Add parallel Print Page Options

Kugwa kwa Babuloni

47 “Tsika, ndi kukhala pa fumbi,
    iwe namwali, Babuloni;
khala pansi wopanda mpando waufumu,
    iwe namwali, Kaldeya
pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera
    kumugwira mosamala.
Tenga mphero ndipo upere ufa;
    chotsa nsalu yako yophimba nkhope
kwinya chovala chako mpaka ntchafu
    ndipo woloka mitsinje.
Maliseche ako adzakhala poyera
    ndipo udzachita manyazi.
Ndidzabwezera chilango
    ndipo palibe amene adzandiletse.”

Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu,
    dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

“Khala chete, ndipo lowa mu mdima,
    iwe namwali, Kaldeya;
chifukwa sadzakutchulanso
    mfumukazi ya maufumu.
Ndinawakwiyira anthu anga,
    osawasamalanso.
Ndinawapereka manja mwako,
    ndipo iwe sunawachitire chifundo.
Iwe unachitira nkhanza
    ngakhale nkhalamba.
Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse
    ngati mfumukazi.’
Koma sunaganizire zinthu izi
    kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.

“Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe,
    amene ukukhala mosatekesekawe,
umaganiza mu mtima mwako kuti,
    ‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina.
Sindidzakhala konse mkazi wamasiye,
    ndipo ana anga sadzamwalira.’
Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi,
    zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira:
    ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye.
Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu
    ngakhale ali ndi amatsenga ambiri
    ndi mawula amphamvu.
10 Iwe unkadalira kuyipa kwako
    ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’
Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza,
    choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti,
    ‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’
11 Ngozi yayikulu idzakugwera
    ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako.
Mavuto adzakugwera
    ndipo sudzatha kuwachotsa;
chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa
    chidzakugwera mwadzidzidzi.

12 “Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako,
    pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo,
    wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako.
Mwina udzatha kupambana
    kapena kuopsezera nazo adani ako.
13 Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi!
    Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni.
Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi
    zimene ziti zidzakuchitikire.
14 Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi;
    adzapsa ndi moto.
Sangathe kudzipulumutsa okha
    ku mphamvu ya malawi a moto.
Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha;
    kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
15 Umu ndi mmene adzachitire amatsenga,
    anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito
    ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako.
Onse adzamwazika ndi mantha,
    sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”

47 Come down, and sit in the dust, O virgin daughter of Babylon, sit on the ground: there is no throne, O daughter of the Chaldeans: for thou shalt no more be called tender and delicate.

Take the millstones, and grind meal: uncover thy locks, make bare the leg, uncover the thigh, pass over the rivers.

Thy nakedness shall be uncovered, yea, thy shame shall be seen: I will take vengeance, and I will not meet thee as a man.

As for our redeemer, the Lord of hosts is his name, the Holy One of Israel.

Sit thou silent, and get thee into darkness, O daughter of the Chaldeans: for thou shalt no more be called, The lady of kingdoms.

I was wroth with my people, I have polluted mine inheritance, and given them into thine hand: thou didst shew them no mercy; upon the ancient hast thou very heavily laid thy yoke.

And thou saidst, I shall be a lady for ever: so that thou didst not lay these things to thy heart, neither didst remember the latter end of it.

Therefore hear now this, thou that art given to pleasures, that dwellest carelessly, that sayest in thine heart, I am, and none else beside me; I shall not sit as a widow, neither shall I know the loss of children:

But these two things shall come to thee in a moment in one day, the loss of children, and widowhood: they shall come upon thee in their perfection for the multitude of thy sorceries, and for the great abundance of thine enchantments.

10 For thou hast trusted in thy wickedness: thou hast said, None seeth me. Thy wisdom and thy knowledge, it hath perverted thee; and thou hast said in thine heart, I am, and none else beside me.

11 Therefore shall evil come upon thee; thou shalt not know from whence it riseth: and mischief shall fall upon thee; thou shalt not be able to put it off: and desolation shall come upon thee suddenly, which thou shalt not know.

12 Stand now with thine enchantments, and with the multitude of thy sorceries, wherein thou hast laboured from thy youth; if so be thou shalt be able to profit, if so be thou mayest prevail.

13 Thou art wearied in the multitude of thy counsels. Let now the astrologers, the stargazers, the monthly prognosticators, stand up, and save thee from these things that shall come upon thee.

14 Behold, they shall be as stubble; the fire shall burn them; they shall not deliver themselves from the power of the flame: there shall not be a coal to warm at, nor fire to sit before it.

15 Thus shall they be unto thee with whom thou hast laboured, even thy merchants, from thy youth: they shall wander every one to his quarter; none shall save thee.