Yesaya 66
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Chiweruzo ndi Chiyembekezo
66 Yehova akuti,
“Kumwamba ndi mpando wanga waufumu
ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.
Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,
ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,
motero zonsezi ndi zanga?”
Akutero Yehova.
“Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:
amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,
ndipo amamvera mawu anga.
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna
amaphanso munthu,
ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa,
amaphanso galu.
Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya
amaperekanso magazi a nkhumba.
Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso
amapembedzanso fano.
Popeza iwo asankha njira zawozawo,
ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa
ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija.
Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha,
pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu.
Anachita zoyipa pamaso panga
ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 Imvani mawu a Yehova,
inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake:
“Abale anu amene amakudani,
ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti,
‘Yehova alemekezeke
kuti ife tione chimwemwe chanu!’
Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 Imvani mfuwu mu mzinda,
imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu!
Limenelo ndi liwu la Yehova,
kulanga adani ake onse.
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa
wachira kale;
asanayambe kumva ululu,
wabala kale mwana wamwamuna.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi?
Ndani anazionapo zinthu zoterezi?
Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi,
kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi?
Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa
nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira,
koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova.
“Kodi ndingatseke mimba
pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye,
inu nonse amene mumakonda Yerusalemu,
kondwera nayeni kwambiri,
nonse amene mumamulira.
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake
ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri
wa mʼmawere
a chitonthozo chake.”
12 Yehova akuti,
“Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi,
ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira.
Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa,
kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo,
moteronso Ine ndidzakusangalatsani;
ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu.
Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu.
Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira
ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto,
ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu;
Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake
ndi malawi amoto.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse
ndi moto ndi lupanga,
Yehova adzapha anthu ambiri.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina. 20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo. 21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova. 23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova. 24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
Isaiah 66
New International Version
Judgment and Hope
66 This is what the Lord says:
“Heaven is my throne,(A)
and the earth is my footstool.(B)
Where is the house(C) you will build for me?
Where will my resting place be?
2 Has not my hand made all these things,(D)
and so they came into being?”
declares the Lord.
“These are the ones I look on with favor:
those who are humble and contrite in spirit,(E)
and who tremble at my word.(F)
3 But whoever sacrifices a bull(G)
is like one who kills a person,
and whoever offers a lamb
is like one who breaks a dog’s neck;
whoever makes a grain offering
is like one who presents pig’s(H) blood,
and whoever burns memorial incense(I)
is like one who worships an idol.
They have chosen their own ways,(J)
and they delight in their abominations;(K)
4 so I also will choose harsh treatment for them
and will bring on them what they dread.(L)
For when I called, no one answered,(M)
when I spoke, no one listened.
They did evil(N) in my sight
and chose what displeases me.”(O)
5 Hear the word of the Lord,
you who tremble at his word:(P)
“Your own people who hate(Q) you,
and exclude you because of my name, have said,
‘Let the Lord be glorified,
that we may see your joy!’
Yet they will be put to shame.(R)
6 Hear that uproar from the city,
hear that noise from the temple!
It is the sound(S) of the Lord
repaying(T) his enemies all they deserve.
7 “Before she goes into labor,(U)
she gives birth;
before the pains come upon her,
she delivers a son.(V)
8 Who has ever heard of such things?
Who has ever seen(W) things like this?
Can a country be born in a day(X)
or a nation be brought forth in a moment?
Yet no sooner is Zion in labor
than she gives birth to her children.(Y)
9 Do I bring to the moment of birth(Z)
and not give delivery?” says the Lord.
“Do I close up the womb
when I bring to delivery?” says your God.
10 “Rejoice(AA) with Jerusalem and be glad for her,
all you who love(AB) her;
rejoice greatly with her,
all you who mourn(AC) over her.
11 For you will nurse(AD) and be satisfied
at her comforting breasts;(AE)
you will drink deeply
and delight in her overflowing abundance.”(AF)
12 For this is what the Lord says:
“I will extend peace(AG) to her like a river,(AH)
and the wealth(AI) of nations like a flooding stream;
you will nurse and be carried(AJ) on her arm
and dandled on her knees.
13 As a mother comforts her child,(AK)
so will I comfort(AL) you;
and you will be comforted over Jerusalem.”
14 When you see this, your heart will rejoice(AM)
and you will flourish(AN) like grass;
the hand(AO) of the Lord will be made known to his servants,(AP)
but his fury(AQ) will be shown to his foes.
15 See, the Lord is coming with fire,(AR)
and his chariots(AS) are like a whirlwind;(AT)
he will bring down his anger with fury,
and his rebuke(AU) with flames of fire.
16 For with fire(AV) and with his sword(AW)
the Lord will execute judgment(AX) on all people,
and many will be those slain(AY) by the Lord.
17 “Those who consecrate and purify themselves to go into the gardens,(AZ) following one who is among those who eat the flesh of pigs,(BA) rats(BB) and other unclean things—they will meet their end(BC) together with the one they follow,” declares the Lord.
18 “And I, because of what they have planned and done,(BD) am about to come[a] and gather the people of all nations(BE) and languages, and they will come and see my glory.(BF)
19 “I will set a sign(BG) among them, and I will send some of those who survive(BH) to the nations—to Tarshish,(BI) to the Libyans[b] and Lydians(BJ) (famous as archers), to Tubal(BK) and Greece,(BL) and to the distant islands(BM) that have not heard of my fame or seen my glory.(BN) They will proclaim my glory among the nations. 20 And they will bring(BO) all your people, from all the nations, to my holy mountain(BP) in Jerusalem as an offering to the Lord—on horses, in chariots and wagons, and on mules and camels,”(BQ) says the Lord. “They will bring them, as the Israelites bring their grain offerings, to the temple of the Lord in ceremonially clean vessels.(BR) 21 And I will select some of them also to be priests(BS) and Levites,” says the Lord.
22 “As the new heavens and the new earth(BT) that I make will endure before me,” declares the Lord, “so will your name and descendants endure.(BU) 23 From one New Moon to another and from one Sabbath(BV) to another, all mankind will come and bow down(BW) before me,” says the Lord. 24 “And they will go out and look on the dead bodies(BX) of those who rebelled(BY) against me; the worms(BZ) that eat them will not die, the fire that burns them will not be quenched,(CA) and they will be loathsome to all mankind.”
Footnotes
- Isaiah 66:18 The meaning of the Hebrew for this clause is uncertain.
- Isaiah 66:19 Some Septuagint manuscripts Put (Libyans); Hebrew Pul
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.