T)
11 God has turned me over to the ungodly
    and thrown me into the clutches of the wicked.(U)
12 All was well with me, but he shattered me;
    he seized me by the neck and crushed me.(V)
He has made me his target;(W)
13     his archers surround me.(X)
Without pity, he pierces(Y) my kidneys
    and spills my gall on the ground.
14 Again and again(Z) he bursts upon me;
    he rushes at me like a warrior.(AA)

15 “I have sewed sackcloth(AB) over my skin
    and buried my brow in the dust.(AC)
16 My face is red with weeping,(AD)
    dark shadows ring my eyes;(AE)
17 yet my hands have been free of violence(AF)
    and my prayer is pure.(AG)

18 “Earth, do not cover my blood;(AH)
    may my cry(AI) never be laid to rest!(AJ)
19 Even now my witness(AK) is in heaven;(AL)
    my advocate is on high.(AM)
20 My intercessor(AN) is my friend[a](AO)
    as my eyes pour out(AP) tears(AQ) to God;
21 on behalf of a man he pleads(AR) with God
    as one pleads for a friend.

22 “Only a few years will pass
    before I take the path of no return.(AS)

Footnotes

  1. Job 16:20 Or My friends treat me with scorn