Add parallel Print Page Options

Chipulumutso kwa Anthu Ena Onse

56 Yehova akuti,

“Chitani chilungamo
    ndi zinthu zabwino,
chifukwa chipulumutso changa chili pafupi
    ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi,
    munthu amene amalimbika kuzichita,
amene amasunga Sabata osaliyipitsa,
    ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”

Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti,
    “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.”
Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti,
    “Ine ndine mtengo wowuma basi.”

Popeza Yehova akuti,

“Wofulidwa amene amasunga masabata anga,
    nachita zokomera Ine
    ndi kusunga pangano langa,
ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino
    mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake,
    kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi.
Ndidzawapatsa dzina labwino,
    losatha ndi losayiwalika.”
Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova,
    motero kuti amamutumikira Iye,
amakonda dzina la Yehova,
    amamugwirira ntchito,
komanso kusunga Sabata osaliyipitsa
    ndi kusunga bwino pangano langa,
amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika,
    ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero.
Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo
    ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe.
Paja nyumba yanga idzatchedwa
    nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa
    Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti,
“Ndidzasonkhanitsano anthu ena
    kuwonjezera amene anasonkhana kale.”

Mulungu Adzazula Anthu Oyipa

Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo,
    inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
10 Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu,
    onse ndi opanda nzeru;
onse ndi agalu opanda mawu,
    samatha kuwuwa:
amagona pansi nʼkumalota
    amakonda kugona tulo.
11 Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu;
    sakhuta konse.
Abusa nawonso samvetsa zinthu;
    onse amachita monga akufunira,
    aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
12 Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo!
    Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta!
Mawa lidzakhala ngati leroli,
    kapena kuposa lero lino.”

Salvation for Foreigners

56 Thus says the Lord:
“Keep justice, and do righteousness,
(A)for soon my salvation will come,
    and my righteousness be revealed.
Blessed is the man who does this,
    and the son of man who holds it fast,
(B)who keeps the Sabbath, not profaning it,
    and keeps his hand from doing any evil.”

Let not (C)the foreigner who has joined himself to the Lord say,
    “The Lord will surely separate me from his people”;
and let not the eunuch say,
    “Behold, I am (D)a dry tree.”
For thus says the Lord:
“To the eunuchs (E)who keep my Sabbaths,
    who choose the things that please me
    and hold fast my covenant,
(F)I will give in my house and within my walls
    a (G)monument and a name
    better than sons and daughters;
(H)I will give them an everlasting name
    that shall not be cut off.

“And (I)the foreigners who join themselves to the Lord,
    to minister to him, to love the name of the Lord,
    and to be his servants,
everyone (J)who keeps the Sabbath and does not profane it,
    and holds fast my covenant—
(K)these I will bring to (L)my holy mountain,
    and make them joyful in my house of prayer;
(M)their burnt offerings and their sacrifices
    will be accepted on my altar;
for (N)my house shall be called a house of prayer
    for all peoples.”
The Lord God,
    (O)who gathers the outcasts of Israel, declares,
(P)“I will gather yet others to him
    besides those already gathered.”

Israel's Irresponsible Leaders

(Q)All you beasts of the field, come to devour—
    all you beasts in the forest.
10 (R)His watchmen are blind;
    they are all without knowledge;
they are all silent (S)dogs;
    they cannot bark,
dreaming, lying down,
    loving to slumber.
11 (T)The dogs have a mighty appetite;
    they never have enough.
But (U)they are shepherds who have no understanding;
    they have all turned to their own way,
    (V)each to his own gain, one and all.
12 (W)“Come,” they say, “let me get wine;
    let us fill ourselves with strong drink;
(X)and tomorrow will be like this day,
    great beyond measure.”