Yesaya 10
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
10 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo,
kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
2 kuwalanda anthu osauka ufulu wawo
ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga,
amalanda zinthu za akazi amasiye
ndi kubera ana amasiye.
3 Kodi mudzatani pa tsiku la chilango,
pofika chiwonongeko chochokera kutali?
Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni?
Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
4 Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa
kapena kufa pamodzi ndi ophedwa.
Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere,
mkono wake uli chitambasulire.
Chiweruzo cha Mulungu pa Asiriya
5 “Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga,
iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
6 Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu,
ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine,
kukafunkha ndi kulanda chuma,
ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
7 Koma izi si zimene akufuna kukachita,
izi si zimene zili mʼmaganizo mwake;
cholinga chake ndi kukawononga,
kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
8 Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
9 ‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi?
Kodi Hamati sali ngati Aripadi,
nanga Samariya sali ngati Damasiko?
10 Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano,
mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
11 nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake
monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’ ”
12 Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake. 13 Pakuti mfumuyo ikuti,
“ ‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa,
ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu.
Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu,
ndinafunkha chuma chawo;
ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
14 Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu
ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame,
ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa,
motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse;
palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake,
kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’ ”
15 Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito,
kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito?
Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula,
kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
16 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse
adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu;
kunyada kwa mfumuyo kudzapsa
ndi moto wosazima.
17 Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto,
Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto.
Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza
ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
18 Ankhondo ake adzawonongedwa
ngati nkhalango yayikulu
ndi ngati nthaka yachonde.
19 Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri,
yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.
Aisraeli Otsala
20 Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli,
opulumuka a nyumba ya Yakobo,
sadzadaliranso anthu
amene anawakantha,
koma adzadalira Yehova,
Woyerayo wa Israeli.
21 Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo
adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
22 Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja,
otsala okha ndiwo adzabwerere.
Chiwonongeko chalamulidwa,
chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
23 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse
monga momwe analamulira.
24 Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti,
“Inu anthu anga okhala mu Ziyoni,
musawaope Asiriya,
amene amakukanthani ndi ndodo
nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
25 Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu
ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”
26 Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu,
monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu;
ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi
ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
27 Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu,
goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu;
golilo lidzathyoka
chifukwa cha kunenepa kwambiri.
28 Adani alowa mu Ayati
apyola ku Migironi;
asunga katundu wawo ku Mikimasi.
29 Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti,
“Tikagona ku Geba”
Rama akunjenjemera;
Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
30 Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu!
Tchera khutu, iwe Laisa!
Iwe Anatoti wosauka!
31 Anthu a ku Madimena akuthawa;
anthu a ku Gebimu bisalani.
32 Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu;
adzagwedeza mikono yawo,
kuopseza anthu a ku Ziyoni,
pa phiri la Yerusalemu.
33 Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,
adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo,
mitengo yodzikweza idzadulidwa,
mitengo yayitali idzagwetsedwa.
34 Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira;
Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.
以赛亚书 10
Chinese Contemporary Bible (Simplified)
10 制定不义律例、起草不公法令的人啊,
你们有祸了!
2 你们冤枉穷人,
夺去我子民中困苦者的权利,
掳掠寡妇,抢劫孤儿。
3 在惩罚的日子,
当灾祸从远方临到你们头上时,
你们怎么办?
你们能跑到谁那里去求救呢?
你们能把财物藏在哪里呢?
4 你们将不是被掳就是被杀。
虽然如此,耶和华的怒气还没有止息,
祂降罚的手没有收回。
主要审判亚述
5 耶和华说:“亚述王有祸了!
他是我的愤怒之棍,
他手中拿着我发烈怒的杖。
6 我要差遣他去攻打一个不虔敬的国家,
一个惹我发怒的民族,
去抢夺、掳掠他们的财物,
像践踏街上的泥土一样践踏他们。
7 可是他却不这样想,
心里也不这样盘算,
他只想毁灭许多国家。
8 他说,‘我的臣仆都要做藩王!
9 迦勒挪岂不是和迦基米施一样吗?
哈马岂不是和亚珥拔一样吗?
撒玛利亚岂不是和大马士革一样吗?
它们不是都被我征服了吗?
10 这些国家都在我的手中,
他们雕刻的偶像不胜过耶路撒冷和撒玛利亚的偶像吗?
11 我怎样毁灭撒玛利亚和它的偶像,
也必怎样毁灭耶路撒冷和它的偶像。’”
12 主完成在锡安山和耶路撒冷要做的事后,必惩罚心里狂妄、眼目高傲的亚述王。
13 因为亚述王说:
“我靠自己的力量和智慧成就了此事,
因为我很聪明。
我废除列国的疆界,
掳掠他们的财物,
像勇士一样征服他们的君王。
14 我夺取列国的财物,
好像探囊取物;
我征服天下,
不过是手到擒来;
无人反抗,无人吭声。”
15 然而,斧头怎能向舞动它的人自夸呢?
锯子怎能向用锯的人炫耀呢?
难道棍子可以挥动举它的人吗?
手杖可以举起它的主人吗?
16 因此,主——万军之耶和华必使亚述王强健的士兵疾病缠身,
使火焰吞噬他的荣耀。
17 以色列的光必成为火焰,
他们的圣者必成为烈火,
一日之间烧光亚述王的荆棘和蒺藜。
18 他茂盛的树林和肥美的田园必被彻底摧毁,
犹如病人渐渐消亡。
19 林中剩下的树木稀少,
连小孩子也能数清。
以色列的余民
20 到那日,以色列的余民,就是雅各家的幸存者,将不再倚靠欺压他们的亚述,他们将真心倚靠耶和华——以色列的圣者, 21 重新归向全能的上帝。 22 以色列啊,你的人民虽多如海沙,将只有剩余的人归回。充满公义的毁灭之事已定。 23 因为主——万军之耶和华必按所定的在整个大地上施行毁灭。
24 因此,主——万军之耶和华说:“我锡安的子民啊,虽然亚述人像埃及人一样挥舞着棍棒毒打你们,你们不要惧怕。 25 因为很快我就不再向你们发怒,我要向他们发怒,毁灭他们。” 26 万军之耶和华要鞭打他们,就像在俄立磐石击杀米甸人,就像祂向海伸杖,使海水淹没埃及人。 27 到那日,祂必除去亚述人加在你们肩头的重担和颈上的轭;那轭必因你们肥壮而折断。
28 亚述大军攻占了亚叶,
穿过米矶仑,
把辎重存放在密抹。
29 他们过了关口,
在迦巴宿营。
拉玛人战战兢兢,
扫罗的乡亲基比亚人仓皇逃跑。
30 迦琳人啊,高声喊叫吧!
莱煞人啊,可怜的亚拿突人啊,
留心听吧!
31 玛得米纳人逃跑,
基柄人躲藏。
32 那时,亚述王必屯兵挪伯,
向着锡安城[a]的山岭,
向着耶路撒冷的山丘摩拳擦掌。
33 看啊,主——万军之耶和华要以大能削去树枝。
高大的树必被斩断,
挺拔的大树必被砍倒,
34 茂密的树林必被铁斧砍掉,
连黎巴嫩的大树也要倒在全能的上帝面前。
Isaiah 10
King James Version
10 Woe unto them that decree unrighteous decrees, and that write grievousness which they have prescribed;
2 To turn aside the needy from judgment, and to take away the right from the poor of my people, that widows may be their prey, and that they may rob the fatherless!
3 And what will ye do in the day of visitation, and in the desolation which shall come from far? to whom will ye flee for help? and where will ye leave your glory?
4 Without me they shall bow down under the prisoners, and they shall fall under the slain. For all this his anger is not turned away, but his hand is stretched out still.
5 O Assyrian, the rod of mine anger, and the staff in their hand is mine indignation.
6 I will send him against an hypocritical nation, and against the people of my wrath will I give him a charge, to take the spoil, and to take the prey, and to tread them down like the mire of the streets.
7 Howbeit he meaneth not so, neither doth his heart think so; but it is in his heart to destroy and cut off nations not a few.
8 For he saith, Are not my princes altogether kings?
9 Is not Calno as Carchemish? is not Hamath as Arpad? is not Samaria as Damascus?
10 As my hand hath found the kingdoms of the idols, and whose graven images did excel them of Jerusalem and of Samaria;
11 Shall I not, as I have done unto Samaria and her idols, so do to Jerusalem and her idols?
12 Wherefore it shall come to pass, that when the Lord hath performed his whole work upon mount Zion and on Jerusalem, I will punish the fruit of the stout heart of the king of Assyria, and the glory of his high looks.
13 For he saith, By the strength of my hand I have done it, and by my wisdom; for I am prudent: and I have removed the bounds of the people, and have robbed their treasures, and I have put down the inhabitants like a valiant man:
14 And my hand hath found as a nest the riches of the people: and as one gathereth eggs that are left, have I gathered all the earth; and there was none that moved the wing, or opened the mouth, or peeped.
15 Shall the axe boast itself against him that heweth therewith? or shall the saw magnify itself against him that shaketh it? as if the rod should shake itself against them that lift it up, or as if the staff should lift up itself, as if it were no wood.
16 Therefore shall the Lord, the Lord of hosts, send among his fat ones leanness; and under his glory he shall kindle a burning like the burning of a fire.
17 And the light of Israel shall be for a fire, and his Holy One for a flame: and it shall burn and devour his thorns and his briers in one day;
18 And shall consume the glory of his forest, and of his fruitful field, both soul and body: and they shall be as when a standard-bearer fainteth.
19 And the rest of the trees of his forest shall be few, that a child may write them.
20 And it shall come to pass in that day, that the remnant of Israel, and such as are escaped of the house of Jacob, shall no more again stay upon him that smote them; but shall stay upon the Lord, the Holy One of Israel, in truth.
21 The remnant shall return, even the remnant of Jacob, unto the mighty God.
22 For though thy people Israel be as the sand of the sea, yet a remnant of them shall return: the consumption decreed shall overflow with righteousness.
23 For the Lord God of hosts shall make a consumption, even determined, in the midst of all the land.
24 Therefore thus saith the Lord God of hosts, O my people that dwellest in Zion, be not afraid of the Assyrian: he shall smite thee with a rod, and shall lift up his staff against thee, after the manner of Egypt.
25 For yet a very little while, and the indignation shall cease, and mine anger in their destruction.
26 And the Lord of hosts shall stir up a scourge for him according to the slaughter of Midian at the rock of Oreb: and as his rod was upon the sea, so shall he lift it up after the manner of Egypt.
27 And it shall come to pass in that day, that his burden shall be taken away from off thy shoulder, and his yoke from off thy neck, and the yoke shall be destroyed because of the anointing.
28 He is come to Aiath, he is passed to Migron; at Michmash he hath laid up his carriages:
29 They are gone over the passage: they have taken up their lodging at Geba; Ramah is afraid; Gibeah of Saul is fled.
30 Lift up thy voice, O daughter of Gallim: cause it to be heard unto Laish, O poor Anathoth.
31 Madmenah is removed; the inhabitants of Gebim gather themselves to flee.
32 As yet shall he remain at Nob that day: he shall shake his hand against the mount of the daughter of Zion, the hill of Jerusalem.
33 Behold, the Lord, the Lord of hosts, shall lop the bough with terror: and the high ones of stature shall be hewn down, and the haughty shall be humbled.
34 And he shall cut down the thickets of the forest with iron, and Lebanon shall fall by a mighty one.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Chinese Contemporary Bible Copyright © 1979, 2005, 2007, 2011 by Biblica® Used by permission. All rights reserved worldwide.