Add parallel Print Page Options

Uthenga Wabwino wa Yehova

61 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine,
    chifukwa Yehova wandidzoza
    kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka.
Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima,
    ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu
    ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake;
    za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake.
Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
    Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni,
nkhata ya maluwa yokongola
    mʼmalo mwa phulusa,
ndiwapatse mafuta achikondwerero
    mʼmalo mwa kulira.
Ndiwapatse chovala cha matamando
    mʼmalo mwa mtima wopsinjika.
Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo,
    yoyidzala Yehova
    kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.

Adzamanganso mabwinja akale a mzinda
    ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso.
Adzakonzanso mizinda imene inapasuka,
    imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu;
    iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova,
    adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu.
Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu,
    ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.

Chifukwa manyazi awo anali owirikiza;
    ndi kuti munalandira
chitonzo ndi kutukwana,
    adzakondwera ndi cholowa chawo,
tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza,
    ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.

“Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo;
    ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa.
Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika
    ndikupangana nawo pangano losatha.
Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu
    ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina.
Aliyense wowaona adzazindikira
    kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”

10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova;
    moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga.
Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso,
    ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo.
Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake,
    ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu
    ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala,
momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando
    pamaso pa mitundu yonse ya anthu.

The Year of the Lord’s Favor

61 The Spirit(A) of the Sovereign Lord(B) is on me,
    because the Lord has anointed(C) me
    to proclaim good news(D) to the poor.(E)
He has sent me to bind up(F) the brokenhearted,
    to proclaim freedom(G) for the captives(H)
    and release from darkness for the prisoners,[a]
to proclaim the year of the Lord’s favor(I)
    and the day of vengeance(J) of our God,
to comfort(K) all who mourn,(L)
    and provide for those who grieve in Zion—
to bestow on them a crown(M) of beauty
    instead of ashes,(N)
the oil(O) of joy
    instead of mourning,(P)
and a garment of praise
    instead of a spirit of despair.
They will be called oaks of righteousness,
    a planting(Q) of the Lord
    for the display of his splendor.(R)

They will rebuild the ancient ruins(S)
    and restore the places long devastated;
they will renew the ruined cities
    that have been devastated for generations.
Strangers(T) will shepherd your flocks;
    foreigners will work your fields and vineyards.
And you will be called priests(U) of the Lord,
    you will be named ministers of our God.
You will feed on the wealth(V) of nations,
    and in their riches you will boast.

Instead of your shame(W)
    you will receive a double(X) portion,
and instead of disgrace
    you will rejoice in your inheritance.
And so you will inherit(Y) a double portion in your land,
    and everlasting joy(Z) will be yours.

“For I, the Lord, love justice;(AA)
    I hate robbery and wrongdoing.
In my faithfulness I will reward my people
    and make an everlasting covenant(AB) with them.
Their descendants(AC) will be known among the nations
    and their offspring among the peoples.
All who see them will acknowledge
    that they are a people the Lord has blessed.”(AD)

10 I delight greatly in the Lord;
    my soul rejoices(AE) in my God.
For he has clothed me with garments of salvation
    and arrayed me in a robe of his righteousness,(AF)
as a bridegroom adorns his head(AG) like a priest,
    and as a bride(AH) adorns herself with her jewels.
11 For as the soil makes the sprout come up
    and a garden(AI) causes seeds to grow,
so the Sovereign Lord will make righteousness(AJ)
    and praise spring up before all nations.

Footnotes

  1. Isaiah 61:1 Hebrew; Septuagint the blind